Mitu

  1. 1
  2. 2
  3. 3
  4. 4
  5. 5
  6. 6
  7. 7
  8. 8
  9. 9
  10. 10
  11. 11
  12. 12
  13. 13
  14. 14
  15. 15
  16. 16
  17. 17
  18. 18
  19. 19
  20. 20
  21. 21
  22. 22
  23. 23
  24. 24
  25. 25
  26. 26
  27. 27
  28. 28
  29. 29
  30. 30
  31. 31
  32. 32
  33. 33
  34. 34
  35. 35
  36. 36
  37. 37
  38. 38
  39. 39
  40. 40
  41. 41
  42. 42
  43. 43
  44. 44
  45. 45
  46. 46
  47. 47
  48. 48
  49. 49
  50. 50
  51. 51
  52. 52
  53. 53
  54. 54
  55. 55
  56. 56
  57. 57
  58. 58
  59. 59
  60. 60
  61. 61
  62. 62
  63. 63
  64. 64
  65. 65
  66. 66
  67. 67
  68. 68
  69. 69
  70. 70
  71. 71
  72. 72
  73. 73
  74. 74
  75. 75
  76. 76
  77. 77
  78. 78
  79. 79
  80. 80
  81. 81
  82. 82
  83. 83
  84. 84
  85. 85
  86. 86
  87. 87
  88. 88
  89. 89
  90. 90
  91. 91
  92. 92
  93. 93
  94. 94
  95. 95
  96. 96
  97. 97
  98. 98
  99. 99
  100. 100
  101. 101
  102. 102
  103. 103
  104. 104
  105. 105
  106. 106
  107. 107
  108. 108
  109. 109
  110. 110
  111. 111
  112. 112
  113. 113
  114. 114
  115. 115
  116. 116
  117. 117
  118. 118
  119. 119
  120. 120
  121. 121
  122. 122
  123. 123
  124. 124
  125. 125
  126. 126
  127. 127
  128. 128
  129. 129
  130. 130
  131. 131
  132. 132
  133. 133
  134. 134
  135. 135
  136. 136
  137. 137
  138. 138
  139. 139
  140. 140
  141. 141
  142. 142
  143. 143
  144. 144
  145. 145
  146. 146
  147. 147
  148. 148
  149. 149
  150. 150

Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 94 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

Mulungu wolungama adzaweruza otpa

1. Mulungu wakubwezera cilango,Yehova, Mulungu wakubwezera cilango, muoneke wowala.

2. Nyamukani, Inu woweruza wa dziko lapansi:Bwezerani odzikuza coyenera iwo.

3. Oipa adzatumpha ndi cimwemwe kufikira liti, Yehova?Oipa adzatero kufikira liti?

4. Anena mau, alankhula zawawa;Adzitamandira onse ocita zopanda pace.

5. Aphwanya anthu anu, Yehova,Nazunza colandira canu.

6. Amapha wamasiye ndi mlendo,Nawapha ana amasiye.

7. Ndipo amati, Yehova sacipenya,Ndi Mulungu wa Yakobo sacisamalira.

8. Zindikirani, opulukira inu mwa anthu;Ndipo opusa inu, mudzacita mwanzeru liti?

9. Kodi Iye wakupanga khutu ngwosamva?Kodi Iye wakuumba diso ngwosapenya?

10. Kodi Iye wakulangiza mitundu ya anthu, ndiye wosadzudzula?Si ndiye amene aphunzitsa munthu nzeru?

11. Yehova adziwa zolingalira za munthu,Kuti ziri zacabe.

12. Wodala munthu amene mumlanga, Yehova;Ndi kumphunzitsa m'cilamulo canu;

13. Kuti mumpumitse masiku oipa;Kufikira atakumbira woipa mbuna.

14. Pakuti Yehova sadzasiya anthu ace,Ndipo sadzataya colandira cace.

15. Pakuti ciweruzo cidzabwera kumka kucilungamo:Ndipo oongoka mtima onse adzacitsata.

16. Adzandiukira ndani kutsutsana nao ocita zoipa?Adzandilimbikira ndani kutsutsana nao ocita zopanda pace?

17. Akadapanda kukhala thandizo langa Yehova,Moyo wanga ukadakhala kuli cete.

18. Pamene ndinati, Litereka phazi langa,Cifundo canu, Mulungu, cinandicirikiza.

19. Pondicurukira zolingalira zanga m'kati mwanga,Zotonthoza zanu zikondweretsa moyo wanga.

20. Kodi uyenera kuyanjana ndi Inu mpando wacifumu wa kusakaza,Wakupanga cobvuta cikhale lamulo?

21. Asonkhana pamodzi pa moyo wa wolungama,Namtsutsa wa mwazi wosacimwa.

22. Koma Yehova wakhala msanje wanga;Ndi Mulungu wanga thanthwe lothawirapo ine.

23. Ndipo anawabwezera zopanda pace zao,Nadzawaononga m'coipa cao;Yehova Mulungu wathu adzawaononga.