Mitu

  1. 1
  2. 2
  3. 3
  4. 4
  5. 5
  6. 6
  7. 7
  8. 8
  9. 9
  10. 10
  11. 11
  12. 12
  13. 13
  14. 14
  15. 15
  16. 16
  17. 17
  18. 18
  19. 19
  20. 20
  21. 21
  22. 22
  23. 23
  24. 24
  25. 25
  26. 26
  27. 27
  28. 28
  29. 29
  30. 30
  31. 31
  32. 32
  33. 33
  34. 34
  35. 35
  36. 36
  37. 37
  38. 38
  39. 39
  40. 40
  41. 41
  42. 42
  43. 43
  44. 44
  45. 45
  46. 46
  47. 47
  48. 48
  49. 49
  50. 50
  51. 51
  52. 52
  53. 53
  54. 54
  55. 55
  56. 56
  57. 57
  58. 58
  59. 59
  60. 60
  61. 61
  62. 62
  63. 63
  64. 64
  65. 65
  66. 66

Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

Ciyamiko ca anthu a Mulungu atalangidwa

1. Tsiku lomwelo udzati, Ndikuyamikani inu Yehova; pakuti ngakhale munandikwiyira, mkwiyo wanu wacoka, ndipo mutonthoza mtima wanga.

2. Taonani, Mulungu ndiye cipulumutso canga; ndidzakhulupira, sindidzaopa; pakuti Yehova Mwini ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga, Iye ndiye cipulumutso canga.

3. Cifukwa cace mudzakondwera pakutunga madzi m'zitsime za cipulumutso.

4. Tsiku lomwelo mudzati, Muyamikire Yehova, bukitsani dzina lace, mulalikire macitidwe ace mwa mitundu ya anthu, munene kuti dzina lace lakwezedwa.

5. Muyimbire Yehova; pakuti wacita zaulemerero; cidziwike ici m'dziko lonse.

6. Tapfuula, takuwa iwe, wokhala m'Ziyoni, cifukwa Woyera wa Israyeli wa m'kati mwako ali wamkuru.