Mitu

  1. 1
  2. 2
  3. 3
  4. 4
  5. 5
  6. 6
  7. 7
  8. 8
  9. 9
  10. 10
  11. 11
  12. 12
  13. 13
  14. 14
  15. 15
  16. 16
  17. 17
  18. 18
  19. 19
  20. 20
  21. 21
  22. 22
  23. 23
  24. 24
  25. 25
  26. 26
  27. 27
  28. 28
  29. 29
  30. 30
  31. 31
  32. 32
  33. 33
  34. 34
  35. 35
  36. 36
  37. 37
  38. 38
  39. 39
  40. 40
  41. 41
  42. 42
  43. 43
  44. 44
  45. 45
  46. 46
  47. 47
  48. 48
  49. 49
  50. 50
  51. 51
  52. 52
  53. 53
  54. 54
  55. 55
  56. 56
  57. 57
  58. 58
  59. 59
  60. 60
  61. 61
  62. 62
  63. 63
  64. 64
  65. 65
  66. 66
  67. 67
  68. 68
  69. 69
  70. 70
  71. 71
  72. 72
  73. 73
  74. 74
  75. 75
  76. 76
  77. 77
  78. 78
  79. 79
  80. 80
  81. 81
  82. 82
  83. 83
  84. 84
  85. 85
  86. 86
  87. 87
  88. 88
  89. 89
  90. 90
  91. 91
  92. 92
  93. 93
  94. 94
  95. 95
  96. 96
  97. 97
  98. 98
  99. 99
  100. 100
  101. 101
  102. 102
  103. 103
  104. 104
  105. 105
  106. 106
  107. 107
  108. 108
  109. 109
  110. 110
  111. 111
  112. 112
  113. 113
  114. 114
  115. 115
  116. 116
  117. 117
  118. 118
  119. 119
  120. 120
  121. 121
  122. 122
  123. 123
  124. 124
  125. 125
  126. 126
  127. 127
  128. 128
  129. 129
  130. 130
  131. 131
  132. 132
  133. 133
  134. 134
  135. 135
  136. 136
  137. 137
  138. 138
  139. 139
  140. 140
  141. 141
  142. 142
  143. 143
  144. 144
  145. 145
  146. 146
  147. 147
  148. 148
  149. 149
  150. 150

Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 64 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

Davide apempha Mulungu amciniirize pa omlalira

Kwa Mkulu wa Nyimbo. Salmo la Davido.

1. Imvani Yehova, mau anga, m'kudandaula kwanga;Sungani moyo wanga angandiopse mdani.

2. Ndibiseni pa upo wacinsinsi wa ocita zoipa;Pa phokoso la ocita zopanda pace:

3. Amene anola lilime lao ngati lupanga,Napiringidza mibvi yao, ndiyo mau akuwawitsa;

4. Kuponyera wangwiro mobisika:Amponyera modzidzimutsa, osaopa.

5. Alimbikitsana m'cinthu coipa;Apangana za kuchera misampha mobisika;Akuti, Adzaiona ndani?

6. Afunafuna zosalungama; kusanthula, asanthuladi kutha;Cingakhale ca m'kati mwace mwa munthu, ndi mtima wozama.

7. Koma Mulungu adzawaponyera mubvi;Adzalaswa modzidzimutsa,

8. Adzawakhumudwitsa, lilime lao lidzawatsutsa;Onse akuwaona adzawathawa.

9. Ndipo anthu onse adzacita mantha;Nadzabukitsa cocita Mulungu,Nadzasamalira nchito yace.

10. Wolungama adzakondwera mwa Yehova, nadzakhulupirira Iye;Ndipo oongoka mtima onse adzalemekeza.