Mitu

  1. 1
  2. 2
  3. 3
  4. 4
  5. 5
  6. 6
  7. 7
  8. 8
  9. 9
  10. 10
  11. 11
  12. 12
  13. 13
  14. 14
  15. 15
  16. 16
  17. 17
  18. 18
  19. 19
  20. 20
  21. 21
  22. 22
  23. 23
  24. 24
  25. 25
  26. 26
  27. 27
  28. 28
  29. 29
  30. 30
  31. 31
  32. 32
  33. 33
  34. 34
  35. 35
  36. 36
  37. 37
  38. 38
  39. 39
  40. 40
  41. 41
  42. 42
  43. 43
  44. 44
  45. 45
  46. 46
  47. 47
  48. 48
  49. 49
  50. 50
  51. 51
  52. 52
  53. 53
  54. 54
  55. 55
  56. 56
  57. 57
  58. 58
  59. 59
  60. 60
  61. 61
  62. 62
  63. 63
  64. 64
  65. 65
  66. 66
  67. 67
  68. 68
  69. 69
  70. 70
  71. 71
  72. 72
  73. 73
  74. 74
  75. 75
  76. 76
  77. 77
  78. 78
  79. 79
  80. 80
  81. 81
  82. 82
  83. 83
  84. 84
  85. 85
  86. 86
  87. 87
  88. 88
  89. 89
  90. 90
  91. 91
  92. 92
  93. 93
  94. 94
  95. 95
  96. 96
  97. 97
  98. 98
  99. 99
  100. 100
  101. 101
  102. 102
  103. 103
  104. 104
  105. 105
  106. 106
  107. 107
  108. 108
  109. 109
  110. 110
  111. 111
  112. 112
  113. 113
  114. 114
  115. 115
  116. 116
  117. 117
  118. 118
  119. 119
  120. 120
  121. 121
  122. 122
  123. 123
  124. 124
  125. 125
  126. 126
  127. 127
  128. 128
  129. 129
  130. 130
  131. 131
  132. 132
  133. 133
  134. 134
  135. 135
  136. 136
  137. 137
  138. 138
  139. 139
  140. 140
  141. 141
  142. 142
  143. 143
  144. 144
  145. 145
  146. 146
  147. 147
  148. 148
  149. 149
  150. 150

Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 42 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

Mtima wolira kuyanjana ndi Mulungu m'Kacisi

Kwa Mkulu wa Nyimbo. Cilangizo ca kwa ana a Kora.

1. Monga nswala ipuma wefuwefu kukhumba mitsinje;Motero moyo wanga upuma wefuwefu kukhumba Inu, Mulungu.

2. Moyo wanga uli ndi ludzu la kwa Mulungu, la kwa Mulungu wamoyo:Ndikadze liti kuoneka pamaso pa Mulungu?

3. Misozi yanga yakhalangati cakudya canga,Usana ndi usiku;Pakunena iwo kwa ine dzuwa lonse,Mulungu wako ali kuti?

4. Ndizikumbukila izi ndipo nditsanulira moyo wanga m'kati mwa ine,Pakuti ndidafopita ndi unyinji wa anthu,Ndinawatsogolera ku nyumba ya Mulungu, ndi mau akuyimbitsa ndi kuyamika,Ndi unyinji wakusunga dzuwa lokondwera.

5. Udziweramiranji moyo wanga iwe?Ndi kuzingwa m'kati mwanga?Yembekeza Mulungu, pakuti ndidzamyamikansoCifukwa ca cipulumutso ca nkhope yace.

6. Mulungu wanga, moyo wangaUdziweramira m'kati mwanga;Cifukwa cace ndikumbukila Inu m'dziko la Yordano,Ndi mu Ahermone, m'kaphiri ka Mizara.

7. Madzi akuya aitanizana ndi madzi akuya,Pa mkokomo wa matiti anu: Mafunde onse a nyondonyondo anandimiza ine.

8. Koma usana Yehova adzalamulira cifundo cace,Ndipo usiku Nyimbo yace idzakhala ndi ine.Inde pemphero la kwa Yehova wa moyowanga.

9. Ndidzati kwa Mulungu, thanthwe langa, mwandiiwala cifukwa ninji?Ndimayenderanji wakulira Cifukwa ca kundipsinja mdaniyo?

10. Adani anga andinyoza ndi kundityola mafupa anga;Pakunena ndine dzuwa lonse,Mulungu wako ali kuti?

11. Udziweramiranji moyo wanga iwe?Ndi kuzingwa m'kati mwanga?Yembekeza Mulungu: pakuti ndidzamlemekeza tsopanonso,Ndiye cipulumutso ca nkhope yanga ndi Mulungu wanga,