1. Mwananga, usaiwale malamulo anga,Mtima wako usunge malangizo anga;
2. Pakuti adzakuonjezera masiku ambiri,Ndi zaka za moyo ndi mtendere.
3. Cifundo ndi coonadi zisakusiye;Uzimange pakhosi pako;Uzilembe pamtima pako;
4. Motero udzapezakisomo ndi nzeru yabwino,Pamaso pa Mulungu ndi anthu.
5. Khulupirira Yehova ndi mtima wako wonse,Osacirikizika pa luntha lako;
6. Umlemekeze m'njira zako zonse,Ndipo Iye adzaongola mayendedwe ako.
7. Usadziyese wekha wanzeru;Opa Yehova, nupatuke pazoipa;
8. Mitsempha yako idzalandirapo moyo,Ndi mafupa ako uwisi.
9. Lemekeza Yehova ndi cuma cako,Ndi zinthu zako zonse zoyambirira kuca;
10. Motero nkhokwe zako zidzangoti the,Mbiya zako zidzasefuka vinyo.
11. Mwananga, usapeputse mwambo wa Yehova,Ngakhale kutopa ndi kudzudzula kwace;
12. Pakuti Yehova adzudzula omwe awakonda;Monga atate mwana amene akondwera naye.
13. Wodala ndi wopeza nzeru,Ndi woona luntha;
14. Pakuti malonda a nzeru aposa malonda a siliva,Phindu lace liposa golidi woyengeka.
15. Mtengo wace uposa ngale;Ndipo zonse zikukondweretsa sizilingana naye.
16. Masiku ambiri ali m'dzanja lamanja lace;Cuma ndi ulemu m'dzanja lace lamanzere.
17. Njira zace ziri zokondweretsa,Mayendedwe ace onse ndiwo mtendere.
18. Ndiyo mtengo wa moyo wa akuigwira;Wakulumirira ngwodala.
19. Yehova anakhazika dziko ndi nzeru;Naika zamwamba ndi luntha.
20. Zakuya zinang'ambika ndi kudziwakwace;Thambo ligwetsa mame.
21. Mwananga, zisacokere ku maso ako;Sunga nzeru yeniyeni ndi kulingalira;
22. Ndipo mtima wako udzatengapo moyo,Ndi khosi lako cisomo.
23. Pompo udzayenda m'njira yako osaopa,Osapunthwa phazi lako.
24. Ukagona, sudzacita mantha;Udzagona tulo tokondweretsa.
25. Usaope zoopsya zodzidzimutsa,Ngakhale zikadza zopasula oipa;
26. Pakuti Yehova adzalimbitsa mtima wako,Nadzasunga phazi lako lingakodwe.
27. Oyenera kulandira zabwino usawamane;Pokhoza dzanja lako kuwacitira zabwino.
28. Usanene kwa mnzako, Ukabwerenso,Ndipo mawa ndidzakupatsa;Pokhala uli nako kanthu.
29. Usapangire mnzako ciwembu;Popeza akhala nawe pafupi osatekeseka.
30. Usakangane ndi munthu cabe,Ngati sanakucitira coipa,
31. Usacitire nsanje munthu waciwawa;Usasankhe njira yace iri yonse.
32. Pakuti wamphulupulu anyansa Yehova;Koma cinsinsi cace ciri ndi oongoka.
33. Mulungu atemberera za m'nyumba ya woipa;Koma adalitsa mokhalamo olungama.
34. Anyozadi akunyoza,Koma apatsa akufatsa cisomo.
35. Anzeru adzalandira ulemu colowa cao;Koma opusa adzakweza manyazi.