1. Yehova ndiye mbusa wanga; sindidzasowa.
2. Andigonetsa ku busa lamsipu:Anditsogolera ku madzi ndikha.
3. Atsitsimutsa moyo wanga;Anditsogolera m'mabande a cilungamo, cifukwa ca dzina lace.
4. Inde, ndingakhale ndiyenda m'cigwa ca mthunzi wa Imfa,Sindidzaopa coipa; pakuti Inu muli ndi ine:Cibonga canu ndi ndodo yanu, izi zindisangalatsa ine,
5. Mundiyalikira gome pamaso panga m'kuona kwa adani anga:Mwandidzoza mutu wanga mafuta; cikho canga cisefuka.
6. Inde ukoma ndi cifundo zidzanditsata masiku onse a moyo wanga:Ndipo ndidzakhala m'nyumba ya Yehova masiku onse.