Mitu

  1. 1
  2. 2
  3. 3
  4. 4
  5. 5
  6. 6
  7. 7
  8. 8
  9. 9
  10. 10
  11. 11
  12. 12
  13. 13
  14. 14
  15. 15
  16. 16
  17. 17
  18. 18
  19. 19
  20. 20
  21. 21
  22. 22
  23. 23
  24. 24
  25. 25
  26. 26
  27. 27
  28. 28
  29. 29
  30. 30
  31. 31
  32. 32
  33. 33
  34. 34
  35. 35
  36. 36
  37. 37
  38. 38
  39. 39
  40. 40
  41. 41
  42. 42
  43. 43
  44. 44
  45. 45
  46. 46
  47. 47
  48. 48
  49. 49
  50. 50
  51. 51
  52. 52
  53. 53
  54. 54
  55. 55
  56. 56
  57. 57
  58. 58
  59. 59
  60. 60
  61. 61
  62. 62
  63. 63
  64. 64
  65. 65
  66. 66
  67. 67
  68. 68
  69. 69
  70. 70
  71. 71
  72. 72
  73. 73
  74. 74
  75. 75
  76. 76
  77. 77
  78. 78
  79. 79
  80. 80
  81. 81
  82. 82
  83. 83
  84. 84
  85. 85
  86. 86
  87. 87
  88. 88
  89. 89
  90. 90
  91. 91
  92. 92
  93. 93
  94. 94
  95. 95
  96. 96
  97. 97
  98. 98
  99. 99
  100. 100
  101. 101
  102. 102
  103. 103
  104. 104
  105. 105
  106. 106
  107. 107
  108. 108
  109. 109
  110. 110
  111. 111
  112. 112
  113. 113
  114. 114
  115. 115
  116. 116
  117. 117
  118. 118
  119. 119
  120. 120
  121. 121
  122. 122
  123. 123
  124. 124
  125. 125
  126. 126
  127. 127
  128. 128
  129. 129
  130. 130
  131. 131
  132. 132
  133. 133
  134. 134
  135. 135
  136. 136
  137. 137
  138. 138
  139. 139
  140. 140
  141. 141
  142. 142
  143. 143
  144. 144
  145. 145
  146. 146
  147. 147
  148. 148
  149. 149
  150. 150

Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

Davide atamadi Yehova, naliradi kuyanjana ndi Mulungu

Salmo la Davide,

1. Yehova ndiye kuunika kwanga ndi cipulumutso canga; ndidzaopa yani?Yehova ndiye mphamvu ya moyo wanga; ndidzacita mantha ndi yani?

2. Pondifika ine ocita zoipa kudzadya mnofu wanga,Inde akundisautsa ndi adani anga, anakhumudwa iwo nagwa.

3. Lingakhale gulu la ankhondo limanga misasa kuti andithyole,Mtima wanga sungacite mantha:Ingakhale nkhondo ikandiukira,Nde pomweponso ndidzakhulupira,

4. Cinthu cimodzi ndinacipempha kwa Yehova, ndidzacilondola ici:Kuti ndikhalitse m'nyumba ya Yehova masiku onse a moyo wanga,Kupenya kukongola kwace kwa Yehova ndi kufunsitsa m'Kacisi wace.

5. Cifukwa kuti pa dzuwa la tsoka Iye adzandibisa mumsasa mwace:Adzandibisa m'tsenjezi mwa cihema cace;Pathanthwe adzandikweza.

6. Ndipo tsopano mutu wanga udzakwezeka pamwamba pa adani anga akundizinga;Ndipo ndidzapereka m'cihema mwace nsembe za kupfuula mokondwera;Ndidzayimba, inde, ndidzayimbira Yehova zomlemekeza.

7. Imvani, Yehova, liu langa popfuula ine:Mundicitirenso cifundo ndipo mundibvomereze.

8. Pamene munati, Punani nkhope yanga; mtima wanga unati kwa Inu:Nkhope yanu, Yehova, ndidzaifuna.

9. Musandibisire ine nkhope yanu;Musacotse kapolo wanu ndi kukwiya:Inu munakhala thandizo langa;Musanditaye, ndipo musandisiye Mulungu wa cipulumutso canga,

10. Pakuti wandisiya atate wanga ndi amai wanga,Koma Yehova anditola.

11. Mundiphunzitse njira yanu, Yehova,Munditsogolere pa njira yacidikha,Cifukwa ca adani anga,

12. Musandipereke ku cifuniro ca akundisautsa;Cifukwa zinandiukira mboni zonama ndi iwo akupumira zaciwawa.

13. Ndikadapanda kukhulupirira kuti ndikaone ubwino wa YehovaM'dziko la amoyo, ndikadatanil

14. Yembekeza Yehova:Limbika, ndipo Iye adzalimbitsa mtima wako;Inde, yembekeza Yehova.