Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 5:10-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Ndipo Elisa anamtumira mthenga, ndi kuti, Kasambe m'Yordano kasanu ndi kawiri, ndi mnofu wako udzabwerera momwe, nudzakhala wokonzeka.

11. Koma Namani adapsa mtima, nacoka, nati, Taona, ndinati m'mtima mwanga, kuturuka adzanditurukira, nadzaima ndi kuitana pa dzina la Yehova Mulungu wace, ndi kuweyula dzanja lace pamalopo, ndi kuciritsa wakhateyo.

12. Nanga Abana ndi Faripara, mitsinje ya Damasiko, siiposa kodi madzi onse a m'Israyeli? ndilekerenji kukasamba m'mwemo, ndi kukonzeka? Natembenuka, nacoka morunda.

13. Pamenepo anyamata ace anasendera, nanena naye, nati, Atate wanga, mneneri akadakuuzani cinthu cacikuru, simukadacicita kodi? koposa kotani nanga ponena iye, Samba, nukonzeke?

14. Potero anatsika, namira m'Yordano kasanu ndi kawiri, monga adanena munthu wa Mulunguyo; ndi mnofu wace unabwera monga mnofu wa mwana wamng'ono, nakonzeka.

15. Pamer nepo anabwerera kwa munthu wa Mulungu iye ndi gulu lace lonse, nadzaima pamaso pace, nati, Taonani, tsopano ndidziwa kuti palibe Mulungu pa dziko lonse lapansi, koma kwa Israyeli ndiko; ndipo tsopano, mulandire cakukuyamikani naco kwa mnyamata wanu.

16. Koma anati, Pali Yehova, amene ndiima pamaso pace, sindidzalandira kanthu. Ndipo anamkangamiza acilandire, koma anakana.

17. Ndipo Namani anati, Mukakana, andipatse akatundu a dothi osenza nyuru ziwiri; pakuti mnyamata wanu sadzaperekanso nsembe yopsereza kapena yophera kwa milungu yina, koma kwa Yehova.

18. Yehova akhululukire mnyamata wanu mwa ici; akalowa mbuye wanga m'nyumba ya Rimoni kulambiramo, nakatsamira pa dzanja langa, nanenso ndikagwadira m'nyumba ya Rimoni, pakugwadira ine m'nyumba ya Rimoni, Yehova akhululukire mnyamata wanu mwa ici.

19. Ndipo ananena naye, Pita mumtendere. Ndipo anacoka, nayenda kanthawi.

20. Koma Gehazi, mnyamata wa Elisa, munthu wa Mulungu, anati, Taona, mbuye wanga analekera Namani uyu wa ku Aramu osalandira m'manja ace cimene anabwera naco; pali Yehova, ndidzathamangira ndi kulandira kanthu kwa iye.

21. Motero Gehazi anatsata Namani. Ndipo pamene Namani anaona wina alikumthamangira, anatsika pagareta kukomana naye, nati, Nkwabwino kodi?

22. Nati, Kuli bwino. Mbuye wanga wandituma, ndi kuti, Taonani, andifikira tsopano apa anyamata awiri a ana a aneneri, ocokera ku mapiri a Efraimu; muwapatse talente wa siliva, ndi zobvala zosintha ziwiri.

23. Nati Namani, Viole ulandire matalente awiri. Namkangamiza namanga matalente awiri a siliva m'matumba awiri, ndi zobvala zosintha ziwiri, nasenzetsa anyamata ace awiri; iwo anatsogola atazisenza.

24. Ndipo pamene anafika kumsanje anazilandira m'manjamwao, naziika m'nyumba; nauza anthuwo amuke, iwo nacoka.

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 5