1. Wokonda mwambo akonda kudziwa;Koma wakuda cidzudzulo apulukira.
2. Yehova akomera mtima munthu wabwino;Koma munthu wa ziwembu amtsutsa,
3. Munthu sadzakhazikika ndi udio,Muzu wa olungama sudzasunthidwa.
4. Mkazi wodekha ndiye korona wa mwamuna wace;Koma wocititsa manyazi akunga cobvunditsa mafupa a mwamunayo.
5. Maganizo a olungama ndi ciweruzo;Koma uphungu wa oipa unyenga.
6. Mau a oipa abisalira mwazi;Koma m'kamwa mwa olungama muwalanditsa.
7. Oipa amagwa kuli zi;Koma banja la olungama limaimabe.
8. Munthu amatamandidwa monga mwa nzeru yace;Koma wokhota mtima adzanyozedwa.
9. Wonyozedwa, amene ali ndi kapolo,Aposa wodzikuza, amene asowa zakudya.
10. Wolungama asamalira moyo wa coweta cace;Koma cifundo ca oipa ndi nkhanza.
11. Zakudyazikwanira wolima minda yace;Koma wotsata anthu opanda pace asowa nzeru.
12. Woipa akhumba cokodwa ndi amphulupulu;Koma muzu wa olungama umabala zipatso.
13. M'kulakwa kwa milomo muli msampha woipa;Koma wolungama amaturuka m'mabvuto.
14. Munthu amakhuta zabwino ndi zipatso za m'kamwa mwace;Zocita za manja ace zidzabwezedwa kwa iye.
15. Njira ya citsiru nlolungama pamaso pace pace;Koma wanzeru amamvera uphungu.
16. Mkwiyo wa citsiru udziwika posacedwa;Koma wanzeru amabisa manyazi.
17. Wolankhula ntheradi aonetsa cilungamo;Koma mboni yonama imanyenga.
18. Alipo wonena mwansontho ngati kupyoza kwa lupanga;Koma lilime la anzeru lilamitsa.
19. Mlomo wa ntheradi ukhazikika nthawi zonse;Koma lilime lonama likhala kamphindi.
20. Cinyengo ciri m'mitima ya oganizira zoipa;Koma aphungu a mtendere amakondwa.
21. Palibe bvuto lidzagwera wolungama;Koma amphulupulu adzadzazidwa ndi zoipa,
22. Milomo yonama inyansa Yehova;Koma ocita ntheradi amsekeretsa.
23. Munthu wanzeru abisa zomwe adziwa;Koma mtima wa opusa ulalikira utsiru.
24. Dzanja la akhama lidzalamulira;Koma wolesi adzakhala ngati kapolo,
25. Nkhawa iweramitsa mtima wa munthu;Koma mau abwino aukondweretsa.
26. Wolungama atsogolera mnzace;Koma njira ya oipa iwasokeretsa.
27. Wolesi samaocha nyama yace anaigwira;Koma wolungama amalandira cuma copambana ca anthu.
28. M'khwalala la cilungamo muli moyo;M'njira ya mayendedwe ace mulibe imfa.