Mitu

  1. 1
  2. 2
  3. 3
  4. 4
  5. 5
  6. 6
  7. 7
  8. 8
  9. 9
  10. 10
  11. 11
  12. 12
  13. 13
  14. 14
  15. 15
  16. 16
  17. 17
  18. 18
  19. 19
  20. 20
  21. 21
  22. 22
  23. 23
  24. 24
  25. 25
  26. 26
  27. 27
  28. 28
  29. 29
  30. 30
  31. 31
  32. 32
  33. 33
  34. 34
  35. 35
  36. 36
  37. 37
  38. 38
  39. 39
  40. 40
  41. 41
  42. 42
  43. 43
  44. 44
  45. 45
  46. 46
  47. 47
  48. 48
  49. 49
  50. 50
  51. 51
  52. 52
  53. 53
  54. 54
  55. 55
  56. 56
  57. 57
  58. 58
  59. 59
  60. 60
  61. 61
  62. 62
  63. 63
  64. 64
  65. 65
  66. 66
  67. 67
  68. 68
  69. 69
  70. 70
  71. 71
  72. 72
  73. 73
  74. 74
  75. 75
  76. 76
  77. 77
  78. 78
  79. 79
  80. 80
  81. 81
  82. 82
  83. 83
  84. 84
  85. 85
  86. 86
  87. 87
  88. 88
  89. 89
  90. 90
  91. 91
  92. 92
  93. 93
  94. 94
  95. 95
  96. 96
  97. 97
  98. 98
  99. 99
  100. 100
  101. 101
  102. 102
  103. 103
  104. 104
  105. 105
  106. 106
  107. 107
  108. 108
  109. 109
  110. 110
  111. 111
  112. 112
  113. 113
  114. 114
  115. 115
  116. 116
  117. 117
  118. 118
  119. 119
  120. 120
  121. 121
  122. 122
  123. 123
  124. 124
  125. 125
  126. 126
  127. 127
  128. 128
  129. 129
  130. 130
  131. 131
  132. 132
  133. 133
  134. 134
  135. 135
  136. 136
  137. 137
  138. 138
  139. 139
  140. 140
  141. 141
  142. 142
  143. 143
  144. 144
  145. 145
  146. 146
  147. 147
  148. 148
  149. 149
  150. 150

Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 91 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

Mulungu asungadi wodzipereka kwa Iye

1. Iye amene akhala pansi m'ngaka yace ya Wam'mwambamwambaAdzagonera mu mthunzi wa Wamphamvuyonse.

2. Ndidzati kwa Yehova, Pothawirapo panga ndi linga langa;Mulungu wanga, amene ndimkhulupirira,

3. Pakuti adzakuonjola ku msampha wa msodzi,Ku mliri wosakaza.

4. Adzakufungatira ndi nthenga zace,Ndipo udzathawira kunsi kwa mapiko ace;Coonadi cace ndico cikopa cocinjiriza.

5. Sudzaopa coopsa ca usiku, Kapena mubvi wopita usana;

6. Kapena mliri woyenda mumdima,Kapena cionongeko cakuthera usana.

7. Pambali pako padzagwa cikwi,Ndi zikwi khumi pa dzanja lamanja lako;Sicidzakuyandikiza iwe.

8. Koma udzapenya ndi maso ako,Nudzaona kubwezera cilango oipa.

9. Popeza udati, Inu Yehova, ndinu pothawirapo pangaUdaika Wam'mwambamwamba cokhalamo cako;

10. Palibe coipa cidzakugwera,Ndipo colanga sicidzayandikiza hema wako.

11. Pakuti adzalamulira angelo ace za iwe,Akusunge m'njira zako zonse.

12. Adzakunyamula pa manja ao,Ungagunde phazi lako pamwala.

13. Udzaponda mkango ndi mphiri;Udzapondereza msona wa mkango ndi cinjoka:

14. Popeza andikondadi ndidzampulumutsa;Ndidzamkweza m'mwamba, papeza adziwa dzina langa.

15. Adzandipfuulira Ine ndipo ndidzamyankha;Kunsautso ndidzakhala naye pamodzi;Ndidzamlanditsa, ndi kumcitira ulemu.

16. Ndidzamkhutitsa ndi masiku ambiri,Ndi kumuonetsera cipulumutso canga,