Mitu

  1. 1
  2. 2
  3. 3
  4. 4
  5. 5
  6. 6
  7. 7
  8. 8
  9. 9
  10. 10
  11. 11
  12. 12
  13. 13
  14. 14
  15. 15
  16. 16
  17. 17
  18. 18
  19. 19
  20. 20
  21. 21
  22. 22
  23. 23
  24. 24
  25. 25
  26. 26
  27. 27
  28. 28
  29. 29
  30. 30
  31. 31
  32. 32
  33. 33
  34. 34
  35. 35
  36. 36
  37. 37
  38. 38
  39. 39
  40. 40
  41. 41
  42. 42
  43. 43
  44. 44
  45. 45
  46. 46
  47. 47
  48. 48
  49. 49
  50. 50
  51. 51
  52. 52
  53. 53
  54. 54
  55. 55
  56. 56
  57. 57
  58. 58
  59. 59
  60. 60
  61. 61
  62. 62
  63. 63
  64. 64
  65. 65
  66. 66
  67. 67
  68. 68
  69. 69
  70. 70
  71. 71
  72. 72
  73. 73
  74. 74
  75. 75
  76. 76
  77. 77
  78. 78
  79. 79
  80. 80
  81. 81
  82. 82
  83. 83
  84. 84
  85. 85
  86. 86
  87. 87
  88. 88
  89. 89
  90. 90
  91. 91
  92. 92
  93. 93
  94. 94
  95. 95
  96. 96
  97. 97
  98. 98
  99. 99
  100. 100
  101. 101
  102. 102
  103. 103
  104. 104
  105. 105
  106. 106
  107. 107
  108. 108
  109. 109
  110. 110
  111. 111
  112. 112
  113. 113
  114. 114
  115. 115
  116. 116
  117. 117
  118. 118
  119. 119
  120. 120
  121. 121
  122. 122
  123. 123
  124. 124
  125. 125
  126. 126
  127. 127
  128. 128
  129. 129
  130. 130
  131. 131
  132. 132
  133. 133
  134. 134
  135. 135
  136. 136
  137. 137
  138. 138
  139. 139
  140. 140
  141. 141
  142. 142
  143. 143
  144. 144
  145. 145
  146. 146
  147. 147
  148. 148
  149. 149
  150. 150

Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 104 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

Ulemerero wa Mulungu m'zolengedwa ndi m'kuzisunga komwe

1. Lemekeza Yehova, moyo wanga;Yehova, Mulungu wanga, Inu ndinu wamkurukuru;

2. Mubvala ulemu ndi cifumu.Amene mudzikuta nako kuunika monga ndi cobvala;Ndi kuyala thambo ngati nsaru yocinga;

3. Amene alumikiza mitanda ya zipinda zace m'madzi;Naika makongwa akhale agareta ace;Nayenda pa mapiko a mphepo;

4. Amene ayesa mphepo amithenga ace;Lawi la moto atumiki ace;

5. Anakhazika dziko lapansi pa maziko ace,Silidzagwedezeka ku nthawi yonse.

6. Mudalikuta ndi nyanja ngati ndi cobvala;Madzi anafikira pamwamba pa mapiri,

7. Pa kudzudzula kwanu anathawa;Anathawa msanga liu la bingu lanu;

8. Anakwera m'mapiri, anatsikira m'zigwa,Kufikira malo mudawakonzeratu.

9. Munaika malire kuti asapitirireko;Kuti asabwererenso kuphimba dziko lapansi.

10. Atumiza akasupe alowe m'makwawa;Ayenda pakati pa mapiri:

11. Zimamwamo nyama zonse za kuthengo;Mbidzi zipherako ludzu lao.

12. Mbalame za mlengalenga zifatsa pamenepo,Zimayimba pakati pa mitawi.

13. Iye amwetsa mapiri mocokera m'zipinda zace:Dziko lakhuta zipatso za nchito zanu.

14. Ameretsa msipu ziudye ng'ombe,Ndi zitsamba acite nazo munthu;Naturutse cakudya cocokera m'nthaka;

15. Ndi vinyo wokondweretsa mtima wa munthu,Ndi mafuta akunyezimiritsa nkhope yace,Ndi mkate wakulimbitsa mtima wa munthu.

16. Mitengo ya Mulungu yadzala ndi madzi;Mikungudza ya ku Lebano imene anaioka;

17. M'mwemo mbalame zimanga zisa zao;Pokhala cumba mpa mitengo ya mikungudza,

18. Mapiri atali ndiwo ayenera zinkhoma;Pamatanthwe mpothawirapo mbira.

19. Anaika mwezi nyengo zace;Dzuwa lidziwa polowera pace.

20. Muika mdima ndipo pali usiku;Pamenepo zituruka zirombo zonse za m'thengo.

21. Misona ya mkango ibangula potsata nyama yao,Nifuna cakudya cao kwa Mulungu.

22. Poturuka dzuwa, zithawa, Zigona pansi m'ngaka mwao.

23. Pamenepo munthu aturukira ku nchito yace,Nagwiritsa kufikira madzulo.

24. Nchito zanu zicurukadi, Yehova!Munazicita zonse mwanzeru;Dziko lapansi lidzala naco cuma canu.

25. Nyanja siyo, yaikuru ndi yacitando,M'mwemo muli zokwawa zosawerengeka;Zamoyo zazing'ono ndi zazikuru.

26. M'mwemo muyenda zombo;Ndi livyatanu amene munamlenga aseweremo.

27. Izi zonse zikulindirirani,Muzipatse cakudya cao pa nyengo yace.

28. Cimene muzipatsa zigwira;Mufumbatula dzanja lanu, zikhuta zabwino.

29. Mukabisa nkhope yanu, ziopsedwa;Mukalanda mpweya wao, zikufa,Nizibwerera kupfumbi kwao.

30. Potumizira mzimu wanu, zilengedwa;Ndipo mukonzanso nkhope ya dziko lapansi.

31. Ulemerero wa Yehova ukhale kosatha;Yehova akondwere mu nchito zace;

32. Amene apenyerera pa dziko lapansi, ndipo linjenjemera;Akhudza mapiri, ndipo afuka.

33. Ndidzayimbira Yehova m'moyo mwanga:Ndidzayimbira Mulungu wanga zomlemekeza pokhala ndiripo.

34. Pomlingirira Iye pandikonde;Ndidzakondwera mwa Yehova.

35. Ocimwa athedwe ku dziko lapansi,Ndi oipa asakhalenso.Yamika Yehova, moyo wanga.Haleluya.