Mitu

  1. 1
  2. 2
  3. 3
  4. 4
  5. 5
  6. 6
  7. 7
  8. 8
  9. 9
  10. 10
  11. 11
  12. 12
  13. 13
  14. 14
  15. 15
  16. 16
  17. 17
  18. 18
  19. 19
  20. 20
  21. 21
  22. 22
  23. 23
  24. 24
  25. 25
  26. 26
  27. 27
  28. 28
  29. 29
  30. 30
  31. 31
  32. 32
  33. 33
  34. 34
  35. 35
  36. 36
  37. 37
  38. 38
  39. 39
  40. 40
  41. 41
  42. 42
  43. 43
  44. 44
  45. 45
  46. 46
  47. 47
  48. 48
  49. 49
  50. 50
  51. 51
  52. 52
  53. 53
  54. 54
  55. 55
  56. 56
  57. 57
  58. 58
  59. 59
  60. 60
  61. 61
  62. 62
  63. 63
  64. 64
  65. 65
  66. 66
  67. 67
  68. 68
  69. 69
  70. 70
  71. 71
  72. 72
  73. 73
  74. 74
  75. 75
  76. 76
  77. 77
  78. 78
  79. 79
  80. 80
  81. 81
  82. 82
  83. 83
  84. 84
  85. 85
  86. 86
  87. 87
  88. 88
  89. 89
  90. 90
  91. 91
  92. 92
  93. 93
  94. 94
  95. 95
  96. 96
  97. 97
  98. 98
  99. 99
  100. 100
  101. 101
  102. 102
  103. 103
  104. 104
  105. 105
  106. 106
  107. 107
  108. 108
  109. 109
  110. 110
  111. 111
  112. 112
  113. 113
  114. 114
  115. 115
  116. 116
  117. 117
  118. 118
  119. 119
  120. 120
  121. 121
  122. 122
  123. 123
  124. 124
  125. 125
  126. 126
  127. 127
  128. 128
  129. 129
  130. 130
  131. 131
  132. 132
  133. 133
  134. 134
  135. 135
  136. 136
  137. 137
  138. 138
  139. 139
  140. 140
  141. 141
  142. 142
  143. 143
  144. 144
  145. 145
  146. 146
  147. 147
  148. 148
  149. 149
  150. 150

Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 38 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

Davide aulula zoipa zace, apempha Mulungu amkhululukire namthandize

Salmo la Davtde, lakukumbutsa.

1. Yehova, musandidzudzule ndi mkwiyo wanu:Ndipo musandilange moopsa m'mtima mwanu.

2. Pakuti mibvi yanu yandilowa,Ndi dzanja lanu landigwera.

3. Mumnofu mwanga mulibe camoyo cifukwa ca ukali wanu;Ndipo m'mafupa anga simuzizira, cifukwa ca colakwa canga.

4. Pakuti mphulupulu zanga zapitirira pamutu panga:Ndathodwa nazo monga ndi katundu wolemera.

5. Mabala anga anunkha, adaola, Cifukwa ca kupusa kwanga.

6. Ndapindika, ndawerama kwakukuru;Ndimayenda woliralira tsiku lonse.

7. Pakuti m'cuuno mwanga mutentha kwambiri;Palibe pamoyo m'mnofu mwanga,

8. Ndafoka ine, ndipo ndacinjizidwa:Ndabangula cifukwa ca kumyuka mtima wanga.

9. Ambuye, cikhumbo canga conse ciri pamaso panu;Ndipo kubuula kwanga sikubisika kwa Inu.

10. Mtima wanga ugundagunda, mphamvu yanga yacoka:Ndipo kuunika kwa maso anga, ndi iko komwe kwandicokera.

11. Ondikonda ndi anzanga apewa mliri wanga;Ndipo anansi anga aima patali.

12. Ndipo andichera misampha iwo akufuna moyo wanga;Ndipo iwo akuyesa kundicitira coipa alankhula zoononga,Nalingirira zonyenga tsiku lonse.

13. Koma ine, monga gonthi, sindimva;Ndipo monga munthu wosalankhula, sinditsegula pakamwa panga.

14. Inde ndikunga munthu wosamva,Ndipo m'kamwa mwanga mulibe makani.

15. Pakuti ndikuyembekezani Inu, Yehova;Inu mudzayankha, Ambuye Mulungu wanga.

16. Pakuti ndinati, Asakondwerere ine:Pakuterereka phazi langa, asadzikuze pa ine.

17. Ndafikana potsimphina;Ndipo cisoni canga ciri pamaso panga cikhalire.

18. Pakuti ndidzafotokozera mphulupulu yanga;Nditenga nkhawa cifukwa ca chimo langa.

19. Koma adani anga ali ndi moyo, nakhalandi mphamvu:Ndipo akundida kopanda cifukwa acuruka.

20. Ndipo iwo akubwezera coipa pa cabwinoAtsutsana nane, popeza nditsata cabwino.

21. Musanditaye, Yehova:Mulungu wanga, musakhale kutali ndi ine.

22. Fulumirani kundithandiza,Ambuye, cipulumutso canga.