Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 12:11-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Ndipo muziidya cotero: okwinda m'cuuno, nsapato zanu pa mapazi anu ndodo yanu m'dzanja lanu, ndipo muziidya msanga; ndiye Paskha wa Yehova.

12. Pakuti ndidzapita pakati pa dziko la Aigupto usiku womwewo, ndi kukantha ana oyamba onse m'dziko la Aigupto, anthu ndi zoweta; ndipo ndidzacita maweruzo pa milungu yonse ya Aigupto; Ine ndine Yehova.

13. Ndipo mwaziwo udzakhala cizindikilo kwa inu pa nyumba zimene mukhalamo; pamene ndiona mwaziwo ndidzapitirira inu, ndipo sipadzakhala mliri wakukuonongani, pakukantha Ine dziko la Aigupto,

14. Ndipo tsiku lino lidzakhala kwa inu cikumbutso, muzilisunga la madyerero a Yehova; ku mibadwo yanu muzilisunga la madyerero, likhale lemba losatha.

15. Masiku asanu ndi awiri muzidya mkate wopanda cotupitsa; lingakhale tsiku loyamba muzicotsa cotupitsa m'nyumba zanu; pakuti ali yense wakudya mkate wa cotupitsa kuyambira tsiku loyamba kufikira tsiku lacisanu ndi ciwiri, munthu amene adzasadzidwa kwa Israyeli.

16. Ndipo tsiku loyamba kukhale kusonkhana kopatulika, ndi tsiku lacisanu ndi ciwiri kukhalenso kusonkhana kopatulika; pasacitike nchito masikuwo, zokhazi zakudya anthu onse ndizo muzicita.

17. Ndipo muzisunga madyerero a mkate wopanda cotupitsa; pakuti tsiku lomwe lino ndinaturutsa makamu anu m'dziko la Aigupto; cifukwa cace muzisunga tsiku lino m'mibadwo yanu, lemba losatha.

18. Mwezi woyamba, tsiku lace lakhumi ndi cinai madzulo ace, muzidya mkate wopanda cotupitsa, kufikira tsiku la makumi awiri mphambu limodzi la mwezi, madzulo ace.

19. Cisapezeke cotupitsa m'nyumba zanu masiku asanu ndi awiri; pakuti ali yense wakudya kanthu ka cotupitsa, munthuyo adzasadzidwa ku msonkhano wa Israyeli, angakhale ndiye mlendo kapena wobadwa m'dziko.

20. Musadye kanthu ka cotupitsa; mokhala inu monse muzidya mkate wopandacotupitsa.

21. Pamenepo Mose anaitana akuru onse a Israyeli, nanena nao, Pitani, dzitengereni ana a nkhosa monga mwa mabanja anu, nimuphere Paskha.

22. Ndipo muzitenga mpukutu wa hisope, ndi kuubviika m'mwazi uli m'mbale, ndi kupaka mwazi uli m'mbalemo pa mphuthu ya pamwamba ndi pambali; koma inu, asaturuke munthu pakhomo pa nyumba yace kufikira m'mawa.

23. Pakuti Yehova adzapita pakatipo kukantha Aaigupto; koma pamene adzaona mwaziwo pa mphuthu pamwamba ndi za pambali, Yehova adzapitirira pakhomopo, osalola woonongaalowe m'nyumba zanu kukukanthani.

24. Ndipo muzisunga cinthu ici cikhale lemba la kwa inu, ndi kwa ana anu ku nthawi zonse.

25. Ndipo kudzakhala, pamene mulowa m'dziko limene Yehova adzakupatsani, mensa analankhula, muzisunga kutumikira kumeneku.

26. Ndipo kudzakhala, pamene ana anu adzanena ndi inu, Kutumikiraku muli nako nkutani?

Werengani mutu wathunthu Eksodo 12