Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 22:22-37 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

22. Koma anapsa mtima Mulungu cifukwa ca kupita iye, ndipo mthenga wa Yehova anadziika m'njira wotsutsana naye, Ndipo anali wokwera pa buru wace, ndi anyamata ace awiri anali naye,

23. Ndipo buruyo anaona mthenga wa Yehova alikuima m'njira, ndi lupanga lace ku dzanja lace; ndi buru anapatuka m'njira, nalowa kuthengo; ndipo Balamu anampanda buru kumbwezera kunjira.

24. Pamenepo mthenga wa Yehova anaima m'njira yopapatiza ya minda yampesa; mbali yina kuli linga, mbali yina linga.

25. Ndipo buru anaona mthenga wa Yehova, nadzikankhira kulinga, nakanikiza phazi la Balamu kulinga; ndipo anampandanso.

26. Pamenepo mthenga wa Yehova anapitiriranso, naima popapatiza, popanda popatukira kulamanja kapena kulamanzere.

27. Ndipo buru wace anaona mthenga wa Yehova, nagona pansi, Balamu ali pamsana pace; ndipo Balamu adapsa mtima, nampanda buru ndi ndodo.

28. Ndipo Yehova anatsegula pakamwa pace pa buru, nati uyu kwa Balamu, Ndakucitanji, kuti wandipanda katatu tsopano?

29. Pamenepo Balamu anati kwa buru, Cifukwa wandipeputsa; mukadakhala lupanga m'dzanja langa tsopano, ndikadakupha iwe.

30. Ndipo buru anati kwa Balamu, Si ndine buru wako amene umayenda wokwera pa ine ciyambire ndiri wako kufikira lero lino? Kodi ndikakucitira cotere ndi kale lonse? Ndipo anati, Iai.

31. Pamenepo Yehova anapenyetsa maso a Balamu, naona iye mthenga wa Yehova alikuima m'njira, lupanga losolola liri kudzanja, ndipo anawerama mutu wace, nagwa nkhope yace pansi.

32. Ndipo mthenga wa Yehova ananena naye, Wapandiranji buru wako katatu tsopano? taona, ndaturuka kuti nditsutsane nawe popeza njira iyi ikugwetsa camtu pamaso panga;

33. koma buru anandiona, nandipatukira nthawi izi zitatu pondiona; akadapanda kundipatukira, ndikadakupha iwe ndithu, ndi kumsunga iye wamoyo.

34. Pamenepo Balamu anati kwa mthenga wa Yehova, Ndacimwa, popeza sindinadziwa kuti munaima mondiletsa m'njira; ndipo tsopano, ngati cikuipirani, ndibwerera.

35. Ndipo mthenga wa Yehova anati kwa Balamu, Pita nao anthuwa; koma mau okha okha ndinena ndi iwe, ndiwo ukanene, Potero Balamu anamuka nao akalonga a Balaki.

36. Pamene Balaki anamva kuti wafika Balamu, anamturukira kukakomana naye ku mudzi wa Moabu, wokhala m'mphepete mwa Arinoni, ndiwo ku malekezero a malire ace.

37. Ndipo Balaki anati kwa Balamu, Kodi sindinatumiza kwa iwe ndithu kukakuitana? Unalekeranji kudza kwa ine? sindikhoza kodi kukucitira ulemu?

Werengani mutu wathunthu Numeri 22