Mitu

  1. 1
  2. 2
  3. 3
  4. 4
  5. 5
  6. 6
  7. 7
  8. 8
  9. 9
  10. 10
  11. 11
  12. 12
  13. 13
  14. 14
  15. 15
  16. 16
  17. 17
  18. 18
  19. 19
  20. 20
  21. 21
  22. 22
  23. 23
  24. 24
  25. 25
  26. 26
  27. 27
  28. 28
  29. 29
  30. 30
  31. 31
  32. 32
  33. 33
  34. 34
  35. 35
  36. 36
  37. 37
  38. 38
  39. 39
  40. 40
  41. 41
  42. 42
  43. 43
  44. 44
  45. 45
  46. 46
  47. 47
  48. 48
  49. 49
  50. 50
  51. 51
  52. 52
  53. 53
  54. 54
  55. 55
  56. 56
  57. 57
  58. 58
  59. 59
  60. 60
  61. 61
  62. 62
  63. 63
  64. 64
  65. 65
  66. 66
  67. 67
  68. 68
  69. 69
  70. 70
  71. 71
  72. 72
  73. 73
  74. 74
  75. 75
  76. 76
  77. 77
  78. 78
  79. 79
  80. 80
  81. 81
  82. 82
  83. 83
  84. 84
  85. 85
  86. 86
  87. 87
  88. 88
  89. 89
  90. 90
  91. 91
  92. 92
  93. 93
  94. 94
  95. 95
  96. 96
  97. 97
  98. 98
  99. 99
  100. 100
  101. 101
  102. 102
  103. 103
  104. 104
  105. 105
  106. 106
  107. 107
  108. 108
  109. 109
  110. 110
  111. 111
  112. 112
  113. 113
  114. 114
  115. 115
  116. 116
  117. 117
  118. 118
  119. 119
  120. 120
  121. 121
  122. 122
  123. 123
  124. 124
  125. 125
  126. 126
  127. 127
  128. 128
  129. 129
  130. 130
  131. 131
  132. 132
  133. 133
  134. 134
  135. 135
  136. 136
  137. 137
  138. 138
  139. 139
  140. 140
  141. 141
  142. 142
  143. 143
  144. 144
  145. 145
  146. 146
  147. 147
  148. 148
  149. 149
  150. 150

Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

Munthu wokhulupira Mulungu akhazikika mtima, osaopa kutayika

Mlkitamu wa Davide.

1. Ndisungeni ine, Mulungu: pakuti ndakhulupirira Inu.

2. Ndinati kwa Yehova, Inu ndinu Ambuye wanga:Ndiribe cabwino cina coposa Inu.

3. Za oyera mtima okhala pa dziko lapansi,Iwo ndiwo omveka mbiri, mwa iwowo muli cikondwero canga conse.

4. Zidzacuruka zisoni zao za iwo otsata mulungu wina:Sindidzathira nsembe zao zamwazi,Ndipo sindidzachula maina ao pakamwa panga,

5. Yehova ndiye gawo la colowa canga ndi cikho canga:Ndinu wondigwirira colandira canga,

6. Zingwe zandigwera mondikondweretsa;Inde cosiyira cokoma ndiri naco.

7. Ndidzadalitsa Yehova, amene anandicitira uphungu:Usikunso imso zanga zindilangiza.

8. Ndaika Yehova patsogolo panga nthawi zonse:Popeza ali pa dzanja langa lamanja, sindidzagwedezeka.

9. Cifukwa cace wasekera mtima wanga, nukondwera ulemu wanga;Mnofu wanganso udzakhala mokhazikika.

10. Pakuti simudzasiya moyo wanga kumanda;Simudzalola wokondedwa wanu abvunde.

11. Mudzandidziwitsa njira ya moyo:Pankhope panu pali cimwemwe cokwanira;M'dzanja lanu lamanja muli zokondweretsa zomka muyaya.