1. Wopanduka afunafuna niro cace,Nakangana ndi nzeru yonse yeniyeni.
2. Wopusa sakondwera ndi kuzindikira;Koma kungobvumbulutsa za m'mtima mwace.
3. Pakudza wamphulupulu padzanso kunyoza;Manyazi natsagana ndi citonzo.
4. Mau a m'kamwa mwa munthu ndiwo madzi akuya;Kasupe wa nzeru ndiye mtsinje wodzala.
5. Kukometsa mlandu wa wamphulupulu mwatsankhu sikuli kwabwino,Ngakhale kucitira cetera wolungama.
6. Milomo ya wopusa ifikitsa makangano;Ndipo m'kamwa mwace muputa kukwapulidwa.
7. M'kamwa mwa wopusa mumuononga,Milomo yace ikhala msampha wa moyo wace.
8. Mau a kazitape akunga zakudya zolongosoka,Zotsikira m'kati mwa mimba.
9. Wogwira nchito mwaulesiNdiye mbale wace wa wosakaza.
10. Dzina la Yehova ndilo linga lolimba;Wolungama athamangiramo napulumuka.
11. Cuma ca wolemera ndico mudzi wace wolimba;Alingalira kuti ndico khoma lalitari.
12. Mtima wa munthu unyada asanaonongeke;Koma cifatso citsogolera ulemu.
13. Wobwezera mau asanamvetse apusa,Nadzicititsa manyazi.
14. Mtima wa munthu umlimbitsa alikudwala;Koma ndani angatukule mtima wosweka?
15. Mtima wa wozindikira umaphunzira;Khutu la anzeru lifunitsa kudziwa.
16. Mtulo wa munthu umtsegulira njira,Numfikitsa pamaso pa akuru.
17. Woyamba kudzinenera ayang'anika wolungama;Koma mnzace afika namuululitsa zace zonse.
18. Ula uletsa makangano,Nulekanitsa amphamvu.
19. Kupembedza mbale utamcimwira nkobvuta,Kulanda mudzi wolimba nkosabvuta;Makangano akunga mipiringidzo ya linga.
20. Mimba ya munthu idzakhuta zipatso za m'kamwa mwace;Iye nadzakhuta phindu la milomo yace.
21. Lilime liri ndi mphamvu pa imfa ndi moyo;Wolikonda adzadya zipatso zace.
22. Wopeza mkazi apeza cinthu cabwino;Yehova amkomera mtima.
23. Wosauka amadandaulira;Koma wolemera ayankha mwaukali.
24. Woyanjana ndi ambiri angodziononga;Koma liripo bwenzi lipambana ndi mbale kuumirira.