Mitu

  1. 1
  2. 2
  3. 3
  4. 4
  5. 5
  6. 6
  7. 7
  8. 8
  9. 9
  10. 10
  11. 11
  12. 12
  13. 13
  14. 14
  15. 15
  16. 16
  17. 17
  18. 18
  19. 19
  20. 20
  21. 21
  22. 22
  23. 23
  24. 24
  25. 25
  26. 26
  27. 27
  28. 28
  29. 29
  30. 30
  31. 31
  32. 32
  33. 33
  34. 34
  35. 35
  36. 36
  37. 37
  38. 38
  39. 39
  40. 40
  41. 41
  42. 42
  43. 43
  44. 44
  45. 45
  46. 46
  47. 47
  48. 48
  49. 49
  50. 50
  51. 51
  52. 52
  53. 53
  54. 54
  55. 55
  56. 56
  57. 57
  58. 58
  59. 59
  60. 60
  61. 61
  62. 62
  63. 63
  64. 64
  65. 65
  66. 66
  67. 67
  68. 68
  69. 69
  70. 70
  71. 71
  72. 72
  73. 73
  74. 74
  75. 75
  76. 76
  77. 77
  78. 78
  79. 79
  80. 80
  81. 81
  82. 82
  83. 83
  84. 84
  85. 85
  86. 86
  87. 87
  88. 88
  89. 89
  90. 90
  91. 91
  92. 92
  93. 93
  94. 94
  95. 95
  96. 96
  97. 97
  98. 98
  99. 99
  100. 100
  101. 101
  102. 102
  103. 103
  104. 104
  105. 105
  106. 106
  107. 107
  108. 108
  109. 109
  110. 110
  111. 111
  112. 112
  113. 113
  114. 114
  115. 115
  116. 116
  117. 117
  118. 118
  119. 119
  120. 120
  121. 121
  122. 122
  123. 123
  124. 124
  125. 125
  126. 126
  127. 127
  128. 128
  129. 129
  130. 130
  131. 131
  132. 132
  133. 133
  134. 134
  135. 135
  136. 136
  137. 137
  138. 138
  139. 139
  140. 140
  141. 141
  142. 142
  143. 143
  144. 144
  145. 145
  146. 146
  147. 147
  148. 148
  149. 149
  150. 150

Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 40 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

Alemekeza cipulumutso ca Mulungu, alalikira poyera cilungamo ca Mulungu

Kwa Mkulu wa Nyimbo. Salmo la Davide.

1. Kuyembekeza ndayembekeza Yehova;Ndipo anandilola, namva kupfuula kwanga.

2. Ndipo anandikweza kunditurutsa m'dzenje la citayiko, ndi m'thope la pacithaphwi;Nandipondetsa pathanthwe, nakhazika mayendedwe anga.

3. Ndipo anapatsa Nyimbo yatsopano m'kamwa mwanga, cilemekezo ca kwa Mulungu wanga;Ambiri adzaciona, nadzaopa,Ndipo adzakhulupirira Yehova.

4. Wodala munthuyo wakuyesa Yehova wokhulupirika;Wosasamala odzikuza, ndi opatukira kubodza.

5. Inu, Yehova, Mulungu wanga, zodabwiza zanu mudazicita nzambiri,Ndipo zolingirira zanu za pa ife;Palibe wina wozifotokozera Inu;Ndikazisimba ndi kuzichula, Zindicurukira kuziwerenga.

6. Nsembe ndi copereka simukondwera nazo;Mwanditsegula makutu:Nsembe yopsereza ndi yamacimo simunapempha.

7. Pamenepo ndinati, Taonani, ndadza;M'buku mwalembedwa za Ine:

8. Kucita cikondwero canu kundikonda, Mulungu wanga;Ndipo malamulo anu ali m'kati mwamtima mwanga.

9. Ndalalikira cilungamo mu msonkano waukuru;Onani, sindidzaletsa milomo yanga,Mudziwa ndinu Yehova.

10. Cilungamo canu sindinacibisa m'kati mwamtima mwanga;Cikhulupiriko canu ndi cipulumutso canu ndinacinena;Cifundo canu ndi coonadi canu sindinacibisira msonkhano waukuru.

11. Inu Yehova, simudzandikaniza nsoni zanu:Cifundo canu ndi coonadi canu zindisunge cisungire.

12. Pakuti zoipa zosawerengeka zandizinga,Zocimwa zanga zandipeza kotero kuti sindikhoza kupenya;Ziposa tsitsi la mutu wanga, ndipo wandicokera mtima.

13. Ndikupemphani, Yehova, ndilanditseni:Fulumirani kudzandithandiza, Yehova.

14. Acite manyazi nadodomeIwo akulondola moyo wanga kuti auononge:Abwerere m'mbuyo, nacite manyazi iwo okondwera kundicitira coipa.

15. Apululuke, mobwezera manyazi aoAmene anena nane, Hede, hede.

16. Asekerere nakondwerere mwa Inu onse akufuna Inu:Iwo akukonda cipulumutso canu asaleke kunena, Abuke Yehova.

17. Ndipo ine ndine wozunzika ndi waumphawi;Koma Ambuye andikumbukila ine:Inu ndinu mthandizi wanga, ndi mpulumutsi wanga:Musamacedwa, Mulungu wanga,