Mitu

  1. 1
  2. 2
  3. 3
  4. 4
  5. 5
  6. 6
  7. 7
  8. 8
  9. 9
  10. 10
  11. 11
  12. 12
  13. 13
  14. 14
  15. 15
  16. 16
  17. 17
  18. 18
  19. 19
  20. 20
  21. 21
  22. 22
  23. 23
  24. 24
  25. 25
  26. 26
  27. 27
  28. 28
  29. 29
  30. 30
  31. 31
  32. 32
  33. 33
  34. 34
  35. 35
  36. 36
  37. 37
  38. 38
  39. 39
  40. 40
  41. 41
  42. 42
  43. 43
  44. 44
  45. 45
  46. 46
  47. 47
  48. 48
  49. 49
  50. 50
  51. 51
  52. 52
  53. 53
  54. 54
  55. 55
  56. 56
  57. 57
  58. 58
  59. 59
  60. 60
  61. 61
  62. 62
  63. 63
  64. 64
  65. 65
  66. 66
  67. 67
  68. 68
  69. 69
  70. 70
  71. 71
  72. 72
  73. 73
  74. 74
  75. 75
  76. 76
  77. 77
  78. 78
  79. 79
  80. 80
  81. 81
  82. 82
  83. 83
  84. 84
  85. 85
  86. 86
  87. 87
  88. 88
  89. 89
  90. 90
  91. 91
  92. 92
  93. 93
  94. 94
  95. 95
  96. 96
  97. 97
  98. 98
  99. 99
  100. 100
  101. 101
  102. 102
  103. 103
  104. 104
  105. 105
  106. 106
  107. 107
  108. 108
  109. 109
  110. 110
  111. 111
  112. 112
  113. 113
  114. 114
  115. 115
  116. 116
  117. 117
  118. 118
  119. 119
  120. 120
  121. 121
  122. 122
  123. 123
  124. 124
  125. 125
  126. 126
  127. 127
  128. 128
  129. 129
  130. 130
  131. 131
  132. 132
  133. 133
  134. 134
  135. 135
  136. 136
  137. 137
  138. 138
  139. 139
  140. 140
  141. 141
  142. 142
  143. 143
  144. 144
  145. 145
  146. 146
  147. 147
  148. 148
  149. 149
  150. 150

Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 88 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

Wa Salmo achula masautso ace, napempha Mulungu amdalitse kuimfa

Nyimbo. Salmo la ana a Kora. Kwa Mkulu wa Nyimbo, pa Mahalata Leanotu. Cilangizo ca Hemana M-ezara.

1. Yehova, Mulungu wa cipulumutso canga,Ndinapfuula pamaso panu usana ndi usiku,

2. Pemphero langa lidze pamaso panu;Mundicherere khutu kukuwa kwanga:

3. Pakuti mzimu wanga wadzala nao mabvuto,Ndi moyo wanga wayandikira kumanda.

4. Anandiwerenga pamodzi nao otsikira kudzenje;Ndakhala ngati munthu wopanda mphamvu:

5. Wotayika pakati pa akufa,Ngati ophedwa akugona m'manda,Amene simuwakumbukilanso;Ndipo anawadula kusiyana ndi dzanja lanu.

6. Munandiika kunsi kwa dzenje,Kuti mdima, kozama.

7. Mkwiyo wanu utsamira pa ine,Ndipo munandizunza ine ndi mafunde anu onse.

8. Munandisiyanitsira wodziwana nane kutali;Munandiika ndiwakhalire conyansa:Ananditsekereza osakhoza kuturuka ine.

9. Diso langa lapuwala cifukwa ca kuzunzika kwanga:Ndimaitana Inu, Yehova, tsiku lonse;Nditambalitsira manja anga kwa Inu.

10. Kodi mudzacitira akufa zodabwiza?Kodi adzaukanso otisiyawo, ndi kukulemekezani?

11. Adzafotokozera cifundo canu kumanda kodi,Cikhulupiriko canu ku malo a cionongeko?

12. Zodabwiza zanu zidzadziwika mumdima kodi,Ndi cilungamo canu m'dziko la ciiwaliko?

13. Koma ndinapfuulira kwa Inu, Yehova,Ndipo pemphero langa likumika Inu mamawa.

14. Yehova mutayiranji moyo wanga?Ndi kundibisira nkhope yanu?

15. Wozunzika ine ndi wofuna kufa kuyambira ubwana wanga;Posenza zoopsa zanu, ndithedwa nzeru.

16. Kuzaza kwanu kwandimiza;Zoopsa zanu zinandiononga,

17. Zinandizungulira ngati madzi tsiku lonse;Zinandizinga pamodzi.

18. Munandicotsera kutali wondikonda ndi bwenzi langa,Odziwana nane akhala kumdima.