Mitu

  1. 1
  2. 2
  3. 3
  4. 4
  5. 5
  6. 6
  7. 7
  8. 8
  9. 9
  10. 10
  11. 11
  12. 12
  13. 13
  14. 14
  15. 15
  16. 16
  17. 17
  18. 18
  19. 19
  20. 20
  21. 21
  22. 22
  23. 23
  24. 24
  25. 25
  26. 26
  27. 27
  28. 28
  29. 29
  30. 30
  31. 31
  32. 32
  33. 33
  34. 34
  35. 35
  36. 36
  37. 37
  38. 38
  39. 39
  40. 40
  41. 41
  42. 42
  43. 43
  44. 44
  45. 45
  46. 46
  47. 47
  48. 48
  49. 49
  50. 50
  51. 51
  52. 52
  53. 53
  54. 54
  55. 55
  56. 56
  57. 57
  58. 58
  59. 59
  60. 60
  61. 61
  62. 62
  63. 63
  64. 64
  65. 65
  66. 66
  67. 67
  68. 68
  69. 69
  70. 70
  71. 71
  72. 72
  73. 73
  74. 74
  75. 75
  76. 76
  77. 77
  78. 78
  79. 79
  80. 80
  81. 81
  82. 82
  83. 83
  84. 84
  85. 85
  86. 86
  87. 87
  88. 88
  89. 89
  90. 90
  91. 91
  92. 92
  93. 93
  94. 94
  95. 95
  96. 96
  97. 97
  98. 98
  99. 99
  100. 100
  101. 101
  102. 102
  103. 103
  104. 104
  105. 105
  106. 106
  107. 107
  108. 108
  109. 109
  110. 110
  111. 111
  112. 112
  113. 113
  114. 114
  115. 115
  116. 116
  117. 117
  118. 118
  119. 119
  120. 120
  121. 121
  122. 122
  123. 123
  124. 124
  125. 125
  126. 126
  127. 127
  128. 128
  129. 129
  130. 130
  131. 131
  132. 132
  133. 133
  134. 134
  135. 135
  136. 136
  137. 137
  138. 138
  139. 139
  140. 140
  141. 141
  142. 142
  143. 143
  144. 144
  145. 145
  146. 146
  147. 147
  148. 148
  149. 149
  150. 150

Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 139 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

Mulungu ali ponse ponse, adziwa zonse

Kwa Mkulu wa Nsembe. Salmo la Davide.

1. Munandisanthula, Yehova, nimundidziwa.

2. Inumudziwakukhalakwangandi kuuka kwanga,Muzindikira lingaliro langa muli kutali.

3. Muyesa popita ine ndi pogona ine,Ndi njira zanga zonse muzolowerana nazo.

4. Pakuti asanafike mau pa lilime langa,Taonani, Yehova, muwadziwa onse.

5. Munandizinga kumbuyo ndi kumaso,Nimunaika dzanja lanu pa ine.

6. Kudziwa ici kundilaka ndi kundidabwiza:Kundikhalira patali, sindifikirako.

7. Ndidzapita kuti kuzembera mzimu wanu?Kapena ndidzathawira kuti kuzembera nkhope yanu?

8. Ndikakwera kumka kumwamba, muli komweko;Kapena ndikadziyalira ku Gehena, taonani, muli komweko.

9. Ndikadzitengera mapiko a mbanda kuca,Ndi kukhala ku malekezero a nyanja;

10. Kungakhale komweko dzanja lanu lidzanditsogolera,Nilidzandigwira dzanja lanu lamanja.

11. Ndipo ndikati, Koma mdima undiphimbe,Ndi kuunika kondizinga kukhale usiku:

12. Ungakhale mdima sudetsa pamaso panu,Koma usiku uwala ngati usana:Mdima ukunga kuunika.

13. Pakuti Inu munalenga imso zanga;Munandiumba ndisanabadwe ine.

14. Ndikuyamikani cifukwa kuti cipangidwe canga ncoopsa ndi codabwiza;Nchito zanu nzodabwiza;Moyo wanga ucidziwa ici bwino ndithu.

15. Thupi langa silinabisikira Inu popangidwa ine mobisika,Poombedwa ine monga m'munsi mwace mwa dziko lapansi.

16. Ndisanaumbidwe ine maso anu anandipenya,Ziwalo zanga zonse zinalembedwa m'buku mwanu,Masiku akuti ziumbidwe, Pakalibe cimodzi ca izo.

17. Potero, Mulungu, ndiziyesa zolingalira zanu za mtengo wace ndithu!Mawerengedwe ace ndi ambirimbiri!

18. Ndikaziwerenga zicuruka koposa mcenga:Ndikauka ndikhalanso nanu.

19. Indedi, mudzaomba woipa, Mulungu:Ndipo amuna inu nkhumba mwazi, cokani kwa ine.

20. Popeza anena za Inu moipa,Ndi adani anu achula dzina lanu mwacabe.

21. Kodi sindidana nao iwo akudana ndi Inu, Yehova?Ndipo kodi sindimva nao cisoni iwo akuukira Inu?

22. Ndidana nao ndi udani weni weni:Ndiwayesa adani.

23. Mundisanthule, Mulungu, nimudziwe mtima wanga;Mundiyese nimudziwe zolingalira zanga.

24. Ndipo mupenye ngati ndiri nao mayendedwe oipa,Nimunditsogolere pa njira yosatha.