Mitu

  1. 1
  2. 2
  3. 3
  4. 4
  5. 5
  6. 6
  7. 7
  8. 8
  9. 9
  10. 10
  11. 11
  12. 12
  13. 13
  14. 14

Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Hoseya 9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

Cimo la Israyeli ndi zotsatira zace

1. Usakondwera, Israyeli, ndi kusekerera, ngati mitundu ya anthu; pakuti wacita cigololo kuleka Mulungu wako, wakonda mphotho ya cigololo pa dwale la tirigu liri lonse.

2. Dwale ndi coponderamo mphesa sizidzawadyetsa, vinyo watsopano adzamsowa.

3. Sadzakhala m'dziko la Yehova; koma Efraimu adza bwerera kumka ku Aigupto; ndipo adzadya cakudya codetsa m'Asuri.

4. Sadzatsanulira Yehova nsembe zavinyo; sizidzamkomera Iye nsembe zao; zidzakhala kwa iwo ngati mkate wa acisoni; onse akudyako adzadetsedwa; pakuti mkate wao udzakhala wa njala yao, uwu sudzalowa m'nyumbaya Yehova.

5. Mudzacitanji tsiku la masonkhano oikika, ndi tsiku la madyerero a Yehova?

6. Pakuti taonani, anacokera cionongeko, koma Aigupto adzawasonkhanitsa, Mofi adzawaika m'manda; khwisa adzalanda zofunika zao zasiliva; minga idzakhala m'mahema mwao.

7. Masiku a kulanga afika, masiku a kubwezera afika; Israyeli adzadziwa; mneneri ali wopusa, munthu wamzimu ali wamisala, cifukwa ca kucuruka mphulupulu yako, ndi popeza udani ndi waukuru.

8. Efraimu ndiye wozonda kwa Mulungu wanga; kunena za mneneri, msampha wa msodzi uli m'njira zace zonse, ndi udani m'nyumba ya Mulungu wace.

9. Anadzibvunditsa kwambiri, monga masiku a Gibeya; adzakumbukila mphulupulu yao, adzalanga zocimwa zao.

10. Ndinapeza Israyeli ngati mphesa m'cipululu, ndinaona makolo anu ngati cipatso coyamba ca mkuyu nyengo yace yoyamba; koma anadza kwa Baala Peori, nadzipatulira conyansaco, nasandulika onyansa, conga cija anacikonda.

11. Kunena za Efraimu, ulemerero wao udzauluka ndi kucoka ngati mbalame; sipadzakhala kubala, ndi kukhala ndi pakati, ndi kuima.

12. Angakhale alera ana ao, koma ndidzawasowetsa, wosatsala munthu; ndithunso tsoka iwowa, pamene ndiwacokera.

13. Efraimu, monga ndaona, akunga Turo, wookedwa pokoma; koma Efraimu adzaturutsira ana ace wakuwaphera.

14. Apatseni, Yehova; mudzapatsa ciani? muwapatse mimba yotayataya, ndi mawere ouma.

15. Coipa cao conse ciri m'Giligala; pakutipamenepo ndinawada, cifukwa ca kuipa kwa macitidwe ao ndidzawainga kuwacotsa m'nyumba mwanga; sindidzawakondanso; akalonga ao onse ndiwo opanduka.

16. Efraimu wakanthidwa, muzu wao wauma, iwo sadzabala zipatso; inde ngakhale abala, koma ndidzapha zipatso zofunika za mimba yao.

17. Mulungu wanga adzawataya, pakuti sanammvera Iye; ndipo adzakhala othawathawa mwa amitundu.