Mitu

  1. 1
  2. 2
  3. 3
  4. 4
  5. 5
  6. 6
  7. 7
  8. 8
  9. 9
  10. 10
  11. 11
  12. 12
  13. 13
  14. 14
  15. 15
  16. 16
  17. 17
  18. 18
  19. 19
  20. 20
  21. 21
  22. 22
  23. 23
  24. 24
  25. 25
  26. 26
  27. 27
  28. 28
  29. 29
  30. 30
  31. 31
  32. 32
  33. 33
  34. 34
  35. 35
  36. 36
  37. 37
  38. 38
  39. 39
  40. 40
  41. 41
  42. 42
  43. 43
  44. 44
  45. 45
  46. 46
  47. 47
  48. 48
  49. 49
  50. 50
  51. 51
  52. 52
  53. 53
  54. 54
  55. 55
  56. 56
  57. 57
  58. 58
  59. 59
  60. 60
  61. 61
  62. 62
  63. 63
  64. 64
  65. 65
  66. 66
  67. 67
  68. 68
  69. 69
  70. 70
  71. 71
  72. 72
  73. 73
  74. 74
  75. 75
  76. 76
  77. 77
  78. 78
  79. 79
  80. 80
  81. 81
  82. 82
  83. 83
  84. 84
  85. 85
  86. 86
  87. 87
  88. 88
  89. 89
  90. 90
  91. 91
  92. 92
  93. 93
  94. 94
  95. 95
  96. 96
  97. 97
  98. 98
  99. 99
  100. 100
  101. 101
  102. 102
  103. 103
  104. 104
  105. 105
  106. 106
  107. 107
  108. 108
  109. 109
  110. 110
  111. 111
  112. 112
  113. 113
  114. 114
  115. 115
  116. 116
  117. 117
  118. 118
  119. 119
  120. 120
  121. 121
  122. 122
  123. 123
  124. 124
  125. 125
  126. 126
  127. 127
  128. 128
  129. 129
  130. 130
  131. 131
  132. 132
  133. 133
  134. 134
  135. 135
  136. 136
  137. 137
  138. 138
  139. 139
  140. 140
  141. 141
  142. 142
  143. 143
  144. 144
  145. 145
  146. 146
  147. 147
  148. 148
  149. 149
  150. 150

Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 49 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

Za pansi pano nza cabe

Kwa Mkulu wa Nyimbo; Salmo la ana a Kora.

1. Dzamveni kuno, anthu inu nonse;Cherani khutu, inu nonse amakono,

2. Awamba ndi omveka omwe,Acuma ndi aumphawi omwe.

3. Pakamwa panga padzanena zanzeru;Ndipo cilingiriro ca mtima wanga cidzakhala ca cidziwitso.

4. Ndidzachera khutu kufanizo:Ndidzafotokozera cophiphiritsa canga poyimbira.

5. Ndidzaoperanji masiku oipa,Pondizinga amphulupulu onditsata kucidendene?

6. Iwo akutama kulemera kwao;Nadzitamandira pa kucuruka kwa cuma cao;

7. Kuombola mbale sangadzamuombole,Kapena kumperekera dipo kwa Mulungu:

8. (Popeza ciombolo ca moyo wao nca mtengo wace wapatali,Ndipo cilekeke nthawi zonse)

9. Kuti akhale ndi moyo osafa,Osaona cibvundi.

10. Pakuti aona anzeru amafa,Monga aonongekera wopusa, wodyerera momwemo,Nasiyira ena cuma cao.

11. Mumtima mwao ayesa kuti nyumba zao zikhala cikhalire,Ndi mokhala iwo ku mibadwo mibadwo;Achapo dzina lao padziko pao.

12. Koma munthu wa ulemu wace sakhalitsa:Afanana ndi nyama za kuthengo, afanana nazo.

13. Njira yao yino ndiyo kupusa kwao:Koma akudza m'mbuyo abvomereza mau ao.

14. Aikidwa m'manda ngati nkhosa;Mbusa wao ndi imfa:Ndipo m'mawa mwace oongoka mtima adzakhala mafumu ao;Ndipo maonekedwe ao adzanyekera kumanda, kuti pokhala pace padzasowa.

15. Koma Mulungu adzaombola moyo wanga ku mphamvu ya manda:Pakuti adzandilandira ine.

16. Usaope polemezedwa munthu,Pocuruka ulemu wa nyumba yace;

17. Pakuti pomwalira iye sadzamuka nako kanthu kali konse;Ulemu wace sutsika naye kumtsata m'mbuyo.

18. Angakhale anadalitsa moyo wace pokhala ndi moyo,Ndipo anthu akulemekeza iwe, podzicitira wekha zokoma,

19. Adzamuka ku mbadwo wa makolo ace;Sadzaona kuunika nthawi zonse.

20. Munthu waulemu, koma wosadziwitsa,Afanana ndi nyama za kuthengo, afanana nazo.