Mitu

  1. 1
  2. 2
  3. 3
  4. 4
  5. 5
  6. 6
  7. 7
  8. 8
  9. 9
  10. 10
  11. 11
  12. 12
  13. 13
  14. 14
  15. 15
  16. 16
  17. 17
  18. 18
  19. 19
  20. 20
  21. 21
  22. 22
  23. 23
  24. 24

Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 2 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

Davide alowa ufumu wa Yuda

1. Ndipo zitatha izi Davide anafunsira kwa Yehova nati, Kodi ndikwere kunka m'mudzi wina wa Yuda? Ndipo Yehova ananena naye, Kwera. Davide nanena naye, Ndikwere kuti? Ndipo anati, Ku Hebroni.

2. Comweco Davide anakwera kunka kumeneko pamodzi ndi akazi ace awiri, ndiwo Ahingamu Mjezreeli, ndi Abigayeli mkazi wa Nabala wa ku Karimeli.

3. Ndipo Davide anakwera nao anyamata ace okhala naye, munthu yense ndi banja lace; iwowa nakhala m'midzi ya Hebroni.

4. Ndipo anthu Ayuda anabwera namdzoza Davide pomwepo akhale mfumu ya nyumba ya Yuda.Ndipo wina anauza Davide kuti, Anthu a ku Jabezi Gileadi ndiwo amene anamuika Sauli.

5. Pamenepo Davide anatumiza mithenga kwa anthu a ku Jabezi Gileadi, nanena nao, Mudalitsike ndi Yehova inu, popeza munacitira cokoma ici mbuye wanu Sauli, ndi kumuika.

6. Ndipo tsopano Yehova acitire inu cokoma ndi coonadi; inenso ndidzakubwezerani cokoma ici, popeza munacita cinthuci.

7. Cifukwa cace tsono manja anu alimbike, nimucite camuna; pakuti Sauli mbuye wanu wafa, ndi a nyumba ya Yuda anandidzoza ndikhale mfumu yao.

Isibosete alowa ufumu wa Israyeli

8. Koma Abineri, mwana wa Neri, kazembe wa khamu la ankhondo a Sauli anatenga Isiboseti mwana wa Sauli, namuolotsa nanka naye ku Mahanaimu;

9. namlonga ufumu wa pa Gileadi ndi Aasuri ndi Jezreeli ndi Efraimu ndi Benjamini ndi Aisrayeli onse.

10. Ndipo Isiboseti mwana wa Sauli anali ndi zaka makumi anai pakuyamba iye kukhala mfumu ya Israyeli, nacita ufumu zaka ziwiri. Koma a nyumba ya Yuda anatsata Davide.

11. Ndipo Davide anali mfumu ya nyumba ya Yuda ku Hebroni zaka zisanu ndi ziwiri kudza miyezi isanu ndi umodzi.

Ayuda ndi Aisrayeli alimbana ku Gibeoni

12. Ndipo Abineri mwana wa Neri ndi anyamata a Isiboseti mwana wa Sauli anaturuka ku Mahanaimu kunka ku Gibeoni.

13. Ndi Yoabu mwana wa Zeruya, ndi anyamata a Davide anaturuka nakomana nao pa thamanda la Gibeoni; nakhala pansi, ena tsidya lino, ndi ena tsidya lija la thamandalo.

14. Ndipo Abineri ananena ndi Yoabu, Aimirire anyamata nasewere pamaso pathu. Nati Yoabu, Aimirire.

15. Pomwepo iwo anaimirira naoloka owerengedwa, khumi ndi awiri a kwa Benjamini, ndi Isiboseti mwana wa Sauli, ndi khumi ndi awiri a anyamata a Davide.

16. Ndipo anagwirana munthu yense kugwira mutu wa mnzace, nagwaza ndi lupanga lace m'nthiti mwa mnzaceo Comweco anagwa limodzi; cifukwa cace malo aja anachedwa Dera la Mipeni la ku Gibeoni.

17. Ndipo tsikulo nkhondo inakula ndithu. Ndi Abineri ndi anthu a Israyeli anathawa pamaso pa anyamata a Davide.

18. Ndipo analipo ana atatu a Zeruya, ndiwo Yoabu, Abisai ndi Asaheli. Ndipo Asaheli anali waliwiro ngati nyama ya kuthengo.

19. Ndipo Asaheli anapitikitsa Abineri. Ndipo m'kuthamanga kwace sanapambukira kulamanja, kapena kulamanzere, pakutsata Abineri.

20. Pomwepo Abineri anaceuka nati, Kodi ndi iwe Asaheli? iye nayankha, Ndine.

21. Ndipo Abineri ananena naye, Patuka iwe kulamanja kapena kulamanzere kwako nudzigwirire wina wa anyamatawo, nutenge zida zace. Koma Asaheli anakana kupambuka pakumtsata iye.

22. Ndipo Abineri anabwereza kunena kwa Asaheli, Pambuka pakunditsata ine. Ndidzakukanthiranji kukugwetsa pansi? ndikatero ndidzaweramutsanso bwanji nkhope yanga kwa mbale wako Yoabu?

23. Koma iye anakana kupambuka; cifukwa cace Abineri anamkantha ndi khali la mkondo m'mimba mwace, ndi khalilo linaturuka kumbuyo kwace. Ndipo anagwako, nafera pomwepo, Ndipo onse akufika kumalo kumene Asaheli anagwa, namwalirapo, anaima pomwepo.

24. Koma Yoabu ndi Abisai anampitikitsa Abineri; ndipo dzuwa linawalowera pofika ku citunda ca Ama, cakuno ca Giya, pa njira ya ku cipululu ca Gibeoni.

25. Ndipo ana a Benjamini anaunjikana pamodzi kutsata Abinen, nakhala gulu limodzi, naima pamwamba pa citunda.

26. Pomwepo Abineri anaitana Yoabu nati, Kodi lupanga lidzaononga cionongere? sudziwa kodi kuti kutha kwace kudzakhala udani ndithu? Tsono udzakhalanso nthawi yanji osauza anthu kubwerera pakutsata abale ao?

27. Yoabu nati, Pali Mulungu, iwe ukadapandakunena, anthu akadabalalika m'mawa osatsata yense mbale wace.

28. Comweco Yoabu anaomba Gpenga, anthu onse naima, naleka kupitikitsa Aisrayeli, osaponyana naonso.

29. Ndipo Abineri ndi anthu ace anacezera usiku wonse kupyola cidikha, naoloka Yordano, napyola Bitroni lonse nafika ku Mahanaimu.

30. Ndipo Yoabu anabwerera pakutsata Abineri. Ndipo pamene anasonkhanitsa pamodzi anthu onse anasowa anthu a Davide khumi ndi asanu ndi anai ndi Asaheli.

31. Koma anyamata a Davide anakantha anthu a Benjamini ndi a Abineri, namwalira mazana atatu mphambu makumi asanu ndi limodzi.

32. Ndipo ananyamula Asaheli namuika m'manda a atate wace ali ku Betelehemu. Ndipo Yoabu ndi anthu ace anacezera kuyenda usiku wonse, ndipo kudawacera ku Hebroni.