1. Mwana wanzeru amamvera mwambo wa atate;Koma wonyoza samvera cidzudzulo.
2. Munthu adzadya zabwino ndi zipatso za m'kamwa mwace;Koma moyo wa aciwembu udzadya ciwawa.
3. Wogwira pakamwa pace asunga moyo wace;Koma woyasamula milomo yace adzaonongeka.
4. Moyo wa wolesi ukhumba osalandira kanthu;Koma moyo wa akhama udzalemera.
5. Wolungama ada mau onama;Koma woipa anyansa, nadzicititsa manyazi,
6. Cilungamo cicinjiriza woongoka m'njira;Koma udio ugwetsa wocimwa.
7. Alipo wodziyesa wolemera, koma alibe kanthu;Alipo wodziyesa wosauka, koma ali ndi cuma cambiri.
8. Ciombolo ca moyo wa munthu ndico cuma cace;Koma wosauka samva cidzudzulo.
9. Kuunika kwa olungama kukondwa;Koma nyali ya oipa idzazima.
10. Kudzikuza kupikisanitsa;Koma omwe anauzidwa uphungu ali ndi nzeru.
11. Cuma colandiridwa mokangaza cidzacepa;Koma wokundika ndi dzanja adzaona zocuruka.
12. Ciyembekezo cozengereza cidwalitsa mtima;Koma pakufika cifuniroco ndico mtengo wa moyo.
13. Wonyoza mau adziononga yekha;Koma woopa malangizo adzalandira mphotho.
14. Malamulo a wanzeru ndiwo kasupe wa moyo,Apatutsa ku misampha ya imfa.
15. Nzeru yabwino ipatsa cisomo;Koma njira ya aciwembu iri makolokoto.
16. Yense wocenjera amacita mwanzeru:Koma wopusa aonetsa utsiru.
17. Mthenga wolakwa umagwa m'zoipa;Koma mtumiki wokhulupirika alamitsa.
18. Wokana mwambo adzasauka nanyozedwa;Koma wolabadira cidzudzulo adzalemekezedwa.
19. Cifuniro cikondweretsa moyo citacitidwa;Koma kusiya zoipa kunyansa opusa,
20. Ukayenda ndi anzeru udzakhala wanzeru:Koma mnzao wa opusa adzaphwetekedwa.
21. Zoipa zilondola ocimwa;Koma olungama adzalandira mphotho yabwino.
22. Wabwino asiyira zidzukulu zace colowa cabwino;Koma wocimwa angosungira wolungama cuma cace.
23. M'kulima kwa osauka muli zakudya zambiri;Koma zinazo zimaonongeka posowa ciweruzo.
24. Wolekereramwanace osammenya amuda;Koma womkonda amyambize kumlanga.
25. Wolungama adya nakhutitsa moyo wace;Koma mimba ya oipa idzasowa.