Mitu

  1. 1
  2. 2
  3. 3
  4. 4
  5. 5
  6. 6
  7. 7
  8. 8
  9. 9
  10. 10
  11. 11
  12. 12
  13. 13
  14. 14
  15. 15
  16. 16
  17. 17
  18. 18
  19. 19
  20. 20
  21. 21
  22. 22
  23. 23
  24. 24
  25. 25
  26. 26
  27. 27
  28. 28
  29. 29
  30. 30
  31. 31
  32. 32
  33. 33
  34. 34
  35. 35
  36. 36
  37. 37
  38. 38
  39. 39
  40. 40
  41. 41
  42. 42
  43. 43
  44. 44
  45. 45
  46. 46
  47. 47
  48. 48
  49. 49
  50. 50
  51. 51
  52. 52
  53. 53
  54. 54
  55. 55
  56. 56
  57. 57
  58. 58
  59. 59
  60. 60
  61. 61
  62. 62
  63. 63
  64. 64
  65. 65
  66. 66
  67. 67
  68. 68
  69. 69
  70. 70
  71. 71
  72. 72
  73. 73
  74. 74
  75. 75
  76. 76
  77. 77
  78. 78
  79. 79
  80. 80
  81. 81
  82. 82
  83. 83
  84. 84
  85. 85
  86. 86
  87. 87
  88. 88
  89. 89
  90. 90
  91. 91
  92. 92
  93. 93
  94. 94
  95. 95
  96. 96
  97. 97
  98. 98
  99. 99
  100. 100
  101. 101
  102. 102
  103. 103
  104. 104
  105. 105
  106. 106
  107. 107
  108. 108
  109. 109
  110. 110
  111. 111
  112. 112
  113. 113
  114. 114
  115. 115
  116. 116
  117. 117
  118. 118
  119. 119
  120. 120
  121. 121
  122. 122
  123. 123
  124. 124
  125. 125
  126. 126
  127. 127
  128. 128
  129. 129
  130. 130
  131. 131
  132. 132
  133. 133
  134. 134
  135. 135
  136. 136
  137. 137
  138. 138
  139. 139
  140. 140
  141. 141
  142. 142
  143. 143
  144. 144
  145. 145
  146. 146
  147. 147
  148. 148
  149. 149
  150. 150

Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 68 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

Mau akuyamikira Mulungu wa cipulumutso conse

1. Auke Mulungu, abalalike adani ace;Iwonso akumuda athawe pamaso pace.

2. Muwacotse monga utsi ucotseka; Monga phula lisungunuka pamoto,Aonongeke oipa pamaso pa Mulungu.

3. Koma olungama akondwere; atumphe ndi cimwemwe pamaso pa Mulungu;Ndipo asekere naco cikondwerero.

4. Yimbirani Yehova, liyimbireni Nyimbo dzina lace;Undirani mseu Iye woberekekayo kucidikha;Dzina lace ndiye Yehova; ndipo tumphani ndi cimwemwe pamaso pace.

5. Mulungu, mokhala mwace mayera,Ndiye Atate wa ana amasiye, ndi woweruza wa akazi amasiye.

6. Mulungu amangitsira banjaanthu a pa okha;Aturutsa am'ndende alemerere;Koma opikisana naye akhala m'dziko lopanda madzi.

7. Pakuturuka paja, Inu Mulungu, ndi kutsogolera anthu anu,Pakuyenda paja Inu m'cipululu;

8. Dziko lapansi linagwedezeka,Inde thambo linakhapamaso pa Mulungu;Sinai lomwe linagwedezeka pamaso pa Mulungu, Mulungu wa Israyeli.

9. Inu, Mulungu, munabvumbitsa cimvula,Munatsitsimutsa colowa canu pamene cidathodwa.

10. Gulu lanu linakhala m'dziko muja:Mwa ukoma wanu munalikonzera ozunzika, Mulungu.

11. Ambuye anapatsa mau:Akazi akulalikira uthengawo ndiwo khamu lalikuru.

12. Mafumu a magulu a ankhondo athawathawa:Ndipo mkazi amene akhala kwao agawa zofunkha.

13. Pogona inu m'makola a zoweta,Mukhala ngati mapiko a njiwa okulira ndi siliva,Ndi nthenga zace zokulira ndi golidi woyenga wonyezimira.

14. Pamene Wamphamvuyonse anabalalitsa mafumu m'dzikomo,Munayera ngati matalala m'Salimoni.

15. Phiri la Basana ndilo phiri la Mulungu;Phiri la Basana ndilo phiri la mitu mitu.

16. Mucitiranji nsanje mapiri inu a mitu mitu,Ndi phirilo Mulungu analikhumba, akhaleko?Inde, Yehova adzakhalabe komweko kosatha.

17. Magareta a Mulungu ndiwo zikwi makumi awiri, inde zikwi zowirikiza-wirikiza:Ambuye ali pakati pao, monga m'Sinai, m'malo opatulika,

18. Munakwera kumka kumwamba, munapita nao undende kuuyesa ndende;Munalandira zaufulu mwa anthu,Ngakhale mwa opikisana nanu, kuti Yehova Mulungu akakhale nao.

19. Wolemekezeka Ambuye, tsiku ndi tsiku atisenzera katundu,Ndiye Mulungu wa cipulumutso cathu.

20. Mulungu akhala kwa ife Mulungu wa cipulumutso;Ndipo Yehova Ambuye ali nazo zopulumutsira kuimfa.

21. Indedi Mulungu adzaphwanya mutu wa adani ace,Pakati pa mutu pa iye woyendabe m'kutsutsika kwace.

22. Ambuye anati, Ndidzawatenganso ku Basana,Ndidzawatenganso kozama kwa nyanja:

23. Kuti ubviike phazi lako m'mwazi,Kuti malilime a agaru ako alaweko adani ako.

24. Anapenya mayendedwe anu, Mulungu,Mayendedwe a Mulungu wanga, Mfumu yanga, m'malo oyera.

25. Oyimbira anatsogolera, oyimba zoyimba anatsata m'mbuyo,Pakatipo anamwali oyimba mangaka.

26. Lemekezani Mulungu m'masonkhano,Ndiye Ambuye, inu a gwero la Israyeli.

27. Apo pali Benjamini wamng'ono, wakuwacita ufumu,Akuru a Yuda, ndi a upo wao,Akulu a Zebuloni, akulu a Naftali.

28. Mulungu wako analamulira mphamvu yako:Limbitsani, Mulungu, cimene munaticitira.

29. Cifukwa ca Kacisi wanu wa m'YerusalemuMafumu adzabwera naco caufulu kukupatsani.

30. Dzudzulani cirombo ca m'bango,Khamu la mphongo ndi zipfulula za anthu,Yense wakudzigonjera ndi ndarama zasiliva;Anabalalitsa mitundu ya anthu ya kukondwera nayo nkhondo.

31. Akulu adzafumira ku Aigupto;Kushi adzafulumira kutambalitsa manja ace kwa Mulungu.

32. Yimbirani Mulungu, maufumu a dziko lapansi inu;Yimbirani Ambuye zomlemekeza;

33. Kwa Iye wakuberekeka pamwambamwamba, oyambira kale lomwe;Taonani; amveketsa liu lace, ndilo liu lamphamvu.

34. Bvomerezani kuti mphamvu nja Mulungu;Ukulu wace uli pa Israyeli,Ndi mphamvu yace m'mitambo.

35. Inu Mulungu, ndinu woopsa m'malo oyera anu;Mulungu wa Israyeli ndiye amene apatsa anthu ace mphamvu ndi cilimbiko.Alemekezeke Mulungu.