Mitu

  1. 1
  2. 2
  3. 3
  4. 4
  5. 5
  6. 6
  7. 7
  8. 8
  9. 9
  10. 10
  11. 11
  12. 12
  13. 13
  14. 14
  15. 15
  16. 16
  17. 17
  18. 18
  19. 19
  20. 20
  21. 21
  22. 22
  23. 23
  24. 24
  25. 25
  26. 26
  27. 27
  28. 28
  29. 29
  30. 30
  31. 31

Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Mwana wanzeru amamvera mwambo wa atate;Koma wonyoza samvera cidzudzulo.

2. Munthu adzadya zabwino ndi zipatso za m'kamwa mwace;Koma moyo wa aciwembu udzadya ciwawa.

3. Wogwira pakamwa pace asunga moyo wace;Koma woyasamula milomo yace adzaonongeka.

4. Moyo wa wolesi ukhumba osalandira kanthu;Koma moyo wa akhama udzalemera.

5. Wolungama ada mau onama;Koma woipa anyansa, nadzicititsa manyazi,

6. Cilungamo cicinjiriza woongoka m'njira;Koma udio ugwetsa wocimwa.

7. Alipo wodziyesa wolemera, koma alibe kanthu;Alipo wodziyesa wosauka, koma ali ndi cuma cambiri.

8. Ciombolo ca moyo wa munthu ndico cuma cace;Koma wosauka samva cidzudzulo.

9. Kuunika kwa olungama kukondwa;Koma nyali ya oipa idzazima.

10. Kudzikuza kupikisanitsa;Koma omwe anauzidwa uphungu ali ndi nzeru.

11. Cuma colandiridwa mokangaza cidzacepa;Koma wokundika ndi dzanja adzaona zocuruka.

12. Ciyembekezo cozengereza cidwalitsa mtima;Koma pakufika cifuniroco ndico mtengo wa moyo.

13. Wonyoza mau adziononga yekha;Koma woopa malangizo adzalandira mphotho.

14. Malamulo a wanzeru ndiwo kasupe wa moyo,Apatutsa ku misampha ya imfa.

15. Nzeru yabwino ipatsa cisomo;Koma njira ya aciwembu iri makolokoto.

16. Yense wocenjera amacita mwanzeru:Koma wopusa aonetsa utsiru.

17. Mthenga wolakwa umagwa m'zoipa;Koma mtumiki wokhulupirika alamitsa.

18. Wokana mwambo adzasauka nanyozedwa;Koma wolabadira cidzudzulo adzalemekezedwa.

19. Cifuniro cikondweretsa moyo citacitidwa;Koma kusiya zoipa kunyansa opusa,

20. Ukayenda ndi anzeru udzakhala wanzeru:Koma mnzao wa opusa adzaphwetekedwa.

21. Zoipa zilondola ocimwa;Koma olungama adzalandira mphotho yabwino.

22. Wabwino asiyira zidzukulu zace colowa cabwino;Koma wocimwa angosungira wolungama cuma cace.

23. M'kulima kwa osauka muli zakudya zambiri;Koma zinazo zimaonongeka posowa ciweruzo.

24. Wolekereramwanace osammenya amuda;Koma womkonda amyambize kumlanga.

25. Wolungama adya nakhutitsa moyo wace;Koma mimba ya oipa idzasowa.