Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 16:5-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Ndipo ku khama la ana a Israyeli atenge atonde awiri akhale a nsembe yaucimo, ndi nkhosa yamphongo imodzi ikhale ya nsembe yopsereza.

6. Ndipo Aroni abwere nayo ng'ombe ya nsembe yaucimo, ndiyo yace yace, nacite codzitetezera iye yekha, ndi mbumba yace.

7. Ndipo atenge mbuzi ziwirizo naziimike pamaso pa Yehova pakhomo pa cihema cokomanako.

8. Ndipo Aroniayesemaere pa mbuzi ziwirizo; maere amodzi kwa Yehova, ndi amodzi kwa Azazeli.

9. Ndipo Aroni abwere nayo mbuzi imene adaigwera maere a Yehova, naiyese nsembe yaucimo.

10. Koma mbuzi imene adaigwera maere a Azazeli, aiike yamoyo pamaso pa Yehova, kuti acite nayo cotetezera, kuitumiza kucipululu ikhale ya Azazeli.

11. Ndipo Aroni abwere nayo ng'ombe ya nsembe yaucimo, ndiyo yace yace, nadzitetezere iye yekha, ndi mbumba yace, ndi kupha ng'ombe ya nsembe yaucimo ndiyo yace yace;

12. natenge mbale ya zofukiza yodzala ndi makara amoto, kuwacotsa pa guwa la nsembe, pamaso pa Yehova, ndi manja ace odzala ndi cofukiza copera ca pfungo lokoma, nalowe nayo m'tseri mwa nsaru yocinga;

13. naike cofukizaco pamoto pamaso pa Yehova, kuti mtambo wa cofukiza ciphimbe cotetezerapo cokhala pamboni, kuti angafe.

14. Ndipo atengeko mwazi wa ng'ombeyo, ndi kuuwaza ndi cala cace pacotetezerapo, mbali ya kum'mawa; nawaze mwazi ndi cala cace cakuno ca cotetezerapo kasanu ndi kawiri.

15. Pamenepo aiphe mbuzi ya nsembe yaucimo, ndiyo yophera anthu, nalowe nao mwazi wace m'tseri mwa nsaru yocinga, nacite nao mwazi wace monga umo anacitira ndi mwazi wa ng'ombe, nauwaze pacotetezerapo ndi cakuno ca cotetezerapo;

16. nacitire cotetezera malo opatulika, cifukwa ca kudetsedwa kwa ana a Israyeli, ndi cifukwa ca zolakwa zao, monga mwa zocimwa zao zonse; nacitire cihema cokomanako momwemo, cakukhala nao pakati pa zodetsa zao.

17. Ndipo musakhale munthu m'cihema cokomanako pakulowa iye kucita cotetezera m'malo opatulika, kufikira aturuka, atacita cotetezera yekha, ndi mbumba yace, ndi msonkhano wonse wa Israyeli.

18. Ndipo aturukire guwa la nsembe lokhala pamaso pa Yehova ndi kulicitira cotetezera; natengeko mwazi wa ng'ombeyo, ndi mwazi wa mbuziyo, ndi kuupaka pa nyanga za guwa la nsembe pozungulira.

19. Ndipo awazepo mwazi wina ndi cala cace kasanu ndi katatu; ndi kuliyeretsa ndi kulipatula kulicotsera zodetsa za ana a Israyeli.

20. Ndipo atatha kucitira cotetezera malo opatulika, ndi cihema cokomanako, ndi guwa la nsembe, abwere nayo mbuzi yamoyo;

21. ndipo Aroni aike manja ace onse awiri pamutu pa mbuzi yamoyo, ndi kubvomereza pa iyo mphulupulu zonse za ana a Israyeli, ndi zolakwa zao zonse, monga mwa zocimwa zao zonse; naike izi pamutu pa mbuziyo, ndi kuitumiza kucipululu ndi dzanja la munthu wompangiratu,

Werengani mutu wathunthu Levitiko 16