Mitu

  1. 1
  2. 2
  3. 3
  4. 4
  5. 5
  6. 6
  7. 7
  8. 8
  9. 9
  10. 10
  11. 11
  12. 12
  13. 13
  14. 14
  15. 15
  16. 16
  17. 17
  18. 18
  19. 19
  20. 20
  21. 21
  22. 22
  23. 23
  24. 24
  25. 25
  26. 26
  27. 27
  28. 28
  29. 29
  30. 30
  31. 31

Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Mkazi yense wanzeru amanga banja lace;Koma wopusa alipasula ndi manja ace.

2. Woyenda moongoka mtima aopa Yehova;Koma wokhota m'njira yace amnyoza,

3. M'kamwa mwa citsiru muli ntyole ya kudzikuza;Koma milomo ya anzeru Idzawasunga.

4. Popanda zoweta modyera muti see;Koma mphamvu ya ng'ombe icurukitsa phindu.

5. Mboni yokhulupirika sidzanama;Koma mboni yonyenga imalankhula zonama.

6. Wonyoza afunafuna nzeru osaipeza;Koma wozindikira saona bvuto m'kuphunzira.

7. Pita pamaso pa munthu wopusa,Sudzazindikira milomo yakudziwa.

8. Nzeru ya wocenjera ndiyo yakuti azindikire njira yace;Koma utsiru wa opusa ndiwo cinyengo.

9. Zitsiru zinyoza kuparamula;Koma mwa oongoka mtima muli ciyanjano.

10. Mtima udziwa kuwawa kwace kwace;Mlendo sadudukira ndi cimwemwe cace.

11. Nyumba ya oipa idzapasuka;Koma hema wa oongoka mtima adzakula.

12. Iripo njira yooneka kwa mwamuna ngati yoongoka;Koma matsiriziro ace ndi njira za imfa.

13. Ngakhale m'kuseka mtima uwawa;Ndipo matsiriziro a ciphwete ndi cisoni.

14. Wobwerera m'mbuyo m'mtima adzakhuta njira zace;Koma munthu wabwino adzakhuta za mwa iye yekha.

15. Wacibwana akhulupirira mau onse;Koma wocenjera asamalira mayendedwe ace.

16. Wanzeru amaopa nasiya zoipa;Koma wopusa amanyada osatekeseka.

17. Wokangaza kukwiya adzacita utsiru;Ndipo munthu wa ziwembu adzadedwa.

18. Acibwana amalandira colowa ca utsiru;Koma ocenjera amabvala nzeru ngati korona.

19. Oipa amagwadira abwino,Ndi ocimwa pa makomo a olungama.

20. Waumphawi adedwa ndi anzace omwe;Koma akukonda wolemera acuruka.

21. Wonyoza anzace acimwa;Koma wocitira osauka cifundo adala.

22. Kodi oganizira zoipa sasocera?Koma akuganizira zabwino adzalandira cifundo ndi ntheradi.

23. M'nchito zonse muli phindu;Koma kulankhula-lankhula kungopatsa umphawi.

24. Korona wa anzeru ndi cuma cao;Utsiru wa opusa ndiwo utsiru.

25. Mboni yoona imalanditsa miyoyo;Koma wolankhula zonama angonyenga.

26. Wakuopa Yehova akhulupirira kolimba;Ndipo ana ace adzakhala ndi pothawirapo.

27. Kuopa Yehova ndiko kasupe wa moyo,Kupatutsa ku misampha ya imfa.

28. Mu unyinji wa anthu muli ulemu wa mfumu;Koma popanda anthu kalonga aonongeka.

29. Wosakwiya msanga apambana kumvetsa;Koma wansontho akuza utsiru.

30. Mtima wabwino ndi moyo wa thupi;Koma nsanje ibvunditsa mafupa.

31. Wotsendereza aumphawi atonza Mlengi wace;Koma wocitira wosauka cifundo amlemekeza.

32. Wocimwa adzakankhidwa m'kuipa kwace;Koma wolungama akhulupirirabe pomwalira,

33. Nzeru ikhalabe m'mtima wa wozindikira,Nidziwika pakati pa opusa.

34. Cilungamo cikuza mtundu wa anthu;Koma cimo licititsa pfuko manyazi.

35. Mfumu ikomera mtima kapolo wocita mwanzeru;Koma idzakwiyira wocititsa manyazi.