Mitu

  1. 1
  2. 2
  3. 3
  4. 4
  5. 5
  6. 6
  7. 7
  8. 8
  9. 9
  10. 10
  11. 11
  12. 12
  13. 13
  14. 14
  15. 15
  16. 16
  17. 17
  18. 18
  19. 19
  20. 20
  21. 21
  22. 22
  23. 23
  24. 24
  25. 25
  26. 26
  27. 27
  28. 28
  29. 29
  30. 30
  31. 31
  32. 32
  33. 33
  34. 34
  35. 35
  36. 36
  37. 37
  38. 38
  39. 39
  40. 40
  41. 41
  42. 42
  43. 43
  44. 44
  45. 45
  46. 46
  47. 47
  48. 48
  49. 49
  50. 50
  51. 51
  52. 52
  53. 53
  54. 54
  55. 55
  56. 56
  57. 57
  58. 58
  59. 59
  60. 60
  61. 61
  62. 62
  63. 63
  64. 64
  65. 65
  66. 66
  67. 67
  68. 68
  69. 69
  70. 70
  71. 71
  72. 72
  73. 73
  74. 74
  75. 75
  76. 76
  77. 77
  78. 78
  79. 79
  80. 80
  81. 81
  82. 82
  83. 83
  84. 84
  85. 85
  86. 86
  87. 87
  88. 88
  89. 89
  90. 90
  91. 91
  92. 92
  93. 93
  94. 94
  95. 95
  96. 96
  97. 97
  98. 98
  99. 99
  100. 100
  101. 101
  102. 102
  103. 103
  104. 104
  105. 105
  106. 106
  107. 107
  108. 108
  109. 109
  110. 110
  111. 111
  112. 112
  113. 113
  114. 114
  115. 115
  116. 116
  117. 117
  118. 118
  119. 119
  120. 120
  121. 121
  122. 122
  123. 123
  124. 124
  125. 125
  126. 126
  127. 127
  128. 128
  129. 129
  130. 130
  131. 131
  132. 132
  133. 133
  134. 134
  135. 135
  136. 136
  137. 137
  138. 138
  139. 139
  140. 140
  141. 141
  142. 142
  143. 143
  144. 144
  145. 145
  146. 146
  147. 147
  148. 148
  149. 149
  150. 150

Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 90 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

Mulungu ndiye wacikhalire, munthu ndiye wakutha msanga

Pemphero la Mose munthu wa Mulungu.

1. Ambuye, Inu munatikhalira mokhalamoM'mibadwo mibadwo.

2. Asanabadwe mapiri,Kapena musanalenge dziko lapansi, ndi lokhalamo anthu,Inde, kuyambira nthawi yosayamba kufikira nthawi yosatha,Inu ndinu Mulungu.

3. Mubweza munthu akhale pfumbi;Nimuti, Bwererani inu, ana a anthu.

4. Pakuti pamaso panu zaka zikwiZikhala ngati dzulo, litapita,Ndi monga ulonda wa usiku.

5. Muwatenga ngati ndi madzi akulu, akhala ngati tulo;Mamawa akhala ngati msipu waphuka.

6. Mamawa uphuka bwino;Madzulo ausenga, nuuma.

7. Pakuti tionongeka mu mkwiyo wanu;Ndipo m'kuzaza kwanu tiopsedwa.

8. Munaika mphulupulu zathu pamaso panu,Ndi zoipa zathu zobisika pounikira nkhope yanu.

9. Pakuti masiku athu onse apitirira m'ukali wanu;Titsiriza moyo wathu ngati lingaliro.

10. Masiku a zaka zathu ndiwo zaka makumi asanu ndi awiri,Kapena tikakhala nayo mphamvudi zaka makumi asanu ndi atatu;Koma teronso kukula kwao kumati cibvuto ndi copanda pace;Pakuti kumapitako msanga ndipo tithawa ife tomwe.

11. Adziwa mphamvu ya mkwiyo wanu ndani,Ndi ukali wanu monga ayenera kukuopani?

12. Mutidziwitse kuwerenga masiku athu motero,Kuti tikhale nao mtima wanzeru.

13. Bwerani, Yehova; kufikira liti?Ndipo alekeni atumiki anu.

14. Mutikhutitse naco cifundo canu m'mawa;Ndipo tidzapfuula mokondwera ndi kukondwera masiku athu onse.

15. Tikondweretseni monga mwa masiku mudatizunzawa,Ndi zaka tidaona coipa.

16. Cocita Inu cioneke kwa atumiki anu,Ndi ulemerero wanu pa ana ao.

17. Ndipo cisomo cace ca Yehova Mulungu wathu cikhale pa ife;Ndipo mutikhazikitsire ife nchito ya manja athu;Inde, nchito ya manja athu muikhazikitse.