Mitu

  1. 1
  2. 2
  3. 3
  4. 4
  5. 5
  6. 6
  7. 7
  8. 8
  9. 9
  10. 10
  11. 11
  12. 12
  13. 13
  14. 14
  15. 15
  16. 16
  17. 17
  18. 18
  19. 19
  20. 20
  21. 21
  22. 22
  23. 23
  24. 24
  25. 25
  26. 26
  27. 27
  28. 28
  29. 29
  30. 30
  31. 31
  32. 32
  33. 33
  34. 34
  35. 35
  36. 36
  37. 37
  38. 38
  39. 39
  40. 40
  41. 41
  42. 42
  43. 43
  44. 44
  45. 45
  46. 46
  47. 47
  48. 48
  49. 49
  50. 50
  51. 51
  52. 52
  53. 53
  54. 54
  55. 55
  56. 56
  57. 57
  58. 58
  59. 59
  60. 60
  61. 61
  62. 62
  63. 63
  64. 64
  65. 65
  66. 66
  67. 67
  68. 68
  69. 69
  70. 70
  71. 71
  72. 72
  73. 73
  74. 74
  75. 75
  76. 76
  77. 77
  78. 78
  79. 79
  80. 80
  81. 81
  82. 82
  83. 83
  84. 84
  85. 85
  86. 86
  87. 87
  88. 88
  89. 89
  90. 90
  91. 91
  92. 92
  93. 93
  94. 94
  95. 95
  96. 96
  97. 97
  98. 98
  99. 99
  100. 100
  101. 101
  102. 102
  103. 103
  104. 104
  105. 105
  106. 106
  107. 107
  108. 108
  109. 109
  110. 110
  111. 111
  112. 112
  113. 113
  114. 114
  115. 115
  116. 116
  117. 117
  118. 118
  119. 119
  120. 120
  121. 121
  122. 122
  123. 123
  124. 124
  125. 125
  126. 126
  127. 127
  128. 128
  129. 129
  130. 130
  131. 131
  132. 132
  133. 133
  134. 134
  135. 135
  136. 136
  137. 137
  138. 138
  139. 139
  140. 140
  141. 141
  142. 142
  143. 143
  144. 144
  145. 145
  146. 146
  147. 147
  148. 148
  149. 149
  150. 150

Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 28 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

Apempha cipulumutso, ayamika populumutsidwa

Salmo la Davide.

1. Kwa Inu, Yehova, ndidzapfuulira;Thanthwe langa, musandikhalire ngati wosamva:Pakuti ngati munditontholera ine,Ndidzafanana nao iwo akutsikira kumanda.

2. Mverani mau a kupemba kwanga, pamene ndilirira Inu,Pamene ndikweza manja anga kuloza ponenera panu poyera.

3. Musandikoke kundicotsa pamodzi ndi oipa,Ndi ocita zopanda pace;Amene alankhula zamtendere ndi anansi ao,Koma mumtima mwao muli coipa.

4. Muwapatse monga mwa nchito zao, ndi monga mwa coipa cocita iwo:Muwapatse monga mwa macitidwe a manja ao;Muwabwezere zoyenera iwo.

5. Pakuti sasamala nchito za Yehova,Kapena macitidwe a manja ace,Adzawapasula, osawamanganso.

6. Wodalitsika Yehova,Pakuti adamva mau a kupemba kwanga.

7. Yehova ndiye mphamvu yanga, ndi cikopa canga;Mtima wanga wakhulupirira Iye, ndipo anandithandiza:Cifukwa cace mtima wanga ukondwera kwakukuru;Ndipo ndidzamyamika nayo Nyimbo yanga.

8. Yehova ndiye mphamvu yao,Inde mphamvu ya cipulumutso ca wodzozedwa wace.

9. Pulumutsani anthu anu, ndi kudalitsa colandira canu:Muwawetenso, ndi kuwanyamula nthawi zonse.