Mitu

  1. 1
  2. 2
  3. 3
  4. 4
  5. 5
  6. 6
  7. 7
  8. 8
  9. 9
  10. 10
  11. 11
  12. 12
  13. 13
  14. 14
  15. 15
  16. 16
  17. 17
  18. 18
  19. 19
  20. 20
  21. 21
  22. 22
  23. 23
  24. 24
  25. 25
  26. 26
  27. 27
  28. 28
  29. 29
  30. 30
  31. 31
  32. 32
  33. 33
  34. 34
  35. 35
  36. 36
  37. 37
  38. 38
  39. 39
  40. 40
  41. 41
  42. 42
  43. 43
  44. 44
  45. 45
  46. 46
  47. 47
  48. 48
  49. 49
  50. 50
  51. 51
  52. 52
  53. 53
  54. 54
  55. 55
  56. 56
  57. 57
  58. 58
  59. 59
  60. 60
  61. 61
  62. 62
  63. 63
  64. 64
  65. 65
  66. 66
  67. 67
  68. 68
  69. 69
  70. 70
  71. 71
  72. 72
  73. 73
  74. 74
  75. 75
  76. 76
  77. 77
  78. 78
  79. 79
  80. 80
  81. 81
  82. 82
  83. 83
  84. 84
  85. 85
  86. 86
  87. 87
  88. 88
  89. 89
  90. 90
  91. 91
  92. 92
  93. 93
  94. 94
  95. 95
  96. 96
  97. 97
  98. 98
  99. 99
  100. 100
  101. 101
  102. 102
  103. 103
  104. 104
  105. 105
  106. 106
  107. 107
  108. 108
  109. 109
  110. 110
  111. 111
  112. 112
  113. 113
  114. 114
  115. 115
  116. 116
  117. 117
  118. 118
  119. 119
  120. 120
  121. 121
  122. 122
  123. 123
  124. 124
  125. 125
  126. 126
  127. 127
  128. 128
  129. 129
  130. 130
  131. 131
  132. 132
  133. 133
  134. 134
  135. 135
  136. 136
  137. 137
  138. 138
  139. 139
  140. 140
  141. 141
  142. 142
  143. 143
  144. 144
  145. 145
  146. 146
  147. 147
  148. 148
  149. 149
  150. 150

Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 41 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

Mulungu adalitsa wosamalira osauka. Adani ndi mabwenzi amcitira Davide zoipa, Mulungu amlanditse

Kwa Mkulu wa Nyimbo. Salmo la Davide.

1. Wodala iye amene asamalira wosauka:Tsiku la tsoka Yehova adzampulumutsa:

2. Yehova adzamsunga, nadzamsunga ndi moyo, ndipo adzadalitsika pa dziko lapansi;Ndipo musampereke ku cifuniro ca adani ace.

3. Yehova adzamgwiriziza pa kama wodwalira;Podwala iye mukonza pogona pace,

4. Ndinati ine, Mundicitire cifundo, Yehova:Ciritsani mtima wanga; pakuti ndacimwira Inu.

5. Adani anga andinenera coipa, ndi kuti,Adzafa liti, ndi kutayika dzina lace?

6. Ndipo akadza kundiona wina angonena bodza;Mumtima mwace adzisonkhera zopanda pace:Akamka nayenda namakanena:

7. Onse akudana nane andinong'onezerana;Apangana condiipsa ine.

8. Camgwera cinthu coopsa, ati;Popeza ali gonire sadzaukanso.

9. Ngakhale bwenzi langa leni leni, amene ndamkhulupirira, ndiye amene adadyako mkate wanga,Anandikwezera cidendene cace.

10. Koma Inu, Yehova, mundicitire cifundo, ndipo mundiutse,Kuti ndiwabwezere.

11. Umo ndidziwa kuti mukondwera ndi ine,Popeza mdani wanga sandiseka.

12. Ndipo ine, mundigwirizize m'ungwiro wanga,Ndipo mundiike pankhope panu ku nthawi yamuyaya.

13. Wodalitsika Yehova, Mulungu wa Israyeli,Kucokera nthawi yosayamba kufikira nthawi yosatha.Amen, ndi Amen.