Mitu

  1. 1
  2. 2
  3. 3
  4. 4
  5. 5
  6. 6
  7. 7
  8. 8
  9. 9
  10. 10
  11. 11
  12. 12
  13. 13
  14. 14
  15. 15
  16. 16
  17. 17
  18. 18
  19. 19
  20. 20
  21. 21
  22. 22
  23. 23
  24. 24
  25. 25
  26. 26
  27. 27
  28. 28
  29. 29
  30. 30
  31. 31
  32. 32
  33. 33
  34. 34
  35. 35
  36. 36
  37. 37
  38. 38
  39. 39
  40. 40
  41. 41
  42. 42
  43. 43
  44. 44
  45. 45
  46. 46
  47. 47
  48. 48
  49. 49
  50. 50
  51. 51
  52. 52
  53. 53
  54. 54
  55. 55
  56. 56
  57. 57
  58. 58
  59. 59
  60. 60
  61. 61
  62. 62
  63. 63
  64. 64
  65. 65
  66. 66

Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

Tsiku la Mulungu, kuyeretsedwa kwa Yerusalemu

1. Ndipo akazi asanu ndi awiri adzagwira mwamuna mmodzi tsiku limenelo, nati, Ife tidzadya cakudya cathu cathu ndi kubvala zobvala zathu zathu; koma tichedwe dzina lako; cotsa citonzo cathu.

2. Tsiku limenelo mphukira ya Yehova idzakhala yokongola ndi ya ulemerero, cipatso ca nthaka cidzakhala cokometsetsa ndi cokongola, kwa iwo amene adzapulumuka a Israyeli.

3. Ndipo padzakhala, kuti iye amene asiyidwa m'Ziyoni, ndi iye amene atsala m'Yerusalemu, adzachedwa woyera; ngakhale yense amene walembedwa mwa amoyo m'Yerusalemu;

4. pamene Ambuye adzasambitsa litsiro la ana akazi a Ziyoni, nadzatsuka mwazi wa Yerusalemu, kucokera pakatipo, ndi mzimu wa ciweruziro, ndi mzimu wakutentha.

5. Ndipo Yehova adzalenga pokhala ponse pa phiri la Ziyoni, ndi pa masonkhano ace, mtambo ndi utsi usana, ndi kung'azimira kwa malawi a moto usiku; cifukwa kuti pa ulemerero wonse padzayalidwa cophimba.

6. Ndipo padzakhala cihema ca mthunzi, nthawi ya usana yopewera kutentha, pothawira ndi pousa mvula ndi mphepo.