1. Mkazi yense wanzeru amanga banja lace;Koma wopusa alipasula ndi manja ace.
2. Woyenda moongoka mtima aopa Yehova;Koma wokhota m'njira yace amnyoza,
3. M'kamwa mwa citsiru muli ntyole ya kudzikuza;Koma milomo ya anzeru Idzawasunga.
4. Popanda zoweta modyera muti see;Koma mphamvu ya ng'ombe icurukitsa phindu.
5. Mboni yokhulupirika sidzanama;Koma mboni yonyenga imalankhula zonama.
6. Wonyoza afunafuna nzeru osaipeza;Koma wozindikira saona bvuto m'kuphunzira.
7. Pita pamaso pa munthu wopusa,Sudzazindikira milomo yakudziwa.
8. Nzeru ya wocenjera ndiyo yakuti azindikire njira yace;Koma utsiru wa opusa ndiwo cinyengo.
9. Zitsiru zinyoza kuparamula;Koma mwa oongoka mtima muli ciyanjano.
10. Mtima udziwa kuwawa kwace kwace;Mlendo sadudukira ndi cimwemwe cace.
11. Nyumba ya oipa idzapasuka;Koma hema wa oongoka mtima adzakula.
12. Iripo njira yooneka kwa mwamuna ngati yoongoka;Koma matsiriziro ace ndi njira za imfa.
13. Ngakhale m'kuseka mtima uwawa;Ndipo matsiriziro a ciphwete ndi cisoni.
14. Wobwerera m'mbuyo m'mtima adzakhuta njira zace;Koma munthu wabwino adzakhuta za mwa iye yekha.
15. Wacibwana akhulupirira mau onse;Koma wocenjera asamalira mayendedwe ace.
16. Wanzeru amaopa nasiya zoipa;Koma wopusa amanyada osatekeseka.
17. Wokangaza kukwiya adzacita utsiru;Ndipo munthu wa ziwembu adzadedwa.
18. Acibwana amalandira colowa ca utsiru;Koma ocenjera amabvala nzeru ngati korona.
19. Oipa amagwadira abwino,Ndi ocimwa pa makomo a olungama.
20. Waumphawi adedwa ndi anzace omwe;Koma akukonda wolemera acuruka.
21. Wonyoza anzace acimwa;Koma wocitira osauka cifundo adala.
22. Kodi oganizira zoipa sasocera?Koma akuganizira zabwino adzalandira cifundo ndi ntheradi.
23. M'nchito zonse muli phindu;Koma kulankhula-lankhula kungopatsa umphawi.
24. Korona wa anzeru ndi cuma cao;Utsiru wa opusa ndiwo utsiru.
25. Mboni yoona imalanditsa miyoyo;Koma wolankhula zonama angonyenga.
26. Wakuopa Yehova akhulupirira kolimba;Ndipo ana ace adzakhala ndi pothawirapo.
27. Kuopa Yehova ndiko kasupe wa moyo,Kupatutsa ku misampha ya imfa.
28. Mu unyinji wa anthu muli ulemu wa mfumu;Koma popanda anthu kalonga aonongeka.
29. Wosakwiya msanga apambana kumvetsa;Koma wansontho akuza utsiru.
30. Mtima wabwino ndi moyo wa thupi;Koma nsanje ibvunditsa mafupa.
31. Wotsendereza aumphawi atonza Mlengi wace;Koma wocitira wosauka cifundo amlemekeza.
32. Wocimwa adzakankhidwa m'kuipa kwace;Koma wolungama akhulupirirabe pomwalira,
33. Nzeru ikhalabe m'mtima wa wozindikira,Nidziwika pakati pa opusa.
34. Cilungamo cikuza mtundu wa anthu;Koma cimo licititsa pfuko manyazi.
35. Mfumu ikomera mtima kapolo wocita mwanzeru;Koma idzakwiyira wocititsa manyazi.