Mitu

  1. 1
  2. 2
  3. 3
  4. 4
  5. 5
  6. 6
  7. 7
  8. 8
  9. 9
  10. 10
  11. 11
  12. 12
  13. 13
  14. 14
  15. 15
  16. 16
  17. 17
  18. 18
  19. 19
  20. 20
  21. 21
  22. 22
  23. 23
  24. 24
  25. 25
  26. 26
  27. 27
  28. 28
  29. 29
  30. 30
  31. 31

Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 1 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

Zocitira miyambi

1. MIYAMBI ya Solomo mwana wa Davide, mfumu ya Israyeli.

2. Kudziwa nzeru ndi mwambo;Kuzindikira mau ozindikiritsa;

3. Kulandira mwambo wakusamalira macitidwe,Cilungamo, ciweruzo ndi zolunjika;

4. Kucenjeza acibwana,Kuphunzitsa mnyamata kudziwa ndi kulingalira;

5. Kuti wanzeru amve, naonjezere kuphunzira;Ndi kuti wozindikira afikire kuuphungu;

6. Kuzindikira mwambi ndi tanthauzo lace,Mau a anzeru, ndi zophiphiritsa zao.

Munthu asalole oipa amcete

7. Kuopa Yehova ndiko ciyambi ca kudziwa;Opusa anyoza nzeru ndi mwambo.

8. Mwananga, tamva mwambo wa atate wako,Ndi kusasiya cilangizo ca amako

9. Pakuti izi ndi korona wa cisomo pamtu pako,Ndi mkanda pakhosi pako.

10. Mwananga, akakukopa ocimwa usalole.

11. Akanena, Idza nafe, tibisalire mwazi,Tilalire osacimwa opanda cifukwa;

12. Tiwameze ali ndi moyo ngati manda,Ali amphumphu, ngati akutsikira kudzenje;

13. Tidzapeza cuma conse ca mtengo wace,Tidzadzaza nyumba zathu ndi zofunkha;

14. Udzacita nafe maere,Tonse tidzakhala ndi cibeti cimodzi;

15. Mwananga, usayende nao m'njira;Letsa phazi lako ku mayendedwe ao;

16. Pakuti mapazi ao athamangira zoipa,Afulumira kukhetsa mwazi.

17. Pakuti kuchera msampha pamaso pa mbalame ndi cabe;

18. Ndipo awa abisalira mwazi wao wao, alalira miyoyo yao yao.

19. Mayendedwe a yense wopindula cuma monyenga ngotere;Cilanda moyo wa eni ace,

Ceniezo la Nzeru

20. Nzeru ipfuula panja;Imveketsa mau ace pabwalo;

21. Iitana posonkhana anthu polowera pacipata;M'mudzi inena mau ace;

22. Kodi mudzakonda zacibwana kufikira liti, acibwana inu?Onyoza ndi kukonda kunyoza,Opusa ndi kuda nzeru?

23. Tembenukani pamene ndikudzudzulani;Taonani, nditsanulira pa inu mzimu wanga,Ndikudziwitsani mau anga.

24. Cifukwa ndaitana, ndipo munakana;Ndatambasula dzanja langa, ndipo panalibe analabadira;

25. Koma munapeputsa uphungu wangawonse,Ndi kukana kudzudzula kwanga.

26. Inetu ndidzacitiraciphwete tsoka lanu,Ndidzatonyola pakudza mantha anu;

27. Pakudza mantha anu ngati mphepo yopasula,Ndi pofika tsoka lanu ngati kabvumvulu;Pakudza kwa inu bvuto ndi nsautso.

28. Pamenepo adzandiitana, koma sindidzabvomera;Adzandifunatu, osandipeza ai;

29. Cifukwa anada nzeru,Sanafuna kuopa Yehova;

30. Anakana uphungu wanga,Nanyoza kudzudzula kwanga konse;

31. Momwemo adzadya zipatso za mayendedwe ao,Nadzakhuta zolingalira zao.

32. Pakuti kubwerera m'mbuyo kwa acibwana kudzawapha;Ndipo mphwai za opusa zidzawaononga.

33. Koma wondimvera ine adzakhala osatekeseka,Nadzakhala phe osaopa zoipa,