Mitu

  1. 1
  2. 2
  3. 3
  4. 4
  5. 5
  6. 6
  7. 7
  8. 8
  9. 9
  10. 10
  11. 11
  12. 12
  13. 13
  14. 14
  15. 15
  16. 16
  17. 17
  18. 18
  19. 19
  20. 20
  21. 21
  22. 22
  23. 23
  24. 24
  25. 25
  26. 26
  27. 27
  28. 28
  29. 29
  30. 30
  31. 31
  32. 32
  33. 33
  34. 34
  35. 35
  36. 36
  37. 37
  38. 38
  39. 39
  40. 40
  41. 41
  42. 42
  43. 43
  44. 44
  45. 45
  46. 46
  47. 47
  48. 48
  49. 49
  50. 50
  51. 51
  52. 52
  53. 53
  54. 54
  55. 55
  56. 56
  57. 57
  58. 58
  59. 59
  60. 60
  61. 61
  62. 62
  63. 63
  64. 64
  65. 65
  66. 66
  67. 67
  68. 68
  69. 69
  70. 70
  71. 71
  72. 72
  73. 73
  74. 74
  75. 75
  76. 76
  77. 77
  78. 78
  79. 79
  80. 80
  81. 81
  82. 82
  83. 83
  84. 84
  85. 85
  86. 86
  87. 87
  88. 88
  89. 89
  90. 90
  91. 91
  92. 92
  93. 93
  94. 94
  95. 95
  96. 96
  97. 97
  98. 98
  99. 99
  100. 100
  101. 101
  102. 102
  103. 103
  104. 104
  105. 105
  106. 106
  107. 107
  108. 108
  109. 109
  110. 110
  111. 111
  112. 112
  113. 113
  114. 114
  115. 115
  116. 116
  117. 117
  118. 118
  119. 119
  120. 120
  121. 121
  122. 122
  123. 123
  124. 124
  125. 125
  126. 126
  127. 127
  128. 128
  129. 129
  130. 130
  131. 131
  132. 132
  133. 133
  134. 134
  135. 135
  136. 136
  137. 137
  138. 138
  139. 139
  140. 140
  141. 141
  142. 142
  143. 143
  144. 144
  145. 145
  146. 146
  147. 147
  148. 148
  149. 149
  150. 150

Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 92 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

Anthu onse ayamike Mulungu cifukwa ca nchito zace, cilungamo cace, ndi cifundo cace

Satmo, Nyimbo ya pa Sabata,

1. Nkokoma kuyamika Yehova,Ndi kuyimbira nyimbo dzina lanu, Wam'mwambamwamba Inu:

2. Kuonetsera cifundo canu mamawa,Ndi cikhulupiriko canu usiku uli wonse.

3. Pa coyimbira ca zingwe khumi ndi pacisakasa;Pazeze ndi kulira kwace.

4. Popeza Inu, Yehova, munandikondweretsa ndi kucita kwanu,Ndidzapfuula mokondwera pa nchito ya manja anu.

5. Ha! nchito zanu nzazikuru, Yehova,Zolingalira zanu nzozama ndithu.

6. Munthu wopulukira sacidziwa;Ndi munthu wopusa sacizindikira ici;

7. Cakuti pophuka oipa ngati msipu,Ndi popindula ocita zopanda pace;Citero kuti adzaonongeke kosatha:

8. Koma Inu, Yehova, muli m'mwamba ku nthawi yonse.

9. Pakuti, taonani, adani anu, Yehova,Pakuti, taonani, adani anu adzatayika;Ocita zopanda pace onse adzamwazika.

10. Koma munakweza nyanga yanga ngati ya njati;Anandidzoza mafuta atsopano.

11. Diso langa lapenya cokhumba ine pa iwo ondilalira,M'makutu mwanga ndamva cokhumba ine pa iwo akucita zoipa akundiukira.

12. Wolungama adzaphuka ngati mgwalangwa;Adzakula ngati mkungudza wa ku Lebano.

13. Iwo ookedwa m'nyumba ya Yehova,Adzaphuka m'mabwalo a Mulungu wathu.

14. Atakalamba adzapatsanso zipatso;Adzadzazidwa ndi madzi nadzakhala abiriwiri:

15. Kulalikira kuti Yehova ngwolunjika;Iye ndiye thanthwe langa, ndipo mwa Iye mulibe cosalungama.