Mitu

  1. 1
  2. 2
  3. 3
  4. 4
  5. 5
  6. 6
  7. 7
  8. 8
  9. 9
  10. 10
  11. 11
  12. 12
  13. 13
  14. 14
  15. 15
  16. 16
  17. 17
  18. 18
  19. 19
  20. 20
  21. 21
  22. 22
  23. 23
  24. 24
  25. 25
  26. 26
  27. 27
  28. 28
  29. 29
  30. 30
  31. 31
  32. 32
  33. 33
  34. 34
  35. 35
  36. 36
  37. 37
  38. 38
  39. 39
  40. 40
  41. 41
  42. 42
  43. 43
  44. 44
  45. 45
  46. 46
  47. 47
  48. 48
  49. 49
  50. 50
  51. 51
  52. 52
  53. 53
  54. 54
  55. 55
  56. 56
  57. 57
  58. 58
  59. 59
  60. 60
  61. 61
  62. 62
  63. 63
  64. 64
  65. 65
  66. 66
  67. 67
  68. 68
  69. 69
  70. 70
  71. 71
  72. 72
  73. 73
  74. 74
  75. 75
  76. 76
  77. 77
  78. 78
  79. 79
  80. 80
  81. 81
  82. 82
  83. 83
  84. 84
  85. 85
  86. 86
  87. 87
  88. 88
  89. 89
  90. 90
  91. 91
  92. 92
  93. 93
  94. 94
  95. 95
  96. 96
  97. 97
  98. 98
  99. 99
  100. 100
  101. 101
  102. 102
  103. 103
  104. 104
  105. 105
  106. 106
  107. 107
  108. 108
  109. 109
  110. 110
  111. 111
  112. 112
  113. 113
  114. 114
  115. 115
  116. 116
  117. 117
  118. 118
  119. 119
  120. 120
  121. 121
  122. 122
  123. 123
  124. 124
  125. 125
  126. 126
  127. 127
  128. 128
  129. 129
  130. 130
  131. 131
  132. 132
  133. 133
  134. 134
  135. 135
  136. 136
  137. 137
  138. 138
  139. 139
  140. 140
  141. 141
  142. 142
  143. 143
  144. 144
  145. 145
  146. 146
  147. 147
  148. 148
  149. 149
  150. 150

Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 144 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

Davide ayamika Mulungu kuti anamcinjiriza, napempha ampulumutse kuti anthu adalenso

Salmo la Davide.

1. Wolemekezeka Yehova thanthwe langa,Wakuphunzitsa manja anga acite nkhondo,Zala zanga zigwirane nao:

2. Ndiye cifundo canga, ndi linga langa,Msanje wanga, ndi mpulumutsi wanga;Cikopa canga, ndi Iye amene ndimtama;Amene andigonjetsera anthu anga.

3. Yehova, munthu ndani kuti mumdziwa?Mwana wa munthu kuti mumsamalira?

4. Munthu akunga mpweya;Masiku ace akunga mthunzi wopitirira.

5. Weramutsani thambo lanu, Yehova, nimutsike:Khudzani mapiri ndipo adzafuka.

6. Ng'animitsani mphezi, ndi kuwabalalitsa;Tumizani mibvi yanu, ndi kuwapitikitsa,

7. Turutsani manja anu kucokera m'mwamba;Ndikwatuleni ndi kundilanditsa ku madzi akuru,Ku dzanja la alendo;

8. Amene pakamwa pao alankhula zacabe,Ndi dzanja lao lamanja ndilo dzanja lacinyengo.

9. Ndidzakuyimbirani nyimbo yatsopano, Mulungu;Pa cisakasa ca zingwe khumi ndidzayimbira zakukulemekezani.

10. Ndiye amene apatsa mafumu cipulumutso:Amene alanditsa Davide mtumiki wace ku lupanga loipa.

11. Ndilanditseni ndi kundipulumutsa ku dzanja la alendo,Amene pakamwa pao alankhula zacabe,Ndi dzanja lao lamanja ndilo dzanja lacinyengo.

12. Kuti ana athu amuna akhale ngati mmera udakula usanakhwime;Ana athu akazi ngati nsanamira za kungondya, zosema zikometsere nyumba ya mfumu.

13. Kuti nkhokwe zathu zidzale, kutipatsa za mitundu mitundu;Ndi kuti nkhosa zathu ziswane zikwi zikwi, inde zikwi khumi kubusako.

14. Kuti ng'ombe zathu zikhale zasenza katundu;Ndi kuti pasakhale kupasula linga kapena kuturukamo,Pasakhalenso kupfuula m'makwalala athu.

15. Odala anthu akuona zotere; Odala anthu amene Mulungu wao ndi Yehova.