Mitu

  1. 1
  2. 2
  3. 3
  4. 4
  5. 5
  6. 6
  7. 7
  8. 8
  9. 9
  10. 10
  11. 11
  12. 12
  13. 13
  14. 14
  15. 15
  16. 16
  17. 17
  18. 18
  19. 19
  20. 20
  21. 21
  22. 22
  23. 23
  24. 24
  25. 25
  26. 26
  27. 27
  28. 28
  29. 29
  30. 30
  31. 31
  32. 32
  33. 33
  34. 34
  35. 35
  36. 36
  37. 37
  38. 38
  39. 39
  40. 40
  41. 41
  42. 42
  43. 43
  44. 44
  45. 45
  46. 46
  47. 47
  48. 48
  49. 49
  50. 50
  51. 51
  52. 52
  53. 53
  54. 54
  55. 55
  56. 56
  57. 57
  58. 58
  59. 59
  60. 60
  61. 61
  62. 62
  63. 63
  64. 64
  65. 65
  66. 66
  67. 67
  68. 68
  69. 69
  70. 70
  71. 71
  72. 72
  73. 73
  74. 74
  75. 75
  76. 76
  77. 77
  78. 78
  79. 79
  80. 80
  81. 81
  82. 82
  83. 83
  84. 84
  85. 85
  86. 86
  87. 87
  88. 88
  89. 89
  90. 90
  91. 91
  92. 92
  93. 93
  94. 94
  95. 95
  96. 96
  97. 97
  98. 98
  99. 99
  100. 100
  101. 101
  102. 102
  103. 103
  104. 104
  105. 105
  106. 106
  107. 107
  108. 108
  109. 109
  110. 110
  111. 111
  112. 112
  113. 113
  114. 114
  115. 115
  116. 116
  117. 117
  118. 118
  119. 119
  120. 120
  121. 121
  122. 122
  123. 123
  124. 124
  125. 125
  126. 126
  127. 127
  128. 128
  129. 129
  130. 130
  131. 131
  132. 132
  133. 133
  134. 134
  135. 135
  136. 136
  137. 137
  138. 138
  139. 139
  140. 140
  141. 141
  142. 142
  143. 143
  144. 144
  145. 145
  146. 146
  147. 147
  148. 148
  149. 149
  150. 150

Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 34 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

Davide alemekeza Yehova womlanditsa, nafulumiza ena amtame

Salimo la Davide. Muja anasintha makhalidwe ace pamaso pa Abimeleke, amene anampitikitsa ndipo anacoka.

1. Ndidzalemekeza Yehova nyengo zonse;Kumlemekeza kwace kudzakhala m'kamwa mwanga kosalekeza.

2. Moyo wanga udzatamanda Yehova;Ofatsa adzakumva nadzakondwera.

3. Bukitsani pamodzi ndine ukuru wa Yehova,Ndipo tikweze dzina lace pamodzi.

4. Ndinafuna Yehova ndipo anandibvomera,Nandlianditsa m'mantha anga Onse.

5. Iwo anayang'ana Iye nasanguruka;Ndipo pankhope pao sipadzacita manyazi,

6. Munthu uyu wozunzika anapfuula, ndipo Yehova anamumva,Nampulumutsa m'masautso ace onse.

7. Mngelo wa Yehova azinga kuwacinjiriza iwo akuopa Iye,Nawalanditsa iwo.

8. Talawani, ndipo onani kuti Yehova ndiye wabwino;Wodala munthuyo wakukhulupirira Iye.

9. Opani Yehova, inu oyera mtima ace;Cifukwa iwo akumuopa Iye sasowa.

10. Misona ya mkango isowa nimva njala:Koma iwo akufuna Yehova sadzasowa kanthu kabwino.

11. Idzani ananu ndimvereni ine:Ndidzakulangizani zakumuopa Yehova.

12. Munthu wokhumba moyo ndani,Wokonda masiku, kuti aone zabwino?

13. Uletse lilime lako lisachule zoipa,Ndipo milomo yako isalankhule cinyengo.

14. Pfutuka pazoipa, nucite zabwino,Funa mtendere ndi kuulondola.

15. Maso a Yehova ali pa olungama mtima,Ndipo makutu ace achereza kulira kwao.

16. Nkhopeya Yehovaitsutsananao akucita zoipa,Kudula cikumbukilo cao pa dziko lapansi.

17. Iwowo anaitana, ndipo Yehova anawamva,Nawalanditsa ku masautso ao onse.

18. Yehova ali pafupi ndi iwo a mtimawosweka,Apulumutsa iwo a mzimu wolapadi,

19. Masautso a wolungama mtima acuruka:Koma Yehova amlanditsa mwa onsewa.

20. Iye asunga mafupa ace onse:Silinatyoka limodzi lonse.

21. Mphulupulu idzamupha woipa:Ndipo adzawatsutsa kumlandu iwo akudana naye wolungama.

22. Yehova aombola moyo wa anyamata ace,Ndipo sadzawatsutsa kumlandu onse akukhulupirira Iye.