Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 29:14-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Ndipo ndidzapezedwa ndi inu, ati Yehova, ndidzabwezanso undende wanu, ndipo ndidzasonkhanitsa inu kwa mitundu yonse, ndi kumalo konse kumene ndinakupitikitsirani inu, ati Yehova; ndipo ndidzakubwezeraninso kumalo kumene ndinakutengani inu andende.

15. Pakuti mwati, Yehova watiutsira ife aneneri m'Babulo.

16. Pakuti Yehova atero za mfumu imene ikhala pa mpando wacifumu wa Davide, ndi za anthu onse amene akhala m'mudzi uno, abale anu amene sanaturukira pamodzi ndiinu kundende;

17. Yehova wa makamu atero: Taonani, ndidzatuma pa iwo lupanga, ndi njala, ndi caola, ndipo ndidzayesa iwo onga nkhuyu zoola, zosadyeka, pokhala nzoipa.

18. Ndipo ndidzatsata iwe ndi lupanga, ndi njala, ndi caola, ndipo ndidzawapereka akhale oopsyetsa m'maufumu onse a dziko la pansi, akhale citemberero, ndi codabwitsa, ndi cotsonyetsa, ndi citonzo, kwa mitundu yonse kumene ndinawapitikitsirako;

19. cifukwa sanamvera mau anga, ati Yehova, amene ndinawatumizira ndi atumiki anga aneneri, ndi kuuka mamawa ndi kuwatuma, koma munakana kumva, ati Yehova.

20. Pamenepo tamvani inu mau a Yehova, inu nonse a m'ndende, amene ndacotsa m'Yerusalemu kunka ku Babulo.

21. Atero Yehova wa makamu, Mulungu wa Israyeli, za Ahabu mwana wace wa Koliya, ndi za Zedekiya mwana wace wa Maseya, amene anenera zonama m'dzina langa: Taonani, Ndidzawapereka m'dzanja la Nebukadirezara mfumu ya ku Babulo; ndipo Iye adzawapha pamaso panu;

22. ndipo am'nsinga onse a Yuda amene ali m'Babulo adzatemberera pali iwo, kuti, Yehova akucitire iwe monga Zedekiya ndi Ahabu, amene mfumu ya ku Babulo inaoca m'moto;

23. cifukwa anacita zopusa m'Israyeli, nacita cigololo ndi akazi a anansi ao, nanena mau onama m'dzina langa, amene ndinawauza kuti asanene; Ine ndine wodziwa, ndi mboni, ati Yehova.

24. Ndipo za Semaya Mnehelamu uzinena, kuti,

25. Atero Yehova wa makamu, Mulungu wa Israyeli, kuti, Cifukwa watumiza akalata m'dzina lako iwe mwini kwa anthu onse amene akhala ku Yerusalemu, ndi kwa Zefaniya mwana wace wa Maseya wansembe, ndi kwa ansembe onse, kuti.

26. Yehova anakuyesa iwe wansembe m'malo mwa Yehoyada wansembe, kuti iwe ndi anzako mudzakhale akapitao m'nyumba ya Yehova, oyang'anira munthu yense wamisala, wodziyesa mneneri, kuti umuike iye m'zigologolo ndi m'gori.

27. Ndipo tsopano, walekeranji kumdzudzula Yeremiya wa ku Anatoti, amene amadziyesa mneneri wanu,

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 29