Mitu

  1. 1
  2. 2
  3. 3
  4. 4
  5. 5
  6. 6
  7. 7
  8. 8
  9. 9
  10. 10
  11. 11
  12. 12
  13. 13
  14. 14
  15. 15
  16. 16
  17. 17
  18. 18
  19. 19
  20. 20
  21. 21
  22. 22
  23. 23
  24. 24
  25. 25
  26. 26
  27. 27
  28. 28
  29. 29
  30. 30
  31. 31

Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Muyeso wonyenga unyansa Yehova;Koma mulingo wamphumphu umsekeretsa.

2. Pakudza kudzikuza padzanso manyazi;Koma nzeru iri ndi odzicepetsa,

3. Kuongoka mtima kwa olungama kuwatsogolera;Koma kukhota kwa aciwembu kudzawaononga.

4. Cuma sicithandiza tsiku la mkwiyo;Koma cilungamo cipulumutsa kuimfa.

5. Cilungamo ca wangwiro cimaongola njira yace;Koma woipa adzagwa ndi zoipa zace.

6. Cilungamo ca oongoka mtima cidzawapulumutsa;Koma aciwembu adzagwidwa ndi mphulupulu yao.

7. Pomwalira woipa cidikiro cace cionongeka;Ciyembekezo ca ucimo cionongeka.

8. Wolungama apulumuka kubvuto;Woipa nalowa m'malo mwace.

9. Wonyoza Mulungu aononga mnzace ndi m'kamwa mwace;Koma olungama adzapulumuka pakudziwa,

10. Olungama akapeza bwino, mudzi usekera;Nupfuula pakuonongeka oipa.

11. Madalitso a olungama akuza mudzi;Koma m'kamwa mwa oipa muupasula.

12. Wopeputsa mnzace asowa nzeru;Koma wozindikira amatonthola.

13. Kazitape woyendayenda amawanditsa zinsinsi;Koma wokhulupirika mtima abisa mau.

14. Popanda upo wanzeru anthu amagwa;Koma pocuruka aphungu pali cipulumutso.

15. Woperekera mlendo cikole adzaphwetekwapo;Koma wakuda cikole akhala ndi mtendere.

16. Mkazi wodekha agwiritsa ulemu;Aukali nagwiritsa cuma.

17. Wacifundo acitira moyo wace zokoma;Koma wankhanza abvuta nyama yace.

18. Woipa alandira malipiro onyenga;Koma wofesa cilungamo aonadi mphotho,

19. Wolimbikira cilungamo alandira moyo;Koma wolondola zoipa adzipha yekha,

20. Okhota mtima anyansa Yehova;Koma angwiro m'njira zao amsekeretsa.

21. Zoonadi, wocimwa sadzapulumuka cilango;Koma mbeu ya olungama idzalanditsidwa.

22. Monga cipini cagolidi m'mphuno ya nkhumba,Momwemo mkazi wokongola wosasinkhasinkha bwino.

23. Cifuniro ca olungama cifikitsa zabwino zokha;Koma ciyembekezo ca oipa mkwiyo.

24. Alipo wogawira, nangolemerabe;Aliponso womana comwe ayenera kupatsa nangosauka.

25. Mtima wa mataya udzalemera;Wothirira madzi nayenso adzathiriridwa.

26. Womana tirigu anthu amtemberera;Koma madalitso adzakhala pamtu pa wogulitsa.

27. Wopwaira ubwino afunitsa cikondwerero;Koma zoipa zidzamfikira wozilondola.

28. Wokhulupmra cuma cace adzagwa;Koma olungama adzaphuka ngati tsamba.

29. Wobvuta banja lace adzalowa m'zomsautsa;Wopusa adzatumikira wanzeru.

30. Cipatso ca wolungama ndi mtengo wa moyo;Ndipo wokola mtima ali wanzeru.

31. Taonani, wolungama adzalandira mphotho kunja kuno;Koposa kotani woipa ndi wocimwa?