Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 8:36-55 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

36. pamenepo mverani Inu m'Mwamba, ndi kukhululukira cimo la akapolo anu, ndi la, anthu anu Aisrayeli; pakuti muwaphunzitsa njira yokoma ayenera kuyendamo, ndi kupatsa mvula pa: dziko lanu, limene munawapatsa anthu anu likhale colowa cao.

37. M'dziko mukakhala odala, mukakhala mliri, mlaza, cinoni, dzombe, kapena kapuci, adani ao akawamangira misasa m'dziko la midzi yao, mukakhala mliri uti wonse, kapena nthenda;

38. tsono pempho ndi pembedzero liri lonse akalipempha munthu ali yense, kapena anthu anu onse Aisrayeli, pakuzindikira munthu yense cinthenda ca mtima wa iye yekha, ndi kutambasulira manja ace ku nyumba yino;

39. pamenepo mverani Inu m'Mwamba mokhala Inu, ndi kukhululukira, ndi kucita, ndi kubwezera munthu yense monga njira zace zonse, amene Inu mumdziwa mtima wace, popeza Inu, Inu nokha, mudziwa mitima ya ana onse a anthu;

40. kuti aope Inu masiku onse akukhala iwowo m'dziko limene Inu munapatsa makolo ao.

41. Ndiponso kunena za mlendo, wosati wa anthu anu Aisrayeli, koma wakufumira m'dziko lakutali cifukwa ca dzina lanu,

42. popeza adzamva za dzina lanu lalikuru ndi dzanja lanu lamphamvu ndi mkono wanu wotambasuka; akabwera iyeyo nadzapemphera molunjika ku nyumba yino;

43. mverani Inu m'Mwamba mokhala Inu, ndipo citani monga mwa zonse mlendoyo azipempha kwa Inu; kuti anthu onse a dziko lapansi adziwe dzina lanu, kuopa Inu, monga amatero anthu anu Aisrayeli, ndi kuti adziwe kuti nyumba yino ndaimangayi yachedwa dzina lanu.

44. Akaturuka anthu anu kukayambana nkhondo ndi adani ao, kumene konse inu mudzawatuma, ndipo akapemphera kwa Yehova molunjika ku mudzi uno munausankha Inu, ndi ku nyumba ndamangira dzina lanu;

45. pamenepo mverani Inu m'Mwamba pempho ndi pembedzero lao, ndi kulimbitsa mlandu wao.

46. Akacimwira Inu, popeza palibe munthu wosacimwa, ndipo mukakwiya nao ndi kuwapereka kwa adani, kuti iwo awatenge ndende kumka nao ku dziko la adani, ngati kutali kapena kufupi,

47. ndipo akakumbukila mitima yao, ali kudziko kumene anatengedwa ukapolo, nakalapa, nakapembedza inu m'dziko la iwo anawatenga ndende, ndi kuti, Tacimwa, ndipo tacita mphulupulu, tacita moipa;

48. ndipo akabwerera kwa Inu ndi mtima wao wonse ndi moyo wao wonse, m'dziko la adani ao adawatenga ndendewo, ndipo akapemphera kwa Inu molunjika ku dziko lao munapatsa makolo aolo, ku mudzi munausankha Inu, ndi kunyumba ndamangira dzina lanu;

49. pamenepo mverani Inu pemphero ndi pembedzero lao m'Mwamba mokhala Inumo, ndi kulimbitsa mlandu wao,

50. ndi kukhululukira anthu anu adacimwira Inu ndi mphulupulu zao zonse adaparamula nazo kwa Inu; ndipo muwacititsire cifundo iwo amene anawagwira ndende, kuti awacitire cifundo;

51. pakuti awa ndi anthu anu ndithu, ndi colowa canu cimene munaturutsa m'Aigupto, m'kati mwa ng'anjo ya citsulo;

52. kuti maso anu akatsegukire pembedzero la kapolo wanu ndi pembedzero la anthu anu Aisrayeli, kuwamveram'menemonseakapfuula kwa Inu.

53. Popeza Inu munawapatula pa anthu onse a pa dziko lapansi akhale colowa canu, monga munanena ndi dzanja la Mose mtumiki wanu, pamene munaturutsa makolo athu m'Aigupto, Yehova Mulungu Inu.

54. Ndipo kunali kuti atatsiriza Solomo kupemphera kwa Yehova pemphero ndi pembedzero lino lonse, ananyamuka ku guwa la nsembe la Yehova pomwe analikugwada pa mabondo ace, ndi manja ace otambasulira kumwamba.

55. Naimirira, nadalitsa msonkhano wonse wa Israyeli ndi mau okweza, nati,

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 8