Mitu

  1. 1
  2. 2
  3. 3
  4. 4
  5. 5
  6. 6
  7. 7
  8. 8
  9. 9
  10. 10
  11. 11
  12. 12
  13. 13
  14. 14
  15. 15
  16. 16
  17. 17
  18. 18
  19. 19
  20. 20
  21. 21
  22. 22
  23. 23
  24. 24
  25. 25
  26. 26
  27. 27
  28. 28
  29. 29
  30. 30
  31. 31
  32. 32
  33. 33
  34. 34
  35. 35
  36. 36
  37. 37
  38. 38
  39. 39
  40. 40
  41. 41
  42. 42
  43. 43
  44. 44
  45. 45
  46. 46
  47. 47
  48. 48
  49. 49
  50. 50
  51. 51
  52. 52
  53. 53
  54. 54
  55. 55
  56. 56
  57. 57
  58. 58
  59. 59
  60. 60
  61. 61
  62. 62
  63. 63
  64. 64
  65. 65
  66. 66

Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 62 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

Cikhalidwe cokoma ca Yerusalemu

1. Cifukwa ca Ziyoni sindidzakhala cete, ndi cifukwa ca Yerusalemu sindidzapuma, kufikira cilungamo cace cidzaturuka monga kuyera, ndi cipulumutso cace monga nyali yoyaka.

2. Ndipo amitundu adzaona cilungamo cako, ndi mafumu onse ulemerero wako; ndipo udzachedwa dzina latsopano, limene m'kamwa mwa Yehova mudzachula.

3. Iwe udzakhalanso korona wokongola m'dzanja la Yehova, korona wacifumu m'dzanja la Mulungu wako.

4. Iwe sudzachedwanso Wosiyidwa; dziko lako silidzachedwanso Bwinja; koma iwe udzachedwa Hefiziba ndi dziko lako Beula; pakuti Yehova akondwera mwa iwe, ndipo dziko lako lidzakwatiwa.

5. Pakuti monga mnyamata akwatira namwali, momwemo ana ako amuna adzakukwama iwe; ndi monga mkwati akondwera ndi mkwatibwi, momwemo Mulungu wako adzakondwera nawe.

6. Ndaika alonda pa malinga ako, Yerusalemu; iwo sadzakhala cete usana pena usiku; inu akukumbutsa Yehova musakhale cete,

7. ndipo musamlole akhale cete, kufikira Iye atakhazikitsa naika Yerusalemu akhale tamando m'dziko lapansi.

8. Yehova analumbira pa dzanja lace lamanja, ndi mkono wace wamphamvu, Zoonadi, sindidzaperekanso tirigu wako akhale cakudya ca adani ako, ndipo alendo sadzamwa vinyo wako amene iwe unagwirira nchito;

9. koma iwo amene adzakolola adzadya ndi kutamanda Yehova; ndi iwo amene adzamchera adzamumwa m'mabwalo a kacisi wanga.

10. Pitani, pitani pazipata; konzani njira ya anthu; undani, undani khwalala; cotsani miyala, kwezani mbendera ya anthu.

11. Taonani, Yehova walalikira kufikira malekezero a dziko lapansi. Nenani kwa mwana wamkazi wa Ziyoni, Taona cipulumutso cako cifika; taona mphotho yace ali nayo, ndi nchito yace iri pamaso pace.

12. Ndipo iwo adzawacha Anthu opatulika, Oomboledwa a Yehova; ndipo iwe udzachedwa Wofunidwa, Mudzi wosasiyidwa.