Mitu

  1. 1
  2. 2
  3. 3
  4. 4
  5. 5
  6. 6
  7. 7
  8. 8
  9. 9
  10. 10
  11. 11
  12. 12
  13. 13
  14. 14
  15. 15
  16. 16
  17. 17
  18. 18
  19. 19
  20. 20
  21. 21
  22. 22
  23. 23
  24. 24
  25. 25
  26. 26
  27. 27
  28. 28
  29. 29
  30. 30
  31. 31
  32. 32
  33. 33
  34. 34
  35. 35
  36. 36
  37. 37
  38. 38
  39. 39
  40. 40
  41. 41
  42. 42
  43. 43
  44. 44
  45. 45
  46. 46
  47. 47
  48. 48
  49. 49
  50. 50
  51. 51
  52. 52
  53. 53
  54. 54
  55. 55
  56. 56
  57. 57
  58. 58
  59. 59
  60. 60
  61. 61
  62. 62
  63. 63
  64. 64
  65. 65
  66. 66
  67. 67
  68. 68
  69. 69
  70. 70
  71. 71
  72. 72
  73. 73
  74. 74
  75. 75
  76. 76
  77. 77
  78. 78
  79. 79
  80. 80
  81. 81
  82. 82
  83. 83
  84. 84
  85. 85
  86. 86
  87. 87
  88. 88
  89. 89
  90. 90
  91. 91
  92. 92
  93. 93
  94. 94
  95. 95
  96. 96
  97. 97
  98. 98
  99. 99
  100. 100
  101. 101
  102. 102
  103. 103
  104. 104
  105. 105
  106. 106
  107. 107
  108. 108
  109. 109
  110. 110
  111. 111
  112. 112
  113. 113
  114. 114
  115. 115
  116. 116
  117. 117
  118. 118
  119. 119
  120. 120
  121. 121
  122. 122
  123. 123
  124. 124
  125. 125
  126. 126
  127. 127
  128. 128
  129. 129
  130. 130
  131. 131
  132. 132
  133. 133
  134. 134
  135. 135
  136. 136
  137. 137
  138. 138
  139. 139
  140. 140
  141. 141
  142. 142
  143. 143
  144. 144
  145. 145
  146. 146
  147. 147
  148. 148
  149. 149
  150. 150

Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 143 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

Davide apempha Mulungu amlanditse msanga kwa adani ace

Salmo la Davide.

1. Imvani pemphero langa, Yehova; ndicherere khutu kupemba kwanga;Ndiyankheni mwa cikhulupiriko canu, mwa cilungamo canu.

2. Ndipo musaitane mlandu wa mtumiki wanu;Pakuti pamaso panu sipadzakhala wolungama wamoyo mmodzi yense.

3. Pakuti mdani alondola moyo wanga;Apondereza pansr moyo wanga;Andikhalitsa mumdima monga iwo adafa kale lomwe.

4. Potero mzimu wanga wakomoka mwa ine;Mtima wanga utenga nkhawa m'kati mwanga,

5. Ndikumbukila masiku a kale lomwe;Zija mudazicita ndilingirirapo;Ndikamba pa ndekha za nchito ya manja anu.

6. Nditambalitsira manja anga kwa Inu:Moyo wanga ulira Inu monga dziko lolira mvula.

7. Fulumirani ndiyankheni, Yehova; mzimu wanga ukutha.Musandibisire nkhope yanu;Ndingafanane nao akutsikira kudzenje.

8. Mundimvetse cifundo canu mamawa;Popeza ndikhulupirira Inu:Mundidziwitse njira ndiyendemo;Popeza ndikweza moyo wanga kwa Inu.

9. Mundilanditse kwa adani anga, Yehova;Ndibisala mwa Inu.

10. Mundiphunzitse cokonda Inu; popeza Inu ndinu Mulungu wanga;Mzimu wanu ndi wokoma; munditsogolere kucidikha.

11. Mundipatse moyo, Yehova, cifukwa ca dzina lanu;Mwa cilungamo canu muturutse moyo wanga m'nsautso.

12. Ndipo mwa cifundo canu mundidulire adani anga,Ndipo muononge onse akusautsa moyo wanga;Pakuti ine ndine mtumiki wanu.