Mitu

  1. 1
  2. 2
  3. 3
  4. 4
  5. 5
  6. 6
  7. 7
  8. 8
  9. 9
  10. 10
  11. 11
  12. 12
  13. 13
  14. 14
  15. 15
  16. 16
  17. 17
  18. 18
  19. 19
  20. 20
  21. 21
  22. 22
  23. 23
  24. 24
  25. 25
  26. 26
  27. 27
  28. 28
  29. 29
  30. 30
  31. 31

Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Wokonda mwambo akonda kudziwa;Koma wakuda cidzudzulo apulukira.

2. Yehova akomera mtima munthu wabwino;Koma munthu wa ziwembu amtsutsa,

3. Munthu sadzakhazikika ndi udio,Muzu wa olungama sudzasunthidwa.

4. Mkazi wodekha ndiye korona wa mwamuna wace;Koma wocititsa manyazi akunga cobvunditsa mafupa a mwamunayo.

5. Maganizo a olungama ndi ciweruzo;Koma uphungu wa oipa unyenga.

6. Mau a oipa abisalira mwazi;Koma m'kamwa mwa olungama muwalanditsa.

7. Oipa amagwa kuli zi;Koma banja la olungama limaimabe.

8. Munthu amatamandidwa monga mwa nzeru yace;Koma wokhota mtima adzanyozedwa.

9. Wonyozedwa, amene ali ndi kapolo,Aposa wodzikuza, amene asowa zakudya.

10. Wolungama asamalira moyo wa coweta cace;Koma cifundo ca oipa ndi nkhanza.

11. Zakudyazikwanira wolima minda yace;Koma wotsata anthu opanda pace asowa nzeru.

12. Woipa akhumba cokodwa ndi amphulupulu;Koma muzu wa olungama umabala zipatso.

13. M'kulakwa kwa milomo muli msampha woipa;Koma wolungama amaturuka m'mabvuto.

14. Munthu amakhuta zabwino ndi zipatso za m'kamwa mwace;Zocita za manja ace zidzabwezedwa kwa iye.

15. Njira ya citsiru nlolungama pamaso pace pace;Koma wanzeru amamvera uphungu.

16. Mkwiyo wa citsiru udziwika posacedwa;Koma wanzeru amabisa manyazi.

17. Wolankhula ntheradi aonetsa cilungamo;Koma mboni yonama imanyenga.

18. Alipo wonena mwansontho ngati kupyoza kwa lupanga;Koma lilime la anzeru lilamitsa.

19. Mlomo wa ntheradi ukhazikika nthawi zonse;Koma lilime lonama likhala kamphindi.

20. Cinyengo ciri m'mitima ya oganizira zoipa;Koma aphungu a mtendere amakondwa.

21. Palibe bvuto lidzagwera wolungama;Koma amphulupulu adzadzazidwa ndi zoipa,

22. Milomo yonama inyansa Yehova;Koma ocita ntheradi amsekeretsa.

23. Munthu wanzeru abisa zomwe adziwa;Koma mtima wa opusa ulalikira utsiru.

24. Dzanja la akhama lidzalamulira;Koma wolesi adzakhala ngati kapolo,

25. Nkhawa iweramitsa mtima wa munthu;Koma mau abwino aukondweretsa.

26. Wolungama atsogolera mnzace;Koma njira ya oipa iwasokeretsa.

27. Wolesi samaocha nyama yace anaigwira;Koma wolungama amalandira cuma copambana ca anthu.

28. M'khwalala la cilungamo muli moyo;M'njira ya mayendedwe ace mulibe imfa.