Mitu

  1. 1
  2. 2
  3. 3
  4. 4
  5. 5
  6. 6
  7. 7
  8. 8
  9. 9
  10. 10
  11. 11
  12. 12
  13. 13
  14. 14
  15. 15
  16. 16
  17. 17
  18. 18
  19. 19
  20. 20
  21. 21
  22. 22
  23. 23
  24. 24
  25. 25
  26. 26
  27. 27
  28. 28
  29. 29
  30. 30
  31. 31
  32. 32
  33. 33
  34. 34
  35. 35
  36. 36
  37. 37
  38. 38
  39. 39
  40. 40
  41. 41
  42. 42
  43. 43
  44. 44
  45. 45
  46. 46
  47. 47
  48. 48
  49. 49
  50. 50
  51. 51
  52. 52
  53. 53
  54. 54
  55. 55
  56. 56
  57. 57
  58. 58
  59. 59
  60. 60
  61. 61
  62. 62
  63. 63
  64. 64
  65. 65
  66. 66

Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 38 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

Kudwala kwa Hezekiya ndi kuciritsidwa kwace

1. Masiku amenewo Hezekiya anadwala, nafuna kufa. Ndipo Yesaya mneneri, mwana wa Amozi, anadza kwa iye, nati kwa iye, Atero Yehova, Konza nyumba yako, pakuti iwe udzafa, sudzakhala ndi moyo.

2. Ndipo Hezekiya analoza nkhope yace kukhoma, napemphera kwa Yehova, nati,

3. Kumbukiranitu tsopano, Yehova, kuti ndayenda pamaso panu m'zoonadi ndi mtima wangwiro, ndipo ndacita zabwino pamaso panu. Ndipo Hezekiya analira kolimba.

4. Ndipo anafika mau a Yehova kwa Yesaya, ndi kuti,

5. Ukanene kwa Hezekiya, Atero Yehova, Mulungu wa Davide, kholo lako, Ndamva kupemphera kwako, ndaona misozi yako; taona, ndidzaonjezera pa masiku ako zaka khumi ndi zisanu.

6. Ndipo ndidzakupulumutsa iwe ndi mudzi uno m'manja mwa mfumu ya Asuri, ndipo ndidzacinjiriza mudzi uno.

7. Ndipo ici cidzakhala cizindikilo kwa iwe cocokera kwa Yehova, kuti Yehova adzacita ici wanenaci;

8. taona, ndidzabweza mthunzi wa pamakwerero, umene watsika pa makwerero a Ahazi ndi dzuwa, ubwerere makwerero khumi. Ndipo dzuwa linabwerera makwerero khumi pamakwerero, pamene udatsika mthunziwo.

9. Malemba a Hezekiya mfumu ya Ayuda muja anadwala, atacira nthenda yace.

10. Ine ndinati, Pakati pa masiku anga ndidzalowa m'zipata za kunsi kwa manda; Ndazimidwa zaka zanga zotsala.

11. Ndinati, Sindidzaona Yehova m'dziko la amoyo; sindidzaonanso munthu pamodzi ndi okhala kunja kuno;

12. Pokhala panga pacotsedwa, pandisunthikira monga hema wambusa;Ndapindapinda moyo wanga ngati muomba;Iye adzandidula ine poomberapo;Kuyambira usana kufikira usiku mudzanditsiriza ine.

13. Ndinadzitonthoza kufikira mamawa; monga mkango, momwemo Iye anatyolatyola mafupa anga onse;Kuyambira usana kufikira usiku mudzanditsiriza ine.

14. Ndinalankhula-lankhula ngati namzeze, pena cumba;Ndinalira maliro ngati nkhunda;Maso anga analephera pogadamira kumwamba.Yehova ndasautsidwa, mundiperekere cikoli.

15. Kodi ndidzanena ciani?Iye wanena kwa ine, ndiponso Iye mwini wacita ici;Ine ndidzayenda cete zaka zanga zonse,Cifukwa ca zowawa za moyo wanga.

16. Ambuye ndi zinthu izi anthu akhala ndi moyo.Ndipo m'menemo monse muli moyo wa mzimu wanga;Cifukwa cace mundiciritse ine,Ndi kundikhalitsa ndi moyo.

17. Taonani, ndinali ndi zowawa zazikuru,Cifukwa ca mtendere wanga;Koma Inu mokonda moyo wanga,Munaupulumutsa m'dzanja la cibvundi,Pakuti mwaponya m'mbuyo mwanu macimo anga onse.

18. Pakuti kunsi kwa manda sikungakuyamikeni Inu;Imfa singakulemekezeni;Otsikira kudzenje sangaziyembekeze zoona zanu.

19. Wamoyo, wamoyo, iye adzakuyamikani inu, monga ine lero;Atate adzadziwitsa ana ace zoona zanu.

20. Yehova ndiye wondipulumutsa ine;Cifukwa cace tidzayimba nyimbo zanga, ndi zoyimba zazingweMasiku onse a moyo wathu m'nyumba ya Yehova.

21. Ndipo Yesaya adati, Atenge mbulu wankhuyu, auike papfundo, Ndipo iye adzacira.

22. Hezekiya anatinso, Cizindikilo nciani, kuti ndidzakwera kunka ku nyumba ya Yehova?