Mitu

  1. 1
  2. 2
  3. 3
  4. 4
  5. 5
  6. 6
  7. 7
  8. 8
  9. 9
  10. 10
  11. 11
  12. 12
  13. 13
  14. 14
  15. 15
  16. 16
  17. 17
  18. 18
  19. 19
  20. 20
  21. 21
  22. 22
  23. 23
  24. 24
  25. 25
  26. 26
  27. 27
  28. 28
  29. 29
  30. 30
  31. 31
  32. 32
  33. 33
  34. 34
  35. 35
  36. 36
  37. 37
  38. 38
  39. 39
  40. 40
  41. 41
  42. 42
  43. 43
  44. 44
  45. 45
  46. 46
  47. 47
  48. 48
  49. 49
  50. 50
  51. 51
  52. 52
  53. 53
  54. 54
  55. 55
  56. 56
  57. 57
  58. 58
  59. 59
  60. 60
  61. 61
  62. 62
  63. 63
  64. 64
  65. 65
  66. 66
  67. 67
  68. 68
  69. 69
  70. 70
  71. 71
  72. 72
  73. 73
  74. 74
  75. 75
  76. 76
  77. 77
  78. 78
  79. 79
  80. 80
  81. 81
  82. 82
  83. 83
  84. 84
  85. 85
  86. 86
  87. 87
  88. 88
  89. 89
  90. 90
  91. 91
  92. 92
  93. 93
  94. 94
  95. 95
  96. 96
  97. 97
  98. 98
  99. 99
  100. 100
  101. 101
  102. 102
  103. 103
  104. 104
  105. 105
  106. 106
  107. 107
  108. 108
  109. 109
  110. 110
  111. 111
  112. 112
  113. 113
  114. 114
  115. 115
  116. 116
  117. 117
  118. 118
  119. 119
  120. 120
  121. 121
  122. 122
  123. 123
  124. 124
  125. 125
  126. 126
  127. 127
  128. 128
  129. 129
  130. 130
  131. 131
  132. 132
  133. 133
  134. 134
  135. 135
  136. 136
  137. 137
  138. 138
  139. 139
  140. 140
  141. 141
  142. 142
  143. 143
  144. 144
  145. 145
  146. 146
  147. 147
  148. 148
  149. 149
  150. 150

Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 51 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

Davide abvomereza kucimwa kwace, apempha Mulungu amkhululukire, asamcotsere Mzimu Woyera

Kwa Mkulu wa Nyimbo. Salmo la Davide; m'mene anamdzera Natani mnenertso atalowa iye kwa Bateseba.

1. Mundicitire ine cifundo, Mulungu,Monga mwa kukoma mtima kwanu;Monga mwa unyinji wa nsoni zokoma zanuMufafanize macimo anga.

2. Mubwereze kunditsuka mphulupulu yanga,Ndipo mundiyeretse kundicotsera coipa canga,

3. Cifukwa ndazindikira macimo anga;Ndipo coipa canga ciri pamaso panga cikhalire:

4. Pa Inu, Inu nokha, ndinacimwa,Ndipo ndinacicita coipaco pamaso panu:Kuti mukhale wolungama pakulankhula Inu,Mukhalenso woyera pa kuweruza kwanu.

5. Onani, ndinabadwa m'mphulupulu:Ndipo mai wanga anandilandira m'zoipa.

6. Onani, Inu mukondwera ndi zoonadi m'malo a m'katimo;Ndipo m'malo a m'tseri mudzandidziwitsa nzeru.

7. Mundiyeretse ndi hisope ndipo ndidzayera;Munditsuke ndipo ndidzakhala wa mbu woposa matalala.

8. Mundimvetse cimwemwe ndi kusekera:Kuti mafupawo munawatyola akondwere.

9. Muzibisire nkhope yanu zolakwa zanga,Ndipo mufafanize mphulupulu zanga zonse.

10. Mundilengere mtima woyera, Mulungu;Mukonze mzimu wokhazikika m'kati mwanga.

11. Musanditaye kundicotsa pamaso panu;Musandicotsere Mzimu wanu Woyera.

12. Mundibwezere cimwemwe ca cipulumutso canu;Ndipo mzimu wakulola undigwirizize.

13. Pomwepo ndidzalangiza ocimwa njira zanu;Ndipo olakwa adzabwera kwa Inu.

14. Mundilanditse ku mlandu wa mwazi, Mulungu,Ndinu Mulungu wa cipulumutso canga;Lilime langalidzakweza Nyimbo ya cilungamo canu.

15. Ambuye, tsegulani pa milomo yanga;Ndipo pakamwa panga padzalalikira ulemekezo wanu.

16. Pakuti simukondwera ndi nsembe, mwenzi nditapereka;Nsembe yopsereza simuikonda.

17. Nsembe za Mulungu ndizo mzimu wosweka;Inu, Mulungu, simudzaupeputsa mtima wosweka ndi wolapa.

18. Citirani Ziyoni cokoma monga mwa kukondwera kwanu;Mumange malinga a miyala a Yerusalemu.

19. Pamenepo mudzakondwera nazo nsembe zacilungamo,Ndi nsembe yopsereza ndi yopsereza yathunthu:Pamenepo adzaperekaNg'ombe pa guwa lanu la nsembe.