1. Mayankhidwe ofatsa abweza mkwiyo;Koma mau owawitsa aputa msunamo.
2. Lilime la anzeru linena bwino zomwe adziwa;Koma m'kamwa mwa opusa mutsanulira utsiru.
3. Maso a Yehova ali ponseponse,Nayang'anira oipa ndi abwino.
4. Kuciza lilime ndiko mtengo wa moyo;Koma likakhota liswa moyo.
5. Citsiru cipeputsa mwambo wa atate wace;Koma wosamalira cidzudzulo amacenjera.
6. M'nyumba ya wolungama muli katundu wambiri;Koma m'phindu la woipa muli bvuto,
7. Milomo ya anzeru iwanditsa nzeru,Koma mtima wa opusa suli wolungama.
8. Nsembe ya oipa inyansa Yehova;Koma pemphero la oongoka mtima limkondweretsa.
9. Njira ya oipa inyansa Yehova;Koma akonda wolondola cilungamo.
10. Wosiya njira adzalangidwa mowawa;Wakuda cidzudzulo adzafa.
11. Kumanda ndi kucionongeko kuli pamaso pa Yehova;Koposa kotani nanga mitima ya ana a anthu?
12. Wonyoza sakonda kudzudzulidwa,Samapita kwa anzeru.
13. Mtima wokondwa usekeretsa nkhope;Koma moyo umasweka ndi zowawa za m'mtima.
14. Mtima wa wozindikira ufunitsa kudziwa;Koma m'kamwa mwa opusa mudya utsiru.
15. Masiku onse a wosauka ali oipa;Koma wokondwera mtima ali ndi phwando losatha.
16. Zapang'ono, ulikuopa Yehova,Zipambana ndi katundu wambiri pokhala phokoso,
17. Kudya masamba, pali cikondano,Kuposa ng'ombe yonenepa pali udani.
18. Munthu wozaza aputa makani;Koma wosakwiya msanga atonthoza makangano.
19. Mayendedwe a wolesi akunga Hnga laminga,Koma njira ya oongoka mtima iundidwa ngati mseu.
20. Mwana wanzeru akondweretsa atate wace;Koma munthu wopusa apeputsa amace.
21. Wosowa nzeru akondwera ndi utsiru;Koma munthu wozindikira aongola mayendedwe ace.
22. Zolingalira zizimidwa popanda upoKoma pocuruka aphungu zikhazikika.
23. Munthu akondwera ndi mayankhidwe a m'kamwa mwace;Ndi mau a pa nthawi yace kodi sali abwino?
24. Anzeru ayesa njira yamoyo yokwerakwera,Kuti apambuke kusiya kunsi kwa manda.
25. Yehova adzapasula nyumba ya wonyada;Koma adzalembera mkazi wamasiye malire ace,
26. Ziwembu zoipa zinyansa Yehova;Koma oyera mtima alankhula mau okondweretsa.
27. Wopindula monyenga abvuta nyumba yace;Koma wakuda mitulo adzakhala ndi moyo.
28. Mtima wa wolungama uganizira za mayankhidwe;Koma m'kamwa mwa ocimwa mutsanulira zoipa.
29. Yehova atarikira oipa;Koma pemphero la olungama alimvera.
30. Kuunika kwa maso kukondweretsa mtima;Ndipo pomveka zabwino mafupa amatenga uwisi.
31. Khutu lomvera cidzudzulo ca moyoLidzakhalabe mwa anzeru.
32. Wokana mwambo apeputsa moyo wace;Koma wosamalira cidzudzulo amatenga nzeru.
33. Kuopa Yehova ndiko mwambo wanzeru;Ndipo cifatso citsogolera ulemu.