Mitu

  1. 1
  2. 2
  3. 3
  4. 4
  5. 5
  6. 6
  7. 7
  8. 8
  9. 9
  10. 10
  11. 11
  12. 12
  13. 13
  14. 14
  15. 15
  16. 16
  17. 17
  18. 18
  19. 19
  20. 20
  21. 21
  22. 22
  23. 23
  24. 24
  25. 25
  26. 26
  27. 27
  28. 28
  29. 29
  30. 30
  31. 31
  32. 32
  33. 33
  34. 34
  35. 35
  36. 36
  37. 37
  38. 38
  39. 39
  40. 40
  41. 41
  42. 42
  43. 43
  44. 44
  45. 45
  46. 46
  47. 47
  48. 48
  49. 49
  50. 50
  51. 51
  52. 52
  53. 53
  54. 54
  55. 55
  56. 56
  57. 57
  58. 58
  59. 59
  60. 60
  61. 61
  62. 62
  63. 63
  64. 64
  65. 65
  66. 66
  67. 67
  68. 68
  69. 69
  70. 70
  71. 71
  72. 72
  73. 73
  74. 74
  75. 75
  76. 76
  77. 77
  78. 78
  79. 79
  80. 80
  81. 81
  82. 82
  83. 83
  84. 84
  85. 85
  86. 86
  87. 87
  88. 88
  89. 89
  90. 90
  91. 91
  92. 92
  93. 93
  94. 94
  95. 95
  96. 96
  97. 97
  98. 98
  99. 99
  100. 100
  101. 101
  102. 102
  103. 103
  104. 104
  105. 105
  106. 106
  107. 107
  108. 108
  109. 109
  110. 110
  111. 111
  112. 112
  113. 113
  114. 114
  115. 115
  116. 116
  117. 117
  118. 118
  119. 119
  120. 120
  121. 121
  122. 122
  123. 123
  124. 124
  125. 125
  126. 126
  127. 127
  128. 128
  129. 129
  130. 130
  131. 131
  132. 132
  133. 133
  134. 134
  135. 135
  136. 136
  137. 137
  138. 138
  139. 139
  140. 140
  141. 141
  142. 142
  143. 143
  144. 144
  145. 145
  146. 146
  147. 147
  148. 148
  149. 149
  150. 150

Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 109 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

Davide apempha Mulungu alange oipa, amlanditse m'manja mwao

Kwa Mkulu wa Nyimbo; Salmo la Davide,

1. Mulungu wa cilemekezo canga, musakhale cete;

2. Pakuti pakamwa pa woipa ndi pakamwa pa cinyengo pananditsegukira;Anandilankhulira ndi m'kamwa mwa bodza.

3. Ndipo anandizinga ndi mau a udani,Nalimbana nane kopanda cifukwa.

4. M'malo mwa cikondi canga andibwezera udani;Koma ine, kupemphera ndiko.

5. Ndipo anandisenza coipa m'malo mwa cokoma,Ndi udani m'malo mwa cikondi canga.

6. Muike munthu woipa akhale mkuru wace;Ndi mdani aime pa dzanja lamanja lace.

7. Ponenedwa mlandu wace aturuke wotsutsika;Ndi pemphero lace likhale ngati kucimwa.

8. Masiku ace akhale owerengeka;Wina alandire udindo wace.

9. Ana ace akhale amasiye, Ndi mkazi wace wamasiye.

10. Ana ace akhale amcirakuyenda ndi opemphapempha;Afunefune zosowa zao kucokera m'mabwinja mwao.

11. Wokongoletsa agwire zonse ali nazo;Ndi alendo alande za nchito yace.

12. Pasakhale munthu wakumdtira cifundo;Kapena kucitira cokoma ana ace amasiye.

13. Zidzukulu zace zidulidwe;Dzina lao lifafanizidwe mu mbadwo ukudza.

14. Mphulupulu za makolo ace zikumbukike ndi Yehova;Ndi cimo la mai wace lisafafanizidwe.

15. Zikhale pamaso pa Yehova cikhalire,Kuti adule cikumbukilo cao kucicotsera ku dziko lapansi.

16. Cifukwa kuti sanakumbukila kucita cifundo,Koma analondola wozunzika ndi waumphawi,Ndi wosweka mtima, kuti awaphe.

17. Inde, anakonda kutemberera, ndipo kudamdzera mwini;Sanakondwera nako kudalitsa, ndipo kudamkhalira kutali.

18. Anabvalanso temberero ngati maraya,Ndipo lidamlowa m'kati mwace ngati madzi,Ndi ngati mafuta m'mafupa ace.

19. Limkhalire ngati cobvala adzikuta naco,Ndi lamba limene adzimangirira nalo m'cuuno cimangirire,

20. Ici cikhale mphotho ya otsutsana nane yowapatsa Yehova,Ndi ya iwo akunenera coipa moyo wanga.

21. Koma Inu, Yehova Ambuye, mucite nane cifukwa ca dzina lanu;Ndilanditseni popeza cifundo canu ndi cabwino.

22. Pakuti ine ndine wozunzika ndi waumphawi,Ndi mtima wanga walaswa m'kati mwanga.

23. Ndamuka ngati mthunzi womka m'taliNdiingidwa kwina ndi kwina ngati dzombe.

24. Mabondo anga agwedezeka cifukwa ca kusala;Ndi mnofu wanga waonda posowa mafuta.

25. Ndiwakhaliranso cotonza;Pakundiona apukusa mutu.

26. Ndithandizeni Yehova, Mulungu wanga:Ndipulumutseni monga mwa cifundo canu;

27. Kuti adziwe kuti ici ndi dzanja lanu;Kuti Inu Yehova munacicita.

28. Atemberere iwowa, koma mudalitse ndinu;Pakuuka iwowa adzacita manyazi, koma mtumiki wanu adzakondwera.

29. Otsutsana nane abvale manyazi,Nadzikute naco cisokonezo cao ngati ndi copfunda.

30. Ndidzayamika Yehova kwakukuru pakamwa panga;Ndi pakati pa anthu aunyinji ndidzamlemekeza.

31. Popeza adzaima pa dzanja lamanja la waumphawiKumpulumutsa kwa iwo akuweruza koipa moyo wace.