Mitu

  1. 1
  2. 2
  3. 3
  4. 4
  5. 5
  6. 6
  7. 7
  8. 8
  9. 9
  10. 10
  11. 11
  12. 12
  13. 13
  14. 14
  15. 15
  16. 16
  17. 17
  18. 18
  19. 19
  20. 20
  21. 21
  22. 22
  23. 23
  24. 24
  25. 25
  26. 26
  27. 27
  28. 28
  29. 29
  30. 30
  31. 31
  32. 32
  33. 33
  34. 34
  35. 35
  36. 36
  37. 37
  38. 38
  39. 39
  40. 40
  41. 41
  42. 42
  43. 43
  44. 44
  45. 45
  46. 46
  47. 47
  48. 48
  49. 49
  50. 50
  51. 51
  52. 52
  53. 53
  54. 54
  55. 55
  56. 56
  57. 57
  58. 58
  59. 59
  60. 60
  61. 61
  62. 62
  63. 63
  64. 64
  65. 65
  66. 66
  67. 67
  68. 68
  69. 69
  70. 70
  71. 71
  72. 72
  73. 73
  74. 74
  75. 75
  76. 76
  77. 77
  78. 78
  79. 79
  80. 80
  81. 81
  82. 82
  83. 83
  84. 84
  85. 85
  86. 86
  87. 87
  88. 88
  89. 89
  90. 90
  91. 91
  92. 92
  93. 93
  94. 94
  95. 95
  96. 96
  97. 97
  98. 98
  99. 99
  100. 100
  101. 101
  102. 102
  103. 103
  104. 104
  105. 105
  106. 106
  107. 107
  108. 108
  109. 109
  110. 110
  111. 111
  112. 112
  113. 113
  114. 114
  115. 115
  116. 116
  117. 117
  118. 118
  119. 119
  120. 120
  121. 121
  122. 122
  123. 123
  124. 124
  125. 125
  126. 126
  127. 127
  128. 128
  129. 129
  130. 130
  131. 131
  132. 132
  133. 133
  134. 134
  135. 135
  136. 136
  137. 137
  138. 138
  139. 139
  140. 140
  141. 141
  142. 142
  143. 143
  144. 144
  145. 145
  146. 146
  147. 147
  148. 148
  149. 149
  150. 150

Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 118 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

Wa Salmo alemekeza Mulungu womlanditsa m'manja mwa adani

1. Yamikani Yehova; pakuti Iye ndiye wabwino;Pakuti cifundo cace ncosatha.

2. Anene tsono Israyeli,Kuti cifundo cace ncosatha.

3. Anene tsono nyumba ya Aroni,Kuti cifundo cace ncosatha.

4. Anene tsono iwo akuopa Yehova,Kuti cifundo cace ncosatha.

5. M'mene ndinasautsika ndinaitanira pa Yehova;Anandiyankha Dandiika motakasuka Yehova.

6. Yehova ndi wanga; sindidzaopa;Adzandicitanji munthu?

7. Yehova ndi wanga, mwa iwo akundithandiza;M'mwemo ndidzaona cofuna ine pa iwo akundida,

8. Kuthawira kwa Yehova nkokomaKoposa kukhulupirira munthu.

9. Kuthawira kwa Yehova nkokomaKoposa kukhulupirira akulu,

10. Amitundu onse adandizinga,Zedi, m'dzina la Yehova ndidzawaduladula.

11. Adandizinga, inde, adandizinga:Indedi, m'dzinala Yehova ndidzawaduladula.

12. Adandizinga ngati njuci;Anazima ngati moto waminga;Indedi, m'dzina la Yehova ndidzawaduladula.

13. Kundikankha anandikankha ndikadagwa;Koma Yehova anandithandiza.

14. Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga;Ndipo anakhala cipulumutso canga.

15. M'mahema a olungama muli liu lakupfuula mokondwera ndi la cipulumutso:

16. Dzanja lamanja la Yehova licita mwamphamvu.

17. Sindidzafa koma ndidzakhala ndi moyo,Ndipo ndidzafotokozera nchito za Yehova.

18. Kulanga anandilangadi Yehova:Koma sanandipereka kuimfa ai.

19. Nditsegulireni zipata za cilungamo;Ndidzalowamo, ndidzayamika Yehova.

20. Cipata ca Yehova ndi ici;Olungama adzalowamo.

21. Ndidzakuyamikani, popeza munandiyankha,Ndipo munakhala cipulumutso canga,

22. Mwala umene omangawo anaukanaWakhala mutu wa pangondya.

23. Ici cidzera kwa Yehova;Ncodabwiza ici pamaso pathu.

24. Tsiku ili ndilo adaliika Yehova;Tidzasekera ndi kukondwera m'mwemo.

25. Tikupemphani, Yehova, tipulumutseni tsopano;Tikupemphani, Yehova, tipindulitseni tsopano.

26. Wodala wakudzayo m'dzina la Yehova;Takudalitsani kocokera m'nyumba ya Yehova.

27. Yehova ndiye Mulungu, amene anatiunikira;Mangani nsembe ndi zingwe, ku nyanga za guwa la nsembe.

28. Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakuyamikani;Ndinu Mulungu wanga, ndidzakukwezani.

29. Yamikani Yehova, pakuti Iye ndiye wabwino,Pakuti cifundo cace ncosatha.