Mitu

  1. 1
  2. 2
  3. 3
  4. 4
  5. 5
  6. 6
  7. 7
  8. 8
  9. 9
  10. 10
  11. 11
  12. 12
  13. 13
  14. 14
  15. 15
  16. 16
  17. 17
  18. 18
  19. 19
  20. 20
  21. 21
  22. 22
  23. 23
  24. 24
  25. 25
  26. 26
  27. 27
  28. 28
  29. 29
  30. 30
  31. 31
  32. 32
  33. 33
  34. 34
  35. 35
  36. 36
  37. 37
  38. 38
  39. 39
  40. 40
  41. 41
  42. 42
  43. 43
  44. 44
  45. 45
  46. 46
  47. 47
  48. 48
  49. 49
  50. 50
  51. 51
  52. 52
  53. 53
  54. 54
  55. 55
  56. 56
  57. 57
  58. 58
  59. 59
  60. 60
  61. 61
  62. 62
  63. 63
  64. 64
  65. 65
  66. 66
  67. 67
  68. 68
  69. 69
  70. 70
  71. 71
  72. 72
  73. 73
  74. 74
  75. 75
  76. 76
  77. 77
  78. 78
  79. 79
  80. 80
  81. 81
  82. 82
  83. 83
  84. 84
  85. 85
  86. 86
  87. 87
  88. 88
  89. 89
  90. 90
  91. 91
  92. 92
  93. 93
  94. 94
  95. 95
  96. 96
  97. 97
  98. 98
  99. 99
  100. 100
  101. 101
  102. 102
  103. 103
  104. 104
  105. 105
  106. 106
  107. 107
  108. 108
  109. 109
  110. 110
  111. 111
  112. 112
  113. 113
  114. 114
  115. 115
  116. 116
  117. 117
  118. 118
  119. 119
  120. 120
  121. 121
  122. 122
  123. 123
  124. 124
  125. 125
  126. 126
  127. 127
  128. 128
  129. 129
  130. 130
  131. 131
  132. 132
  133. 133
  134. 134
  135. 135
  136. 136
  137. 137
  138. 138
  139. 139
  140. 140
  141. 141
  142. 142
  143. 143
  144. 144
  145. 145
  146. 146
  147. 147
  148. 148
  149. 149
  150. 150

Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 103 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

Alemekeze Yehovapa cifundo cace cacikuru

Salmo la Da vide.

1. Lemekeza Yehova, moyo wanga;Ndi zonse za m'kati mwanga zilemekeze dzina lace loyera.

2. Lemekeza Yehova, moyo wanga,Ndi kusaiwala zokoma zace zonse aticitirazi:

3. Amene akhululukira mphulupulu zako zonse;Naciritsa nthenda zako zonse;

4. Amene aombola moyo wako ungaonongeke;Nakubveka korona wa cifundo ndi nsoni zokoma:

5. Amene akhutitsa m'kamwa mwako ndi zabwino;Nabweza ubwana wako unge mphungu.

6. Yehova acitira onse osautsidwa Cilungamo ndi ciweruzo.

7. Analangiza Mose njira zace,Ndi ana a Israyeli macitidwe ace.

8. Yehova ndiye wa nsoni zokoma ndi wacisomo,Wosakwiya msanga, ndi wa cifundo cocuruka.

9. Sadzatsutsana nao nthawi zanse;Ndipo sadzasunga mkwiyo wace kosatha.

10. Sanaticitira monga mwa zolakwa zathu,Kapena kutibwezera monga mwa mphulupulu zathu.

11. Pakuti monga m'mwamba mutalikira ndi dziko lapansi,Motero cifundo cace cikulira iwo akumuopa Iye.

12. Monga kum'mawa kutanimpha ndi kumadzulo,Momwemo anatisiyanitsira kutali zolakwa zathu.

13. Monga atate acitira ana ace cifundo,Yehova acitira cifundo iwo akumuopa Iye.

14. Popeza adziwa mapangidwe athu;Akumbukila kuti ife ndife pfumbi.

15. Koma munthu, masiku ace akunga udzu;Aphuka monga duwa la kuthengo.

16. Pakuti mphepo ikapitapo pakhala palibe:Ndi malo ace salidziwanso.

17. Koma cifundo ca Yehova ndico coyambira nthawi yosayamba kufikira nthawi yosatha kwa iwo akumuopa Iye,Ndi cilungamo cace kufikira kwa ana a ana;

18. Kwa iwo akusunga cipangano cace,Ndi kwa iwo akukumbukila malangizo ace kuwacita.

19. Yehova anakhazika mpando wacifumu wace Kumwamba;Ndi ufumu wace ucita mphamvu ponsepo,

20. Lemekezani Yehova, inu angelo ace;A mphamvu zolimba, akucita mau ace,Akumvera liu la mau ace.

21. Lemekezani Yehova, inu makamu ace onse;Inu atumiki ace akucita comkondweretsa Iye,

22. Lemekezani Yehova, inu, nchito zace zonse,Ponse ponse pali ufumu wace:Lemekeza Yehova, moyo wanga iwe.