Mitu

  1. 1
  2. 2
  3. 3
  4. 4
  5. 5
  6. 6
  7. 7
  8. 8
  9. 9
  10. 10
  11. 11
  12. 12
  13. 13
  14. 14
  15. 15
  16. 16
  17. 17
  18. 18
  19. 19
  20. 20
  21. 21
  22. 22
  23. 23
  24. 24
  25. 25
  26. 26
  27. 27
  28. 28
  29. 29
  30. 30
  31. 31
  32. 32
  33. 33
  34. 34
  35. 35
  36. 36
  37. 37
  38. 38
  39. 39
  40. 40
  41. 41
  42. 42
  43. 43
  44. 44
  45. 45
  46. 46
  47. 47
  48. 48
  49. 49
  50. 50
  51. 51
  52. 52
  53. 53
  54. 54
  55. 55
  56. 56
  57. 57
  58. 58
  59. 59
  60. 60
  61. 61
  62. 62
  63. 63
  64. 64
  65. 65
  66. 66
  67. 67
  68. 68
  69. 69
  70. 70
  71. 71
  72. 72
  73. 73
  74. 74
  75. 75
  76. 76
  77. 77
  78. 78
  79. 79
  80. 80
  81. 81
  82. 82
  83. 83
  84. 84
  85. 85
  86. 86
  87. 87
  88. 88
  89. 89
  90. 90
  91. 91
  92. 92
  93. 93
  94. 94
  95. 95
  96. 96
  97. 97
  98. 98
  99. 99
  100. 100
  101. 101
  102. 102
  103. 103
  104. 104
  105. 105
  106. 106
  107. 107
  108. 108
  109. 109
  110. 110
  111. 111
  112. 112
  113. 113
  114. 114
  115. 115
  116. 116
  117. 117
  118. 118
  119. 119
  120. 120
  121. 121
  122. 122
  123. 123
  124. 124
  125. 125
  126. 126
  127. 127
  128. 128
  129. 129
  130. 130
  131. 131
  132. 132
  133. 133
  134. 134
  135. 135
  136. 136
  137. 137
  138. 138
  139. 139
  140. 140
  141. 141
  142. 142
  143. 143
  144. 144
  145. 145
  146. 146
  147. 147
  148. 148
  149. 149
  150. 150

Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

Ayamikira cipulumutso cacikuru

Kwa Mkulu wa Nyimbo; pa Mut-laben. Salmo la Davide.

1. Ndidzayamika Yehova ndi mtima wanga wonse;Ndidzawerengera zodabwiza zanu zonse.

2. Ndidzakondwerera ndi kusekera mwa Inu;Ndidzayimbira dzina lanu, Wam'mwambamwamba Inu.

3. Pobwerera m'mbuyo adani anga,Akhumudwa naonongeka pankhope panu,

4. Pakuti mwandiweruzira mlandu wanga;Mwakhala pa mpando wacifumu, Woweruza wolungama.

5. Mwadzudzula amitundu, mwaononga woipayo,Mwafafaniza dzina lao ku nthawi Yomka muyaya.

6. Adaniwo atha psiti, apululuka nthawi zonse;Ndipo midziyo mwaipasula,Cikumbukilo cao pamodzi catha.

7. Koma Yehova akhala cikhalire:Anakonzeratu mpando wacifumu wace kuti aweruze.

8. Ndipo Iyeyu adzaweruza dziko lapansi m'cilungamo,Nadzaweruza anthu molunjika.

9. Ndipo Yehova adzakhala msanje kwa iye wokhalira mphanthi.Msanje m'nyengo za nsautso;

10. Ndipo iwo akudziwa dzina lanu adzakhulupirira Inu;Pakuti, Inu Yehova, simunawasiya iwo akufuna Inu.

11. Yimbirani zoyamika Yehova, wokhala ku Ziyoni;Lalikirani mwa anthu nchito zace.

12. Pakuti Iye wofuna camwazi awakumbukila;Saiwala kulira kwa ozunzika.

13. Ndicitireni cifundo, Yehova;Penyani kuzunzika kwanga kumene andicitira ondidawo,Inu wondinyamula kundicotsa ku zipata za imfa;

14. Kuti ndibukitse lemekezo lanu lonse;Pa bwalo la mwana wamkazi wa Ziyoni,Ndidzakondwera naco cipulumutso canu.

15. Amitundu anagwa m'mbuna imene anaikumba:Lakodwa phazi lao muukonde anaucha.

16. Anadziwika Yehova, anacita kuweruza:Woipayo anakodwa ndi nchito ya manja ace.

17. Oipawo adzabwerera kumanda,Inde amitundu onse akuiwala Mulungu.

18. Pakuti sadzaiwalika nthawi zonse waumphawi,Kapena ciyembekezo ca ozunzika sicidzaonongeka kosatha.

19. Ukani, Yehova, asalimbike munthu;Amitundu aweruzidwe pankhope panu.

20. Muwacititse mantha, Yehova; Adziwe amitundu kuti ali anthu.