Mitu

  1. 1
  2. 2
  3. 3
  4. 4
  5. 5
  6. 6
  7. 7
  8. 8
  9. 9
  10. 10
  11. 11
  12. 12
  13. 13
  14. 14
  15. 15
  16. 16
  17. 17
  18. 18
  19. 19
  20. 20
  21. 21
  22. 22
  23. 23
  24. 24
  25. 25
  26. 26
  27. 27
  28. 28
  29. 29
  30. 30
  31. 31
  32. 32
  33. 33
  34. 34
  35. 35
  36. 36
  37. 37
  38. 38
  39. 39
  40. 40
  41. 41
  42. 42
  43. 43
  44. 44
  45. 45
  46. 46
  47. 47
  48. 48
  49. 49
  50. 50
  51. 51
  52. 52
  53. 53
  54. 54
  55. 55
  56. 56
  57. 57
  58. 58
  59. 59
  60. 60
  61. 61
  62. 62
  63. 63
  64. 64
  65. 65
  66. 66
  67. 67
  68. 68
  69. 69
  70. 70
  71. 71
  72. 72
  73. 73
  74. 74
  75. 75
  76. 76
  77. 77
  78. 78
  79. 79
  80. 80
  81. 81
  82. 82
  83. 83
  84. 84
  85. 85
  86. 86
  87. 87
  88. 88
  89. 89
  90. 90
  91. 91
  92. 92
  93. 93
  94. 94
  95. 95
  96. 96
  97. 97
  98. 98
  99. 99
  100. 100
  101. 101
  102. 102
  103. 103
  104. 104
  105. 105
  106. 106
  107. 107
  108. 108
  109. 109
  110. 110
  111. 111
  112. 112
  113. 113
  114. 114
  115. 115
  116. 116
  117. 117
  118. 118
  119. 119
  120. 120
  121. 121
  122. 122
  123. 123
  124. 124
  125. 125
  126. 126
  127. 127
  128. 128
  129. 129
  130. 130
  131. 131
  132. 132
  133. 133
  134. 134
  135. 135
  136. 136
  137. 137
  138. 138
  139. 139
  140. 140
  141. 141
  142. 142
  143. 143
  144. 144
  145. 145
  146. 146
  147. 147
  148. 148
  149. 149
  150. 150

Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 39 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

Kupepuka kwa moyo uno

Kwa Mkulu wa Nyimbo, kwa Yedutun, Salmo la Davide.

1. Ndinati, Ndidzasunga njira zanga,Kuti ndingacimwe ndi lilime langa:Ndidzasunga pakamwa panga ndi cam'kamwa,Pokhala woipa ali pamaso panga.

2. Ndinatonthola osanena mau, ndinakhala cete osalawa cokoma;Ndipo cisoni canga cinabuka.

3. Mtima wanga unatentha m'kati mwaine;Unayaka moto pakulingirira ine:Pamenepo ndinalankhula ndi lilime langa:

4. Yehova, mundidziwitse cimariziro canga,Ndi mawerengedwe a masiku anga ndi angati;Ndidziwe malekezero anga,

5. Onani, munaika masiku anga akhale monga kuyesa dzanja;Ndipo zaka zanga ziri ngati cabe pamaso panu:Indedi munthu ali yense angakhale wokhazikika, ali cabe konse.

6. Indedi munthu ayenda ngati mthunzi:Indedi abvutika cabe:Asonkhanitsa cuma, ndipo sadziwa adzacilandira ndani?

7. Ndipo tsopano, Ambuye, ndilindira ciani?Ciyembekezo canga ciri pa Inu.

8. Ndipulumutseni kwa zolakwa zangazonse:Musandiike ndikhale cotonza ca wopusa.

9. Ndinakhala du, sindinatsegula pakamwa panga;Cifukwa inu mudacicita.

10. Mundicotsere cobvutitsa canu;Pandithera ine cifukwa ca kulanga kwa dzanja lanu.

11. Pamene mulanga munthu ndi zomdzudzula cifukwa ca mphulupulu,Mukanganula kukongola kwace monga mumacita ndi kadzoce:Indedi, munthu ali yense ali cabe.

12. Imvani pemphero langa, Yehova, ndipo cherani khutu kulira kwanga;Musakhale cete pa misozi yanga:Pakuti ine ndine mlendo ndi Inu,Wosakhazikika, monga makolo anga onse.

13. Ndiloleni, kuti nditsitsimuke,Ndisanamuke ndi kukhala kuli zi.