Mitu

  1. 1
  2. 2
  3. 3
  4. 4
  5. 5
  6. 6
  7. 7
  8. 8
  9. 9
  10. 10
  11. 11
  12. 12
  13. 13
  14. 14
  15. 15
  16. 16
  17. 17
  18. 18
  19. 19
  20. 20
  21. 21
  22. 22
  23. 23
  24. 24
  25. 25
  26. 26
  27. 27
  28. 28
  29. 29
  30. 30
  31. 31
  32. 32
  33. 33
  34. 34
  35. 35
  36. 36
  37. 37
  38. 38
  39. 39
  40. 40
  41. 41
  42. 42
  43. 43
  44. 44
  45. 45
  46. 46
  47. 47
  48. 48
  49. 49
  50. 50
  51. 51
  52. 52
  53. 53
  54. 54
  55. 55
  56. 56
  57. 57
  58. 58
  59. 59
  60. 60
  61. 61
  62. 62
  63. 63
  64. 64
  65. 65
  66. 66
  67. 67
  68. 68
  69. 69
  70. 70
  71. 71
  72. 72
  73. 73
  74. 74
  75. 75
  76. 76
  77. 77
  78. 78
  79. 79
  80. 80
  81. 81
  82. 82
  83. 83
  84. 84
  85. 85
  86. 86
  87. 87
  88. 88
  89. 89
  90. 90
  91. 91
  92. 92
  93. 93
  94. 94
  95. 95
  96. 96
  97. 97
  98. 98
  99. 99
  100. 100
  101. 101
  102. 102
  103. 103
  104. 104
  105. 105
  106. 106
  107. 107
  108. 108
  109. 109
  110. 110
  111. 111
  112. 112
  113. 113
  114. 114
  115. 115
  116. 116
  117. 117
  118. 118
  119. 119
  120. 120
  121. 121
  122. 122
  123. 123
  124. 124
  125. 125
  126. 126
  127. 127
  128. 128
  129. 129
  130. 130
  131. 131
  132. 132
  133. 133
  134. 134
  135. 135
  136. 136
  137. 137
  138. 138
  139. 139
  140. 140
  141. 141
  142. 142
  143. 143
  144. 144
  145. 145
  146. 146
  147. 147
  148. 148
  149. 149
  150. 150

Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 50 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

Mulungu woweruza wa dziko lapansi

Salmo la Asafu.

1. Mulungu wa milungu, Yehova, wanena,Aitana dziko lapansi kuyambira kuturuka kwa dzuwa kufikira kulowa kwace.

2. Mulungu awalira m'Ziyoni, mokongola mwangwiro.

3. Adzafika Mulungu wathu, ndipo sadzakhala cete:Moto udzanyeka pankhope pace,Ndipo pozungulira pace padzasokosera kwakukuru.

4. Kumwamba adzaitana zakumwamba,Ndi dziko lapansi, kuti aweruze anthu ace:

5. Mundisonkhanitsire okondedwa anga;Amene anapangana ndi Ine ndi nsembe.

6. Ndipo zakumwamba zionetsera cilungamo cace;Pakuti Mulungu mwini wace ndiye woweruza.

7. Imvani, anthu anga, ndipo ndidzanena;Israyeli, ndipo ndidzacita mboni pa iwe:Ine Mulungu, ndine Mulungu wako.

8. Sindikudzudzula iwe cifukwa ca nsembe zako;Popeza nsembe zako zopsereza ziri pamaso panga cikhalire.

9. Sindidzatenga ng'ombe m'nyumbamwako,Kapena mbuzi m'makola mwako.

10. Pakuti zamoyo zonse za kuthengo ndi zanga,Ndi ng'ombe za pa mapiri zikwi.

11. Ndidziwa mbalame zonse za m'mapiri:Ndipo nyama za kuthengo ziri ndi Ine.

12. Ndikamva njala, sindidzakuuza:Pakuti dziko lonse ndi langa, ndi kudzala kwace komwe.

13. Kodi ndidzadya nyama ya ng'ombe,Kapena kumwa mwazi wa mbuzi?

14. Pereka kwa Mulungu nsembe yaciyamiko;Numcitire Wam'mwambamwamba cowinda cako:

15. Ndipo undiitane tsiku la cisautso:Ndidzakulanditsa, ndipo iwe udzandilemekeza.

16. Koma kwa woipa Mulungu anena,Uli nao ciani malemba anga kulalikira,Ndi kuchula pangano langa pakamwa pako?

17. Popeza udana naco cilangizo,Nufulatira mau anga.

18. Pakuona mbala, ubvomerezana nayo,Nucita nao acigololo.

19. Pakamwa pako mpocita zocimwa,Ndipo lilime lako likonza cinyengo.

20. Ukhala, nuneneza mbale wako;Usinjirira mwana wa mai wako.

21. Izi unazicita iwe, ndipo ndinakhala cete Ine;Unayesa kuti ndifanana nawe:Ndidzakudzudzula, ndi kucilongosola pamaso pako.

22. Dziwitsani ici inu oiwala Mulungu,Kuti ndingakumwetuleni, ndipo mungasowepo mpulumutsi:

23. Wopereka nsembe yaciyamiko andilemekeza Ine;Ndipo kwa iye wosunga mayendedwe aceNdidzamuonetsa cipulumutso ca Mulungu.