Mitu

  1. 1
  2. 2
  3. 3
  4. 4
  5. 5
  6. 6
  7. 7
  8. 8
  9. 9
  10. 10
  11. 11
  12. 12
  13. 13
  14. 14
  15. 15
  16. 16
  17. 17
  18. 18
  19. 19
  20. 20
  21. 21
  22. 22
  23. 23
  24. 24
  25. 25
  26. 26
  27. 27
  28. 28
  29. 29
  30. 30
  31. 31
  32. 32
  33. 33
  34. 34
  35. 35
  36. 36
  37. 37
  38. 38
  39. 39
  40. 40
  41. 41
  42. 42
  43. 43
  44. 44
  45. 45
  46. 46
  47. 47
  48. 48
  49. 49
  50. 50
  51. 51
  52. 52
  53. 53
  54. 54
  55. 55
  56. 56
  57. 57
  58. 58
  59. 59
  60. 60
  61. 61
  62. 62
  63. 63
  64. 64
  65. 65
  66. 66
  67. 67
  68. 68
  69. 69
  70. 70
  71. 71
  72. 72
  73. 73
  74. 74
  75. 75
  76. 76
  77. 77
  78. 78
  79. 79
  80. 80
  81. 81
  82. 82
  83. 83
  84. 84
  85. 85
  86. 86
  87. 87
  88. 88
  89. 89
  90. 90
  91. 91
  92. 92
  93. 93
  94. 94
  95. 95
  96. 96
  97. 97
  98. 98
  99. 99
  100. 100
  101. 101
  102. 102
  103. 103
  104. 104
  105. 105
  106. 106
  107. 107
  108. 108
  109. 109
  110. 110
  111. 111
  112. 112
  113. 113
  114. 114
  115. 115
  116. 116
  117. 117
  118. 118
  119. 119
  120. 120
  121. 121
  122. 122
  123. 123
  124. 124
  125. 125
  126. 126
  127. 127
  128. 128
  129. 129
  130. 130
  131. 131
  132. 132
  133. 133
  134. 134
  135. 135
  136. 136
  137. 137
  138. 138
  139. 139
  140. 140
  141. 141
  142. 142
  143. 143
  144. 144
  145. 145
  146. 146
  147. 147
  148. 148
  149. 149
  150. 150

Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 45 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

Nyimbo voyimbira ukwati wa mfumu

Kwa Mkulu wa Nyimbo pa Syosyanim. Cilangizo ca kwa ana a Kora. Nyimbo ya cikondi.

1. Mtima wanga usefukira naco cinthu cokoma:Ndinena zopeka ine za mfumu:Lilime langa ndilo peni yofulumiza kulemba.

2. Inu ndinu wokongola ndithu kuposa ana a anthu;Anakutsanulirani cisomo pa milomo yanu:Cifukwa cace Mulungu anakudalitsani kosatha.

3. Dzimangireni lupanga lanu m'cuuno mwanu, wamphamvu inu,Ndi ulemerero wanu ndi ukulu wanu.

4. Ndipo pindulani, m'ukulu wanu yendani,Kaamba ka coonadi ndi cifatso ndi cilungamo:Ndipo dzanja lanu lidzakuphunzitsani zoopsa.

5. Mibvi yanu njakuthwa;Mitundu ya anthu igwa pansi pa Inu:Iwalasa mumtima adani a mfumu.

6. Mpando wacifumu wanu, Mulungu, ukhala nthawi zonse zamkamuyaya:Ndodo yacifumu ya ufumu wanu ndiyo ndodo yolunjika.

7. Mukonda cilungamo, ndipo mudana naco coipa:Cifukwa cace Mulungu, ndiye Mulungu wanu, wadzoza inuNdi mafuta a cikondwerero kuposa anzanu.

8. Zobvala zanu zonse nza mure, ndi khonje, ndi kasya;M'zinyumba za mfumu zomanga ndi minyanga ya njobvu mwatoruka zoyimba za zingwe zokukondweretsani.

9. Mwa omveka anu muli ana akazi amafumu:Ku dzanja lamanja lanu aima mkazi wa mfumu wobvala golidi wa ku Ofiri.

10. Tamvera, mwana wamkaziwe, taona, tachera khutu lako;Uiwalenso mtundu wako ndi nyumba ya atate wako;

11. Potero mfumuyo adzakhumba kukoma kwako:Pakuti ndiye mbuye wako; ndipo iwe umgwadire iye.

12. Ndipo mwana wamkazi wa Turo adzafika nayo mphatso;Acuma a mwa anthu adzapempha kudziwika nanu.

13. Mwana wamkazi wa mfumu ngwa ulemerero wonse m'kati mwa nyumba:Zobvala zace nza made agolidi.

14. Adzamtsogolera kwa mfumu wabvala zamawanga-mawanga:Anamwali anzace omtsata adzafika nao kwa inu.

15. Adzawatsogolera ndi cimwemwe ndi kusekerera:Adzalowa m'nyumba ya mfumu.

16. M'malo mwa makolo ako mudzakhala ana ako,Udzawaika akhale mafumu m'dziko lonse lapansi.

17. Ndidzawakumbutsa dzina lanu m'mibadwo mibadwo:Cifukwa cace mitundu ya anthu idzayamika Inu ku nthawi za nthawi.