Mitu

  1. 1
  2. 2
  3. 3
  4. 4
  5. 5
  6. 6
  7. 7
  8. 8
  9. 9
  10. 10
  11. 11
  12. 12
  13. 13
  14. 14
  15. 15
  16. 16
  17. 17
  18. 18
  19. 19
  20. 20
  21. 21
  22. 22
  23. 23
  24. 24
  25. 25
  26. 26
  27. 27
  28. 28
  29. 29
  30. 30
  31. 31

Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 2 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

Ukoma ndi phindu tace la Nzeru

1. Mwananga, ukalandira mau anga,Ndi kusunga malamulo anga;

2. Kucherera makutu ako kunzeru,Kulozetsa mtima wako kukuzindikira;

3. Ukaitananso luntha,Ndi kupfuulira kuti ukazindikire;

4. Ukaifunafuna ngati siliva,Ndi kuipwaira ngati cuma cobisika;

5. Pompo udzazindikira kuopa YehovaNdi kumdziwadi Mulungu.

6. Pakuti Yehova apatsa nzeru;Kudziwa ndi kuzindikira kuturuka m'kamwa mwace;

7. Iye asungira oongoka mtima nzeru yeniyeni;Ndiye cikopa ca oyenda molunjika;

8. Kuti acinjirize njira za ciweruzo,Nadikire khwalala la opatulidwa ace.

9. Pamenepo udzazindikira cilungamo ndi ciweruzo,Zolunjika ndi mayendedwe onse abwino.

10. Pakuti nzeru idzalowa m'mtima mwako,Moyo wako udzakondwera ndi kudziwa,

11. Kulingalira kudzakudikira,Kuzindikira kudzakucinjiriza;

12. Kukupulumutsa ku njira yoipa,Kwa anthu onena zokhota;

13. Akusiya mayendedwe olungama,Akayende m'njira za mdima;

14. Omwe asangalala pocita zoipa,Nakondwera ndi zokhota zoipa;

15. Amene apotoza njira zao,Nakhotetsa mayendedwe ao;

16. Nzeru idzakupulumutsa kwa mkazi waciwerewere,Kwa mkazi wacilendo wosyasyalika ndi mau ace;

17. Wosiya bwenzi la ubwana wace,Naiwala cipangano ca Mulungu wace;

18. Nyumba yace itsikira kuimfa,Ndi mayendedwe ace kwa akufa;

19. Onse akunka kwa iye sabweranso,Safika ku njira za moyo;

20. Nzeru idzakuyendetsa m'njira ya anthu abwino,Kuti usunge mayendedwe a olungama.

21. Pakuti oongoka mtima adzakhala m'dziko,Angwiro nadzatsalamo.

22. Koma oipa adzalikhidwa m'dziko,Aciwembu adzazulidwamo.